< Izaiáš 34 >

1 Přistuptež národové, abyste slyšeli, a lidé pozorujte. Nechať slyší země i plnost její, okršlek zemský i všeliký plod jeho.
Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
2 Proto že hněv Hospodinův jest proti všechněm národům, a prchlivost proti všemu vojsku jejich: vyhubí je jako proklaté, a vydá je k zabití.
Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
3 I budou povrženi zbití jejich, a z těl mrtvých jejich vzejde smrad, a rozplynou se hory od krve jejich.
Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
4 Chřadnouti bude i všecko vojsko nebeské, a svinuta budou nebesa jako kniha, a všecko vojsko jejich sprchne, jako prší list s vinného kmene, a jako nezralé ovoce s fíku.
Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
5 Nebo opojen jest na nebi meč můj; na Idumejské sstoupí, a na lid, na nějž jsem klatbu vydal, aby trestán byl.
Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
6 Meč Hospodinův bude plný krve, umastí se tukem a krví beranů a kozlů, tukem ledvin skopových; obět zajisté bude míti Hospodin v Bozra, a zabijení veliké v zemi Idumejské.
Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
7 Sstoupí s nimi i jednorožcové a volčata s voly, i opije se země jejich krví, a prach jejich tukem se omastí.
Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
8 Nebo den pomsty Hospodinovy, léto odplacování se, aby mštěno bylo Siona.
Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
9 A obráceni budou potokové její v smolu, a prach její v siru, a země její obrátí se v smolu hořící.
Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 V noci ani ve dne neuhasne, na věky vystupovati bude dým její, od národu až do pronárodu pustá zůstane, na věky věků nebude, kdo by šel přes ni.
Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Ale osednou ji pelikán a výr, kalous také a krkavec budou bydliti v ní, a roztáhne po ní šňůru zahanbení a závaží marnosti.
Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Šlechticů jejích volati budou k království, ale nebude tam žádného, nebo všecka knížata její zhynou.
Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 A vzroste na palácích jejích trní, kopřivy a bodláčí na hradích jejích, a bude příbytkem draků a obydlím sov.
Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
14 Tam se budou potkávati spolu zvěř s ptactvem, a příšera jedna druhé se ozývati; tam toliko noční přeluda se usadí, a odpočinutí sobě nalezne.
Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
15 Tam se zhnízdí sup, a škřečeti bude, a když vysedí, shromáždí je pod stín svůj; tam také shledají se luňáci jeden s druhým.
Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
16 Hledejte v knize Hospodinově, a čtěte. Ani jedno z těch nechybí, a jeden každý bez své druže nebude; nebo to ústa Páně přikázala, a duch jeho shromáždí je.
Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Onť zajisté vrže jim losy, a ruka jeho jim rozdělí ji provazcem; až na věky dědičně ji osednou, od národu až do pronárodu v ní přebývati budou.
Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

< Izaiáš 34 >