< Izaiáš 17 >

1 Břímě Damašku. Aj, Damašek přestane býti městem, a bude hromadou rumu.
Uthenga wonena za Damasiko: “Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda, koma udzasanduka bwinja.
2 Zpuštěná města Aroer pro stáda budou, a odpočívati tam budou, a nebude žádného, kdo by je strašil.
Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi popanda wina woziopseza.
3 I bude odjata pevnost od Efraima, a království od Damašku i ostatků Syrských; jako i sláva synů Izraelských na nic přijdou, praví Hospodin zástupů.
Ku Efereimu sikudzakhalanso linga, ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu; Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu monga anthu a ku Israeli,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 I bude v ten den, že opadne sláva Jákobova, a tuk těla jeho vymizí.
“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira; ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
5 Nebo bude Assur jako ten, jenž shromažďuje ve žni obilé, a rámě jeho žne klasy, anobrž bude jako ten, jenž zbírá klasy v údolí Refaim.
Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu umene anatsiriza kukolola. Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
6 Paběrkové však zanecháni v něm budou, jako po očesání olivy dvě neb tři olivky na vrchu větve, a čtyry neb pět na ratolestech jejích plodistvých, praví Hospodin Bůh Izraelský.
Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,” akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.
7 V ten den patřiti bude člověk k Učiniteli svému, a oči jeho k Svatému Izraelskému hleděti budou.
Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
8 A nebude patřiti k oltářům, dílu rukou svých; ani k tomu, což učinili prstové jeho, hleděti bude, ani k hájům, ani k obrazům slunečným.
Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe, ntchito ya manja awo, ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera, ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.
9 V ten den budou města síly jeho opuštěna jako chrastinka a růžťka, kteráž opuštěna budou od synů Izraelských, i spustneš, ó země.
Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.
10 Nebos se zapomněla na Boha spasení svého, a na skálu síly své nezpomenulas. Protož ačkoli štěpy rozkošné štěpuješ, a kmen vinný přespolní sázíš,
Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu; simunakumbukire Thanthwe, linga lanu. Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino, ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
11 V čas štěpování tvého štípí, aby rostlo, opatruješ, nýbrž téhož jitra o to, což seješ, aby se pučilo, pečuješ: v den však užitku odejde žeň, na žalost tvou přetěžkou.
nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo ndi kuphukira maluwa mmawa mwake, komabe zimenezi sizidzakupindulirani pa tsiku la mavuto.
12 Běda množství lidí mnohých, kteříž jako zvuk mořský ječí, a hlučícím národům, kteříž jako zvuk vod násilných hlučí,
Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri, akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja! Aa, phokoso la anthu a mitundu ina, akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
13 Národům jako zvuk vod mnohých zvučícím; nebo je Bůh okřikne. Pročež daleko utíkati budou, a honěni budou jako plevy po vrších od větru, a jako chumel od vichřice.
Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri, koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula. Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri, ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
14 Nebo u večer aj, předěšení, a než jitro přijde, anť ho není. Tenť jest podíl těch, kteříž nás potlačují, a los těch, kteříž nás loupí.
Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika, ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa. Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu, gawo la amene amatibera zinthu zathu.

< Izaiáš 17 >