< Izaiáš 40 >

1 Potěšujte, potěšujte lidu mého, dí Bůh váš.
Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
2 Mluvte k srdci Jeruzaléma, a ohlašujte jemu, že se již doplnil čas uložený jeho, že jest odpuštěna nepravost jeho, a že vzal z ruky Hospodinovy dvojnásobně za všecky hříchy své.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
3 Hlas volajícího: Připravtež na poušti cestu Hospodinovu, přímou učiňte na pustině stezku Boha našeho.
Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
4 Každé údolí ať jest vyvýšeno, a všeliká hora i pahrbek ať jest snížen; což jest křivého, ať jest přímé, a místa nerovná ať jsou rovinou.
Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
5 Nebo se zjeví sláva Hospodinova, a uzří všeliké tělo spolu, že ústa Hospodinova mluvila.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
6 Hlas řkoucího: Volej. I řekl: Co mám volati? To, že všeliké tělo jest tráva, a všeliká vzácnost jeho jako květ polní.
Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
7 Usychá tráva, květ prší, jakž vítr Hospodinův povane na něj. V pravděť jsou lidé ta tráva.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
8 Usychá tráva, květ prší, ale slovo Boha našeho zůstává na věky.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
9 Na horu vysokou vystup sobě, Sione, zvěstovateli věcí potěšených, povyš mocně hlasu svého, Jeruzaléme, zvěstovateli věcí potěšených, povyš, aniž se boj. Rci městům Judským: Aj, Bůh váš.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
10 Aj, Panovník Hospodin proti silnému přijde, a rámě jeho panovati bude nad ním; aj, mzda jeho s ním, a dílo jeho před ním.
Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 Jako pastýř stádo své pásti bude, do náručí svého shromáždí jehňátka, a v klíně svém je ponese, březí pak poznenáhlu povede.
Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
12 Kdo změřil hrstí svou vody, a nebesa pídí rozměřil? A kdo změřil měrou prach země, a zvážil na váze hory, a pahrbky na závaží?
Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Kdo vystihl ducha Hospodinova, a rádcím jeho byl, že by mu oznámil?
Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 S kým se radil, že by mu přidal srozumění, a naučil jej stezce soudu, a vyučil jej umění, a cestu všelijaké rozumnosti jemu v známost uvedl?
Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
15 Aj, národové jako krůpě od okova, a jako prášek na vážkách se počítají, ostrovy jako nejmenší věc zachvacuje.
Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 Ani Libán nepostačil by k zanícení ohně, a živočichové jeho nepostačili by k zápalné oběti.
Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 Všickni národové jsou jako nic před ním, za nic a za marnost pokládají se u něho.
Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
18 K komu tedy připodobníte Boha silného? A jaké podobenství přirovnáte jemu?
Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 Jakžkoli rytinu líčí řemeslník, a zlatník zlatem ji potahuje, a řetízky stříbrné k ní slévá;
Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
20 A ten, kterýž pro chudobu nemá co obětovati, dřevo, kteréž by nepráchnivělo, vybírá, a řemeslníka umělého sobě hledá k přistrojení rytiny, aby se nepohnula.
Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
21 Zdaliž nevíte? Zdaliž neslýcháte? Zdaliž se vám nezvěstuje od počátku? Zdaliž nesrozumíváte z základů země?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 Ten, kterýž sedí nad okršlkem země, jejížto obyvatelé jako kobylky, kterýž rozprostřel jako kortýnu nebesa, a roztáhl je jako stánek k přebývání,
Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 Onť přivodí knížata na nic, soudce zemské jako nic rozptyluje,
Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 Tak že nebývají štípeni ani sáti, aniž kořene pouští do země pařez jejich. Nebo jakž jen zavane na ně, hned usychají, a vicher jako plevu zanáší je.
Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
25 K komu tedy připodobníte mne, abych podobný byl jemu, praví Svatý?
Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Pozdvihněte zhůru očí svých, a vizte, kdo to stvořil? Kdo vyvodí v počtu vojsko jejich, a všeho toho zejména povolává? Vedlé množství síly a veliké moci ani jedno z nich nehyne.
Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
27 Pročež tedy říkáš, Jákobe, a mluvíš, Izraeli: Skrytať jest cesta má před Hospodinem, a pře má před Boha mého nepřichází?
Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Zdaliž nevíš, zdaž jsi neslýchal, že Bůh věčný Hospodin, kterýž stvořil končiny země, neustává ani zemdlívá, a že vystižena býti nemůže moudrost jeho?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 On dává ustalému sílu, a tomu, ješto žádné síly nemá, moci hojně udílí.
Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Ustává a umdlévá mládež, a mládenci těžce klesají,
Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 Ale ti, jenž očekávají na Hospodina, nabývají nové síly. Vznášejí se peřím jako orlice; běží, a však neumdlévají, chodí, a neustávají.
koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.

< Izaiáš 40 >