< Izaiáš 43 >

1 Ale nyní takto praví Hospodin stvořitel tvůj, ó Jákobe, a učinitel tvůj, ó Izraeli: Neboj se, nebo vykoupil jsem tě, a povolal jsem tě jménem tvým. Můj jsi ty.
Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
2 Když půjdeš přes vody, s tebou budu, pakli přes řeky, nepřikvačí tě; půjdeš-li přes oheň, nespálíš se, aniž plamen chytí se tebe.
Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
3 Nebo já Hospodin Bůh tvůj, Svatý Izraelský, jsem spasitel tvůj. Dal jsem na výplatu za tebe Egypt, zemi Mouřenínskou a Sábu místo tebe.
Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
4 Hned jakž jsi drahým učiněn před očima mýma, zveleben jsi, a já jsem tě miloval; protož dal jsem lidi za tebe, a národy za život tvůj.
Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
5 Nebojž se, nebo já s tebou jsem. Od východu zase přivedu símě tvé, a od západu shromáždím tě.
Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
6 Dím půlnoční straně: Navrať, a polední: Nezbraňuj. Přiveď zase syny mé zdaleka, a dcery mé od končin země,
Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
7 Každého toho, jenž se nazývá jménem mým, a kteréhož jsem k slávě své stvořil, jejž jsem sformoval, a kteréhož jsem učinil.
onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
8 Vyveď lid slepý, kterýž již má oči, a hluché, kteříž již mají uši.
Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
9 Všickni národové nechať se spolu shromáždí, a sberou se lidé. Kdo jest mezi nimi, ješto by to zvěstoval, a to, což se předně státi má, aby oznámil nám? Nechť vystaví svědky své, a spravedlivi budou, aneb ať slyší, a řeknou: Pravdať jest.
Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
10 Vy svědkové moji jste, praví Hospodin, a služebník můj, kteréhož jsem vyvolil, tak že můžete věděti, a mně věřiti, i rozuměti, že já jsem, a že přede mnou nebyl sformován Bůh silný, aniž po mně bude.
Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
11 Já, já jsem Hospodin, a žádného není kromě mne spasitele.
Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
12 Já oznamuji, i vysvobozuji, jakž předpovídám, a ne někdo mezi vámi z cizích bohů, a vy mi toho svědkové jste, praví Hospodin, že já Bůh silný jsem.
Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
13 Ještě prvé nežli den byl, já jsem, a není žádného, kdož by vytrhl z ruky mé. Když co dělám, kdo ji odvrátí?
“Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
14 Takto praví Hospodin vykupitel váš, Svatý Izraelský: Pro vás pošli do Babylona, a sházím závory všecky, i Kaldejské s lodimi veselými jejich.
Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
15 Já jsem Hospodin svatý váš, stvořitel Izraele, král váš.
Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
16 Takto praví Hospodin, kterýž způsobuje na moři cestu, a na prudkých vodách stezku,
Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
17 Kterýž vyvodí vozy a koně, vojsko i sílu, činí, že v náhle padají, až i povstati nemohou, hasnou, jako knot hasne:
Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
18 Nezpomínejte na první věci, a na starodávní se neohlédejte.
“Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
19 Aj, já učiním věc novou, a tudíž se zjeví. Zdaliž o tom nezvíte? Nadto způsobím na poušti cestu, a na pustinách řeky.
Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
20 I slaviti mne bude zvěř polní, drakové i sovy, že jsem vyvedl na poušti vody a řeky na pustinách, abych dal nápoj lidu svému, vyvolenému svému.
Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
21 Lid, kterýž nastrojím sobě, chválu mou vypravovati bude,
Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
22 Poněvadž jsi mne nevzýval, ó Jákobe, nýbrž steskloť se se mnou, ó Izraeli.
“Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
23 Nepřivedl jsi mi hovádka k zápalům svým, a obětmi svými neuctils mne; nenutil jsem tě, abys mi sloužil obětmi suchými, aniž jsem tě tím obtěžoval, abys mi kadil.
Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
24 Nekoupil jsi mi za peníze vonných věcí, ani tukem obětí svých zavlažil jsi mne, ale zaměstknal jsi mne hříchy svými, a obtížils mne nepravostmi svými.
Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
25 Já, já sám shlazuji přestoupení tvá pro sebe, a na hříchy tvé nezpomínám.
“Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
26 Přiveď mi ku paměti, suďme se spolu; oznam ty, podlé čeho bys mohl spravedliv býti.
Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
27 Otec tvůj první zhřešil, a učitelé tvoji přestoupili proti mně.
Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
28 A protož smeci knížata z míst svatých, a vydám v prokletí Jákoba, a Izraele v pohanění.
Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

< Izaiáš 43 >