< Izaiáš 54 >

1 Prozpěvuj, neplodná, kteráž nerodíš, zvučně prozpěvuj a prokřikni, kteráž ku porodu nepracuješ, nebo více bude synů opuštěné, nežli synů té, kteráž má muže, praví Hospodin.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Rozšiř místo stanu svého, a čalounů příbytků svých roztáhnouti nezbraňuj; natáhni i provazů svých, a kolíky své utvrď.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 Nebo na pravo i na levo se rozmůžeš, a símě tvé národy dědičně vládnouti bude, a města pustá osadí.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 Nebojž se, nebo nebudeš zahanbena, aniž se zapyřuj, nebo nebudeš v potupu uvedena; nýbrž na potupu mladosti své zapomeneš, a na pohanění vdovství svého nezpomeneš více.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 Nebo manželem tvým jest Učinitel tvůj, jehož jméno Hospodin zástupů, a vykupitel tvůj Svatý Izraelský Bohem vší země slouti bude.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 Nebo jako ženy propuštěné a v duchu sevřené povolá tě Hospodin, a jako ženy mladice, když v pohrdnutí budeš, praví Bůh tvůj.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 Na maličkou chvilku poopustil jsem tě, ale v slitování převelikém shromáždím tě.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 V maličkém hněvě skryl jsem tvář svou na maličko před tebou, ale v milosrdenství věčném slituji se nad tebou, praví vykupitel tvůj Hospodin.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 Neboť jest to u mne, co při potopě Noé. Jakož jsem přisáhl, že se nebudou více rozlévati vody Noé po zemi, tak jsem přisáhl, že se nerozhněvám na tě, aniž tobě přísně domlouvati budu.
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 A byť se i hory pohybovaly, a pahrbkové ustupovali, milosrdenství mé však od tebe neodstoupí, a smlouva pokoje mého se nepohne, praví slitovník tvůj Hospodin.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 Ó ssoužená, vichřicí zmítaná, potěšení zbavená, aj, já položím na karbunkulích kamení tvé, a založím tě na zafiřích.
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 A vzdělám z křištálu skla tvá, a brány tvé z kamení třpytícího se, i všecka pomezí tvá z kamení drahého.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 Synové pak tvoji všickni vyučení budou od Hospodina, a hojnost pokoje budou míti synové tvoji.
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Na spravedlnosti upevněna budeš. Vzdálíš se od ssoužení, protož se ho nebudeš báti, a od setření, nebo nepřiblíží se k tobě.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Aj, budouť nejedni bydliti s tebou, kteříž nejsou moji, ale kdož by bydleje s tebou, byl proti tobě, padne.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Aj, já stvořil jsem kováře dýmajícího při ohni na uhlí, a vynášejícího nádobí k dílu svému, já také stvořil jsem zhoubce, aby hubil.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 Žádný nástroj proti tobě udělaný nepodaří se, a každý jazyk, povstávající proti tobě na soudu, potupíš. Toť jest dědictví služebníků Hospodinových, a spravedlnost jejich ode mne, praví Hospodin.
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.

< Izaiáš 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark