< Jeremiáš 30 >

1 Slovo, kteréž se stalo k Jeremiášovi od Hospodina, řkoucí:
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Takto praví Hospodin, Bůh Izraelský, řka: Spiš sobě do knihy všecka slova, kterážť jsem mluvil.
“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza.
3 Aj, dnové zajisté jdou, dí Hospodin, přivedu zase zajaté lidu svého Izraelského i Judského, praví Hospodin, a uvedu je do země, kterouž jsem byl dal otcům jejich, a dědičně ji obdrží,
Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
4 Tatoť pak jsou slova, kteráž mluvil Hospodin o Izraelovi a Judovi:
Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda:
5 Takto zajisté praví Hospodin: Hlas předěšení a hrůzy slyšíme, a že není žádného pokoje.
“Yehova akuti: “Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa, ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
6 Ptejte se nyní, a vizte rodívá-li samec. Pročež tedy vidím, an každý muž rukama svýma drží se za bedra svá jako rodička, a obrácené všechněch oblíčeje v zsinalost?
Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti: Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira? Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
7 Ach, nebo veliký jest den tento, tak že nebylo žádného jemu podobného. Ale jakť koli čas jest ssoužení Jákobova, předceť z něho vysvobozen bude.
Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri! Sipadzakhala lina lofanana nalo. Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo, koma adzapulumuka ku masautsowo.”
8 Stane se zajisté v ten den, dí Hospodin zástupů, že polámi jho jeho z šíje tvé, a svazky tvé potrhám, i nebudou ho více v službu podrobovati cizozemci.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo ndipo ndidzadula zingwe zowamanga; Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
9 Ale sloužiti budou Hospodinu Bohu svému, a Davidovi králi svému, kteréhož jim vzbudím.
Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo ndiponso Davide mfumu yawo, amene ndidzawasankhira.
10 Protož ty neboj se, služebníče můj Jákobe, dí Hospodin, aniž se strachuj, ó Izraeli, nebo aj, já vysvobodím tě zdaleka, i símě tvé z země zajetí jejich. I navrátí se Jákob, aby odpočíval, a pokoj měl, a nebude žádného, kdo by jej předěsil.
“‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo; usade nkhawa, iwe Israeli,’ akutero Yehova. ‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali, zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere, ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
11 Neboť já s tebou jsem, dí Hospodin, abych tě vysvobodil, když učiním konec všechněm národům, mezi kteréž tě rozptýlím. Tobě však neučiním konce, ale budu tě trestati v soudu, ačkoli tě bez trestání naprosto nenechám.
Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu kumene ndinakubalalitsirani, koma inu sindidzakuwonongani kotheratu. Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa. Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’”
12 Takto zajisté praví Hospodin: Přetěžké bude potření tvé, přebolestná rána tvá.
Yehova akuti, “Chilonda chanu nʼchosachizika, bala lanu ndi lonyeka.
13 Nebude, kdo by přisoudil při tvou k uléčení; lékařství platného žádného míti nebudeš.
Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu, palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira, palibe mankhwala ochiritsa inu.
14 Všickni, kteříž tě milují, zapomenou se nad tebou, aniž tě navštíví, když tě raním ranou nepřítele, a trestáním přísným pro mnohou nepravost tvou a nesčíslné hříchy tvé.
Abwenzi anu onse akuyiwalani; sasamalanso za inu. Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira. Ndipo ndakulangani mwa nkhanza, chifukwa machimo anu ndi ambiri, ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
15 Proč křičíš nad svým potřením a těžkou bolestí svou? Pro mnohou nepravost tvou a nesčíslné hříchy tvé to činím tobě.
Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu? Bala lanu silingapole ayi. Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
16 A však všickni, kteříž zžírají tebe, sežráni budou, a všickni, kteříž utiskají tebe, všickni, pravím, do zajetí půjdou, a kteříž tě pošlapávají, pošlapáni budou, a všecky, kteříž tě loupí, v loupež vydám,
“Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa; adani anu onse adzapita ku ukapolo. Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso; onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
17 Tehdáž když tobě navrátím zdraví, a na rány tvé zhojím tě, dí Hospodin, proto že zahnanou nazývali tebe, říkajíce: Tato jest Sion, není žádného, kdo by ji navštívil.
Ndidzachiza matenda anu ndi kupoletsa zilonda zanu, akutero Yehova, ‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika. Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’”
18 Takto praví Hospodin: Aj, já zase přivedu zajaté stánků Jákobových, a nad příbytky jeho slituji se, i budeť zase vzděláno město na prvním místě svém, a palác podlé způsobu svého vystaven.
Yehova akuti, “Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo; mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake, nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
19 A bude pocházeti od nich díků činění a hlas veselících se; nebo je rozmnožím, a nebudou umenšení bráti, zvelebím je, a nebudou sníženi.
Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo. Ndidzawachulukitsa, ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika; ndidzawapatsa ulemerero, ndipo sadzanyozedwanso.
20 A budou synové jeho tak jako i prvé, a shromáždění jeho přede mnou utvrzeno bude, trestati pak budu všecky, kteříž jej ssužují.
Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale, ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga; ndidzalanga onse owazunza.
21 A povstane z něho nejdůstojnější jeho, a panovník jeho z prostředku jeho vyjde, kterémuž rozkáži přiblížiti se, aby předstoupil přede mne. Nebo kdo jest ten, ješto by slíbil za sebe, že předstoupí přede mne? dí Hospodin.
Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo. Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo. Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira. Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane popanda kuyitanidwa?” akutero Yehova.
22 I budete mým lidem, a já budu vaším Bohem.
“Choncho inu mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
23 Aj, vicher Hospodinův s prchlivostí vyjde, vicher trvající nad hlavou nešlechetných trvati bude.
Taonani ukali wa Yehova wowomba ngati mphepo ya mkuntho. Mphepo ya namondwe ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
24 Neodvrátíť se prchlivost hněvu Hospodinova, dokudž neučiní toho, a dokudž nevykoná úmyslu srdce svého. Tehdáž porozumíte tomu.
Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka mpaka atakwaniritsa zolinga za mu mtima mwake. Mudzamvetsa zimenezi masiku akubwerawo.

< Jeremiáš 30 >