< Jeremiáš 12 >

1 Spravedlivý zůstaneš, Hospodine, povedu-li odpor proti tobě, a však o soudech tvých mluviti budu s tebou. Proč se cestě bezbožníků šťastně vede? Mají pokoj všickni, kteříž se pyšně zpronevěřili.
Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
2 Štěpuješ je, ano i vkořeňují se; rostou, ano i ovoce nesou ti, jejichžto úst blízko jsi, ale daleko od ledví jejich.
Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
3 Ale ty, Hospodine, znáš mne, prohlédáš mne, a zkusils srdce mého, že s tebou jest, onyno pak táhneš jako ovce k zabíjení, a připravuješ je ke dni zabití.
Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
4 Dokudž by žalostila země, a bylina všeho pole svadla pro zlost přebývajících v ní, a hynulo každé hovado i ptactvo? Nebo říkají: Nevidíť Bůh skončení našeho.
Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
5 Poněvadž tebe s pěšími běžícího k ustání přivodí, kterakž bys tedy stačil při koních? A poněvadž v zemi pokojné, jíž jsi se dověřil, ustáváš, což pak spravíš při tom zdutém Jordánu?
Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
6 Nebo i bratří tvoji i dům otce tvého zpronevěřili se tobě, a ti také povolávají za tebou plnými ústy. Nevěř jim, byť pak mluvili s tebou přátelsky.
Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
7 Opustil jsem dům svůj, zavrhl jsem dědictví své, dal jsem to, což velice milovala duše má, v ruce nepřátel jeho.
“Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
8 Učiněno jest mi dědictví mé podobné lvu v lese, vydává proti mně hlas svůj, pročež ho nenávidím.
Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
9 A což ptákem dravým jest mi dědictví mé? Což ptactvo vůkol bude proti němu? Jdětež nu, shromažďte se všecka zvířata polní, sejděte se k jídlu.
Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 Mnozí pastýři zkazí vinici mou, pošlapají podíl můj, podíl mně velmi milý obrátí v poušť nejhroznější,
Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
11 Obrátí jej v pustinu. Kvíliti bude, spustošen jsa ode mne; spustne všecka tato země, nebo není žádného, kdo by to v srdci skládal.
Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
12 Na všecka místa vysoká po poušti potáhnou zhoubcové, meč zajisté Hospodinův zžíře od jednoho kraje země až do druhého, nebude míti pokoje žádné tělo.
Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 Nasejí pšenice, ale trní žíti budou; bolestně to ponesou, že užitku nevezmou, a styděti se budou za úrody své pro prchlivost hněvu Hospodinova.
Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
14 Takto praví Hospodin o všech mých sousedech zlých, jenž se dotýkají dědictví, kteréž jsem uvedl v dědictví lidu svému Izraelskému: Aj, já vypléním je z země jejich, když dům Judský vypléním z prostředku jejich.
“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
15 Stane se však, když je vypléním, že se navrátím a smiluji se nad nimi, a přivedu zase jednoho každého z nich k dědictví jeho, a jednoho každého do země jeho.
Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
16 Stane se také, jestliže by se pilně učili cestám lidu mého, a přisahali by ve jménu mém, říkajíce: Živť jest Hospodin, jakž oni učívali lid můj přisahati skrze Bále, že vzděláni budou u prostřed lidu mého.
Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
17 Jestliže by pak neposlouchali, tedy pléniti budu národ ten ustavičně a hubiti, dí Hospodin.
Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

< Jeremiáš 12 >