< Ezdráš 8 >

1 Tito jsou pak přednější po čeledech svých otcovských, a rod těch, kteříž vyšli se mnou za kralování Artaxerxa krále z Babylona:
Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
2 Z synů Fínesových Gersom, z synů Itamarových Daniel, z synů Davidových Chattus.
Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
3 Z synů Sechaniášových, jenž byl z synů Farosových, Zachariáš, a s ním počet mužů sto a padesáte.
mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
4 Z synů Pachat Moábových Eliehoenai syn Zerachiášův, a s ním dvě stě mužů.
Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
5 Z synů Sechaniášových syn Jachazielův, a s ním tři sta mužů.
Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
6 Z synů Adinových Ebed syn Jonatanův, a s ním padesát mužů.
Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
7 Z synů pak Elamových Izaiáš syn Ataliášův, a s ním sedmdesát mužů.
Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
8 Z synů Sefatiášových Zebadiáš syn Michaelův, a s ním osmdesáte mužů.
Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
9 Z synů Joábových Abdiáš syn Jechielův, a s ním dvě stě a osmnácte mužů.
Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
10 Z synů Selomitových syn Josifiášův, a s ním sto a šedesáte mužů.
Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
11 Z synů Bebai Zachariáš syn Bebai, a s ním osmmecítma mužů.
Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
12 Z synů Azgadových Jochanan syn Hakatanův, a s ním sto a deset mužů.
Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
13 Z synů Adonikamových poslednějších, jichž jména jsou tato: Elifelet, Jehiel, Semaiáš, a s ním šedesáte mužů.
Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
14 Z synů Bigvai Utai a Zabbud, a s nimi sedmdesáte mužů.
Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
15 Shromáždil jsem je pak u potoku, kterýž vpadá do Ahavy, a leželi jsme tu tři dni. Potom přehlédal jsem lid a kněží, a z synů Léví nenašel jsem tu žádného.
Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
16 Protož poslal jsem Eliezera, Ariele, Semaiáše, Elnatana, Jariba, Elnatana, Nátana, Zachariáše a Mesullama, přednější, a Joiariba a Elnatana, muže učené,
Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
17 A rozkázal jsem jim k Iddovi, knížeti v Chasifia místě, a naučil sem je, jak by měli mluviti k Iddovi, Achivovi a Netinejským v Chasifia místě, aby nám přivedli služebníky domu Boha našeho.
ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
18 I přivedli nám s pomocí Boží muže rozumného z synů Moholi, syna Léví, syna Izraelova, a Serebiáše s syny jeho, a bratří jeho osmnácte,
Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
19 A Chasabiáše, a s ním Izaiáše z synů Merari, bratří jeho a synů jejich dvadceti.
Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
20 Z Netinejských pak, kteréž byl zřídil David a knížata k službě Levítům, dvě stě a dvadceti Netinejských. A ti všickni ze jména vyčteni byli.
Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
21 Tedy vyhlásil jsem tu půst u řeky Ahava, abychom se ponižovali před Bohem svým, a hledali od něho cesty přímé sobě a dítkám svým, i všemu jmění našemu.
Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
22 Nebo styděl jsem se žádati od krále vojska a jízdných, aby nás bránili před nepřátely na cestě; nebo jsme byli pravili králi, řkouce: Ruka Boha našeho jest nade všemi, kteříž ho hledají upřímě, ale moc a prchlivost jeho proti všechněm, kteříž ho opouštějí.
Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
23 A když jsme se postili a hledali v tom Boha svého, tedy vyslyšel nás.
Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
24 Oddělil jsem pak přednějších kněží dvanácte: Serebiáše, Chasabiáše, a s nimi z bratří jejich deset.
Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
25 I odvážil jsem jim stříbro a zlato, a to nádobí, obět domu Boha našeho, kterouž obětovali král i rady jeho, i knížata jeho a všecken lid Izraelský, což se ho našlo.
ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
26 Odvážil jsem, pravím, do rukou jejich stříbra šest set centnéřů a padesát, a nádobí stříbrného sto centnéřů, a zlata sto centnéřů,
Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
27 A koflíků zlatých dvadceti, každý v tisíc drachem, a dvě nádoby z mosazi nejlepší, tak vzácné jako zlato.
mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
28 Potom jsem jim řekl: Vy jste posvěceni Hospodinu, i tyto nádoby posvěceny jsou, a to stříbro i zlato jest obět dobrovolná Hospodinu Bohu otců vašich.
Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
29 Pilni toho buďte a ostříhejte, až to i odvážíte před kněžími přednějšími a Levíty, i předními z čeledí otcovských z Izraele v Jeruzalémě v pokojích domu Hospodinova.
Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
30 A tak přijali kněží a Levítové váhu stříbra, zlata a nádobí, aby donesli do Jeruzaléma, do domu Boha našeho.
Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
31 Zatím hnuli jsme se od řeky Ahava, dvanáctého dne měsíce prvního, abychom se brali do Jeruzaléma, a ruka Boha našeho byla s námi, a vytrhla nás z ruky nepřátel a úkladníků na cestě.
Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
32 I přišli jsme do Jeruzaléma, a pobyli jsme tu tři dni.
Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
33 Ètvrtého pak dne odváženo jest stříbro a zlato, a nádobí to v domě Boha našeho k ruce Meremota syna Uriáše kněze, s nímž byl Eleazar syn Fínesův, a pomocníci jejich Jozabad syn Jesua, a Noadiáš syn Binnui, Levítové,
Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
34 Vše v počtu a váze, a zapsána jest všecka ta váha toho času.
Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
35 Vrátivše se pak z zajetí ti, kteříž byli přestěhováni, obětovali zápaly Bohu Izraelskému, volků dvanáct za všecken lid Izraelský, skopců devadesát a šest, beránků sedmdesát a sedm, kozlů za hřích dvanáct, vše v obět zápalnou Hospodinu.
Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
36 I dali výpovědi královy vládařům královským i vývodám za řekou. Kteříž pomocni byli lidu i domu Božímu.
Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.

< Ezdráš 8 >