< Izaiáš 52 >

1 Probuď se, probuď se, oblec se v sílu svou, Sione, oblec se v roucho okrasy své, ó Jeruzaléme, město svaté; neboť nebude již více na tě dotírati neobřezaný a nečistý.
Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
2 Otřes se z prachu, povstaň, posaď se, Jeruzaléme; dobuď se z okovů hrdla svého, ó jatá dcerko Sionská.
Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
3 Takto zajisté dí Hospodin: Darmo jste sebe prodali, protož bez peněz budete vykoupeni.
Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
4 Nebo takto praví Panovník Hospodin: Do Egypta sstoupil lid můj předešle, aby tam byl pohostinu, ale Assur bez příčiny jej ssužuje.
Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
5 Nyní tedy což mám činiti? praví Hospodin. Poněvadž jest lid můj zajat darmo, a panovníci jeho k úpění jej přivodí, praví Hospodin. Nad to ustavičně každého dne jménu mému útržka se činí.
Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
6 Protož poznáť lid můj jméno mé, protož poznáť, pravím, v ten den, že já tentýž, kterýž mluvím, aj, přítomen budu.
Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
7 Ó jak krásné na horách nohy toho, ješto potěšené věci zvěstuje, a ohlašuje pokoj, toho, ješto zvěstuje dobré, ješto káže spasení, a mluví k Sionu: Kralujeť Bůh tvůj.
Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
8 Strážní tvoji hlasu, hlasu pozdvihnou, a spolu prokřikovati budou; neboť okem v oko uzří, že Hospodin zase přivede Sion.
Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
9 Zvučte, prozpěvujte spolu pustiny Jeruzalémské; neboť jest potěšil Hospodin lidu svého, vykoupil Jeruzalém.
Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
10 Ohrnul Hospodin rámě svatosti své před očima všech národů, aby viděly všecky končiny země spasení Boha našeho.
Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
11 Odejděte, odejděte, vyjděte z Babylona, nečistého se nedotýkejte; vyjděte z prostředku jeho, očisťte se vy, kteříž nosíte nádobí Hospodinovo.
Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
12 Nebo ne s chvátáním vyjdete, aniž s utíkáním půjdete; předcházeti zajisté bude vás Hospodin, a zbéře vás Bůh Izraelský.
Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
13 Aj, služebníku mému šťastně se povede, vyvýšen, vznešen a zveleben bude velmi.
Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
14 A jakož mnozí se nad ním užasnou, že tak zohavena jest nad jiné lidi osoba jeho, způsob jeho nad syny lidské:
Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
15 Tak zase skropí národy mnohé, i králové před ním zacpají ústa svá, proto že což jim nebylo vypravováno, to uzří, a tomu, o čemž neslýchali, porozumějí.
Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.

< Izaiáš 52 >