< Jeremiáš 11 >

1 Slovo, kteréž se stalo k Jeremiášovi od Hospodina, řkoucí:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Slyšte slova smlouvy této, kteráž byste mluvili mužům Judským, a obyvatelům Jeruzalémským,
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 A rci jim: Takto praví Hospodin Bůh Izraelský: Zlořečený ten člověk, kterýž by neposlechl slov smlouvy této,
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 Kterouž jsem vydal otcům vašim tehdáž, když jsem je vyvedl z země Egyptské, z peci železné, řka: Poslouchejte hlasu mého, a čiňte to všecko, tak jakž přikazuji vám, i budete lidem mým, a já budu Bohem vaším,
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 Abych splnil přísahu, kterouž jsem učinil otcům vašim, že jim dám zemi oplývající mlékem a strdí, jakž dnešní den jest. Jemuž odpověděv, řekl jsem: Amen, Hospodine.
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 Potom řekl mi Hospodin: Ohlašuj všecka slova tato po městech Judských, a po ulicích Jeruzalémských, řka: Slyšte slova smlouvy této, a čiňte je.
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 Nebo častokrát osvědčoval jsem se otcům vašim, od toho dne, jakž jsem je vyvedl z země Egyptské, až do dne tohoto; ráno přivstávaje a osvědčuje se, říkával jsem: Poslouchejte hlasu mého.
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 Ale neposlouchali, aniž naklonili ucha svého, nýbrž chodil jeden každý po zdání srdce svého zlého. Pročež uvedl jsem na ně všecka slova smlouvy této, kterouž jsem přikázal plniti, ale neplnili.
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 Tehdy řekl mi Hospodin: Nalézá se spiknutí mezi muži Judskými, a mezi obyvateli Jeruzalémskými.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 Obrátili se k nepravostem otců svých starých, kteříž nechtěli poslouchati slov mých. Tolikéž tito chodí za bohy cizími, sloužíce jim; dům Izraelský a dům Judský zrušili smlouvu mou, kterouž jsem učinil s otci jejich.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 Protož takto praví Hospodin: Aj, já uvedu na ně zlé, z něhož nebudou moci vyjíti. By pak volali ke mně, nevyslyším jich.
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 I půjdou města Judská i obyvatelé Jeruzalémští, a budou volati k bohům těm, kterýmž kadí, ale nikoli nevysvobodí jich v čas bídy jejich,
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 Ačkoli podlé počtu měst máš bohy své, ó Judo, a podlé počtu ulic Jeruzalémských nastavěli jste oltářů ohavnosti té, oltářů, na nichž byste kadili Bálovi.
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 Protož ty nemodl se za lid tento, aniž pozdvihuj za ně hlasu a modlitby; neboť nikoli nevyslyším jich v ten čas, když by volali ke mně příčinou svého zlého.
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 Co jest milému mému do mého domu, poněvadž nestydatě páše nešlechetnosti s mnohými, a oběti svaté odešly od tebe, a že v zlosti své pléšeš?
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 Byltě Hospodin nazval jméno tvé olivou zelenající se, pěknou pro ovoce ušlechtilé, ale s zvukem bouře veliké zapálí ji s hůry, když polámí ratolesti její.
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 Nebo Hospodin zástupů, kterýž tě byl štípil, vyřkl zlé proti tobě, pro nešlechetnost domu Izraelského a domu Judského, kterouž mezi sebou páchali, aby mne popouzeli, kadíce Bálovi.
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 Hospodin zajisté oznámil mi, i dověděl jsem se. Tehdáž jsi mi ukázal předsevzetí jejich,
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 Když jsem já byl jako beránek a volček, kterýž veden bývá k zabití. Nebo nevěděl jsem, by proti mně rady skládali: Zkazme strom s ovocem jeho, a vyhlaďme jej z země živých, aby jméno jeho nebylo připomínáno více.
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 Ale ó Hospodine zástupů, soudce spravedlivý, kterýž zkušuješ ledví i srdce, nechť se podívám na pomstu tvou nad nimi; nebo jsem tobě zjevil při svou.
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 Protož takto praví Hospodin o Anatotských, kteříž hledají bezživotí tvého, říkajíce: Neprorokuj ve jménu Hospodinovu, abys neumřel v ruce naší:
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 Protož takto praví Hospodin zástupů: Aj, já navštívím je. Mládenci zbiti budou mečem, synové jejich i dcery jejich zemrou hladem,
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 A nebudou míti potomků, když uvedu zlé na Anatotské, času toho, v němž je navštívím.
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”

< Jeremiáš 11 >