< Jeremiáš 24 >

1 Ukázal mi Hospodin, a aj, dva košové fíků postaveni byli před chrámem Hospodinovým, když byl přestěhoval Nabuchodonozor král Babylonský Jekoniáše syna Joakimova, krále Judského, a knížata Judská, i tesaře a kováře z Jeruzaléma, a přivedl je do Babylona.
Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
2 Jeden koš byl fíků velmi dobrých, jacíž bývají fíkové ranní, druhý pak koš fíků velmi zlých, jakýchž nelze jísti pro trpkost.
Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
3 Tedy řekl mi Hospodin: Co vidíš, Jeremiáši? I řekl jsem: Fíky, dobré fíky, a to velmi dobré, zlé pak, a to velmi zlé, jichž nelze jísti pro trpkost.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
4 I stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Tsono Yehova anandiwuza kuti,
5 Takto praví Hospodin, Bůh Izraelský: Jako fíkové tito dobří, tak mně příjemní budou zajatí Judští, kteréž jsem zaslal z místa tohoto do země Kaldejské k dobrému.
“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
6 Obrátím zajisté oči své k nim k dobrému, a přivedu je zase do země této, kdežto vzdělám je, a nezkazím, štípím je, a nevypléním.
Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
7 Nebo dám jim srdce, aby znali mne, že já jsem Hospodin. I budou mým lidem, a já budu jejich Bohem, když se obrátí ke mně celým srdcem svým.
Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
8 Naodpor, jako fíky zlé, kterýchž nelze jísti pro trpkost, tak zavrhu (toť zajisté praví Hospodin), Sedechiáše krále Judského s knížaty jeho, a ostatek Jeruzalémských pozůstalých v zemi této, i ty, kteříž bydlí v zemi Egyptské.
“‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
9 Vydám je, pravím, v posmýkání k zlému po všech královstvích země, v pohanění a v přísloví, v rozprávku a v proklínání po všech těch místech, kamž je rozženu.
Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
10 A budu posílati na ně meč, hlad a mor, dokudž by do konce vyhlazeni nebyli z země, kterouž jsem byl dal jim i otcům jejich.
Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”

< Jeremiáš 24 >