< Izaiáš 18 >

1 Běda zemi zastěňující se křídly, kteráž jest při řekách země Mouřenínské,
Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 Posílající po moři posly, v nástrojích z sítí po vodách, řka: Jděte, poslové rychlí, k národu rozptýlenému a zloupenému, k lidu hroznému zdávna i posavad, k národu všelijak potlačenému, jehož zemi řeky roztrhaly.
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Všickni obyvatelé světa, a přebývající na zemi, když bude korouhev vyzdvižena na horách, uzříte, a když troubiti se bude trubou, uslyšíte.
Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
4 Nebo takto praví Hospodin ke mně: Spokojímť se, a podívám z příbytku svého, a budu jako teplo vysušující po dešti, a jako oblak dešťový v čas horké žně.
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 Před vinobraním zajisté, když se vypučí pupenec, a květ vydá hrozen trpký, ještě rostoucí, tedy podřeže révíčko noži, a rozvody odejme a zpodtíná.
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 I budou zanecháni všickni spolu ptactvu z hor, a šelmám zemským, a bude na nich přes léto ptactvo, a všeliké šelmy zemské na nich přes zimu zůstanou.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 V ten čas přinesen bude dar Hospodinu zástupů (od lidu rozptýleného a zloupeného, od lidu hrozného zdávna i posavad, národu všelijak potlačeného, jehožto zemi řeky rozchvátaly), k místu jména Hospodina zástupů, hoře Sion.
Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.

< Izaiáš 18 >