< Izaiáš 10 >

1 Běda těm, kteříž ustanovují práva nepravá, a spisovatelům, kteříž těžkosti spisují,
Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
2 Aby odstrkovali nuzné od soudu, a vydírali spravedlnost chudých lidu mého, vdovy aby byly kořist jejich, a sirotky aby loupili.
kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
3 I což učiníte v den navštívení a zpuštění, kteréž zdaleka přijde? K komu se o pomoc utečete? A kde zanecháte slávy své,
Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
4 By nemusila skloniti se mezi vězni, a mezi zbitými klesnouti? Ve všem tom neodvrátí se prchlivost jeho, ale předce ruka jeho bude vztažená.
Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
5 Běda Assurovi, metle hněvu mého, ačkoli hůl rozhněvání mého jest v rukou jeho,
“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
6 A na národ ošemetný pošli jej, a o lidu hněvu mého přikáži jemu, aby směle bral kořisti, a loupil bez milosti, a položil jej v pošlapání jako bláto na ulicích.
Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
7 Ale on ne tak se bude domnívati, ani srdce jeho tak mysliti bude; nebo srdce jeho jest hubiti a pléniti národy mnohé.
Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
8 Nebo řekne: Zdaliž knížata má nejsou také i králové?
Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
9 Zdaliž jako Charkemis není Chalno? Zdali není jako Arfad Emat? Zdali není jako Damašek Samaří?
‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
10 Jakož nalezla ruka má království bohů, ješto rytiny jejich byly nad Jeruzalémských a Samařských,
Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
11 Zdaliž jako jsem učinil Samaří a modlám jeho, tak neučiním Jeruzalému a obrazům jeho?
nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
12 I staneť se, když dokoná Pán všecko dílo své na hoře Sion a v Jeruzalémě, že navštívím ovoce pyšného srdce krále Assyrského, a nádhernost vysokých očí jeho.
Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
13 Nebo řekne: V síle ruky své to jsem vykonal, a v moudrosti své; nebo jsem rozumný byl, a odjal jsem meze národů, a poklady jejich jsem vzebral, a strhl jsem dolů, jako mocný, obyvatele.
Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
14 Anobrž jako hnízdo nalezla ruka má zboží národů, a jako zbírána bývají vejce opuštěná, tak všecku zemi já jsem sebral, aniž byl, kdo by křídlem hnul, aneb otevřel ústa a siptěl.
Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
15 Zdaliž se bude sekera velebiti nad toho, kdož ní seká? Zdaliž se honositi bude pila nad toho, kdož ní tře? Jako by se zpínala metla proti tomu, kdož by ji zdvihl; jako by se chlubila hůl, že není dřevem.
Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
16 Protož pošle Pán, Hospodin zástupů, na vytylé jeho vyzáblost, a po zpodku slávu jeho prudce zapálí, jako silný oheň.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
17 Nebo světlo Izraelovo bude ohněm, a Svatý jeho plamenem, i spálí a sžíře trní i bodláčí jeho jednoho dne.
Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
18 Též spanilost lesu jeho, i úrodných polí jeho, od duše až do těla, všecko vyhubí. I stane se, že předěšený jsa, bude utíkati.
Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
19 A pozůstalého dříví lesu jeho malý počet bude, tak že by je mohlo dítě popsati.
Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
20 I stane se v ten den, nebudou více ostatkové Izraelští a pozůstalí z domu Jákobova zpoléhati na toho, kdož je tepe, ale zpoléhati budou na Hospodina, Svatého Izraelského v pravdě.
Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
21 Ostatkové obrátí se, ostatkové Jákobovi k Bohu silnému, reku udatnému.
Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
22 Nebo byť bylo lidu tvého, Izraeli, jako písku mořského, ostatkové jeho obrátí se. Pohubení uložené rozhojní spravedlnost.
Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
23 Pohubení, pravím, a to jisté, Pán, Hospodin zástupů, učiní u prostřed vší této země.
Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
24 Protož takto praví Pán, Hospodin zástupů: Neboj se Assyrského, lide můj, kterýž přebýváš na Sionu. Prutem umrská tě, a holí svou opřáhne na tebe na cestě Egyptské.
Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
25 Po maličkém zajisté času dokoná se hněv a prchlivost má k vyhlazení jich.
Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
26 Nebo vzbudí na něj Hospodin zástupů bič, jako porážku Madianských na skále Goréb, a jakož pozdvihl holi své na moře, tak jí pozdvihne na něj, na cestě Egyptské.
Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
27 I stane se v ten den, že složeno bude břímě jeho s ramene tvého, a jho jeho s šíje tvé, nýbrž zkaženo bude jho od přítomnosti pomazaného.
Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
28 Přitáhne do Aiat, přejde přes Migron, v Michmas složí nádobí svá.
Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
29 Projdou průchod, v Gabaa budou míti hospodu k přenocování; ulekne se Ráma, Gabaa Saulovo uteče.
Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
30 Naříkej hlasem svým, město Gallim, ať se slyší v Lais: Ach, ubohá Anatot.
Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
31 Pohne se Madmena, obyvatelé Gábim schopí se.
Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
32 Ještě téhož dne zastavě se v Nobe, pohrozí rukou svou hoře dcery Sionské, pahrbku Jeruzalémskému.
Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
33 Aj, Panovník Hospodin zástupů oklestí vší silou ratolesti, ty pak, kteříž jsou vysokého zrostu, podetne; i budou vysocí sníženi.
Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
34 Vyseká též houšť lesů sekerou, i Libán od velikomocného padne.
Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.

< Izaiáš 10 >