< Ezechiel 9 >

1 Potom zavolal hlasem velikým, tak že jsem slyšel, řka: Přistupte hejtmané k tomuto městu, a jeden každý s zbrojí svou hubící v ruce své.
Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
2 A aj, šest mužů přišlo cestou k bráně hořejší, kteráž patří na půlnoci, maje každý zbroj svou rozrážející v ruce své. Muž pak jeden byl u prostřed nich, oděný rouchem lněným, a kalamář písařský při bedrách jeho; a přišedše, stáli u oltáře měděného.
Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
3 Sláva pak Boha Izraelského sstoupila byla s cherubína, na kterémž byla, k prahu domu, a zvolala na muže toho oděného rouchem lněným, při jehož bedrách byl kalamář písařský.
Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
4 I řekl jemu Hospodin: Přejdi prostředkem města, prostředkem Jeruzaléma, a znamenej znamením na čelích muže ty, kteříž vzdychají a naříkají nade všemi ohavnostmi dějícími se u prostřed něho.
ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
5 Oněmno pak řekl tak, že jsem slyšel: Projděte skrze město za ním, a bíte; neodpouštějž oko vaše, aniž se slitovávejte.
Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
6 Starce, mládence i pannu, maličké i ženy mordujte do vyhubení, ale ke všelikému muži, na němž by bylo znamení, nepřistupujte, a od svatyně mé počněte. Takž začali od mužů těch starších, kteříž byli před chrámem.
Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
7 (Nebo jim byl řekl: Poškvrňte domu, a naplňte síně zbitými. Jdětež.) A vyšedše, bili v městě.
Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
8 I stalo se, když je bili, a já pozůstal, že jsem padl na tvář svou, a zvolal jsem, řka: Ach, Panovníče Hospodine, zdaliž zahubíš všecken ostatek Izraelský, vylévaje prchlivost svou na Jeruzalém?
Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
9 I řekl mi: Nepravost domu Izraelského a Judského veliká jest velmi velice, a naplněna jest země mordy, a město plné jest převrácenců. Nebo říkali: Opustil Hospodin zemi tuto, a Hospodin nikoli nevidí nás.
Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
10 Protož já také cestu jejich na hlavu jejich obrátím; neodpustí oko mé, aniž se slituji.
Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
11 A aj, muž oděný rouchem lněným, při jehož bedrách byl kalamář, oznámil to, řka: Učinil jsem, jakž jsi mi rozkázal.
Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

< Ezechiel 9 >