< Jeremiáš 38 >

1 Slyšel pak Sefatiáš syn Matanův, a Gedaliáš syn Paschurův, a Juchal syn Selemiášův, a Paschur syn Malkiášův slova, kteráž Jeremiáš mluvil ke všemu lidu, řka:
Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
2 Takto praví Hospodin: Kdo by zůstal v městě tomto, zahyne mečem, hladem aneb morem, ale kdož by vyšel k Kaldejským, že bude živ, a že bude míti život svůj místo kořisti, a živ zůstane.
“Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
3 Takto praví Hospodin: Jistotně vydáno bude město toto v ruku vojska krále Babylonského, a vezme je.
Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
4 Protož řekla ta knížata králi: Nechť jest usmrcen muž ten, poněvadž zemdlívá ruce mužů bojovných, pozůstalých v městě tomto, i ruce všeho lidu, mluvě jim slova taková; nebo muž ten nikoli neobmýšlí pokoje lidu tomuto, ale zlé.
Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
5 Tedy řekl král Sedechiáš: Aj, v ruce vaší jest, neboť král zhola nic nemůže proti vám.
Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
6 I vzali Jeremiáše, kterýž byl v síni stráže, a uvrhli jej do jámy Malkiášovy, syna králova, a spustili Jeremiáše po provazích. V té pak jámě nebylo nic vody, ale bláto, tak že Jeremiáš tonul v tom blátě.
Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
7 Ale jakž uslyšel Ebedmelech Mouřenín, dvořan, kterýž byl v domě královském, že dali Jeremiáše do té jámy, (král pak seděl v bráně Beniaminské),
Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
8 Hned vyšel Ebedmelech z domu královského, a mluvil s králem, řka:
Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
9 Pane můj, králi, zle učinili muži tito všecko, což učinili Jeremiášovi proroku, že jej uvrhli do té jámy; neboť by byl umřel i na prvním místě hladem, poněvadž již není žádného chleba v městě.
“Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
10 Protož poručil král Ebedmelechovi Mouřenínu, řka: Vezmi s sebou odsud třidceti mužů, a vytáhni Jeremiáše proroka z té jámy, prvé než by umřel.
Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
11 Tedy vzal Ebedmelech ty muže s sebou, a všel do domu královského pod pokladnici, a nabral starých hadrů strhaných, hadrů, pravím, zkažených, kteréž spustil k Jeremiášovi do té jámy po provazích.
Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
12 A řekl Ebedmelech Mouřenín Jeremiášovi: Nu, podlož ty staré, strhané hadry a zkažené pod paže rukou svých s provazy. I učinil tak Jeremiáš.
Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
13 Takž vytáhli Jeremiáše po provazích, a dobyli jej z té jámy. I seděl Jeremiáš v síni stráže.
ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
14 Potom poslav král Sedechiáš, vzal Jeremiáše proroka k sobě do třetího průchodu, kterýž byl při domu Hospodinovu, a řekl král Jeremiášovi: Zeptám se tebe na něco, netaj přede mnou ničehož.
Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
15 I řekl Jeremiáš Sedechiášovi: Oznámím-liť, zdaliž mne konečně neusmrtíš? A poradím-liť, neuposlechneš mne.
Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
16 Tedy přisáhl král Sedechiáš Jeremiášovi tajně, řka: Živť jest Hospodin, kterýž učinil nám život tento, že tě neusmrtím, aniž tě vydám v ruku mužů těch, kteříž hledají bezživotí tvého.
Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
17 I řekl Jeremiáš Sedechiášovi: Takto praví Hospodin Bůh zástupů, Bůh Izraelský: Jestliže dobrovolně vyjdeš k knížatům krále Babylonského, i duše tvá živa bude, i město toto nebude vypáleno ohněm, a tak živ zůstaneš ty i dům tvůj.
Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
18 Jestliže pak nevyjdeš k knížatům krále Babylonského, jistě že vydáno bude město toto v ruku Kaldejských, a vypálí je ohněm, ano i ty neznikneš ruky jejich.
Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
19 Tedy řekl král Sedechiáš Jeremiášovi: Velmi se bojím Židů, kteříž ustoupili k Kaldejským, aby mne snad nevydali v ruku jejich, i učinili by sobě ze mne posměch.
Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
20 Ale Jeremiáš řekl: Nevydadí. Uposlechni, prosím, hlasu Hospodinova, o kterémž já mluvím tobě, a bude dobře tobě, i duše tvá živa bude.
Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
21 Jestliže pak nebudeš chtíti vyjíti, toto jest slovo to, kteréž mi ukázal Hospodin,
Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
22 Že aj, všecky ženy, kteréž pozůstaly v domě krále Judského, přivedeny budou knížatům krále Babylonského, a samyť říkati budou: Nabádaliť jsou tě, a obdrželi na tobě ti, kteříž tě troštovali pokojem; uvázlyť v bahně nohy tvé, a nazpět obráceny.
Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
23 Všecky také manželky tvé i syny tvé dovedou k Kaldejským, i ty sám neznikneš ruky jejich, ale rukou krále Babylonského jat budeš, a město toto vypálíš ohněm,
“Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
24 Tedy řekl Sedechiáš Jeremiášovi: Žádný ať neví o věcech těchto, abys neumřel.
Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
25 Pakli uslyšíce knížata, že jsem mluvil s tebou, přišli by k tobě, a řekliť by: Oznam medle nám, cos mluvil s králem, netaj před námi, a neusmrtíme tě, a co mluvil s tebou král?
Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
26 Tedy rci jim: Předkládal jsem poníženou a pokornou prosbu svou před krále, aby mne nedal zase voditi do domu Jonatanova, abych tam neumřel.
udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
27 I sešla se všecka knížata k Jeremiášovi, aby se ho tázali. Kterýžto oznámil jim podlé toho všeho, jakž přikázal král. Takž mlčkem odešli od něho, když nebylo slyšeti o té věci.
Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
28 Jeremiáš pak seděl v síni stráže až do toho dne, v němž dobyt jest Jeruzalém, kdežto byl, když dobýván byl Jeruzalém.
Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.

< Jeremiáš 38 >