< Ezechiel 5 >

1 Potom ty synu člověčí, vezmi sobě nůž ostrý, totiž břitvu holičů, vezmi jej sobě, a ohol ním hlavu i bradu svou. Potom vezma sobě váhu, rozděl to.
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
2 Třetinu ohněm spal u prostřed města, když se vyplní dnové obležení; zatím vezma druhou třetinu, posekej mečem okolo něho; ostatní pak třetinu rozptyl u vítr. Nebo mečem dobytým budu je stihati.
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
3 A však odejmi odtud něco málo, a zavaž do křídel svých.
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
4 A i z těch ještě vezma, uvrz je do prostřed ohně, a spal je ohněm, odkudž vyjde oheň na všecken dům Izraelský.
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
5 Takto praví Panovník Hospodin: Tento Jeruzalém, kterýž jsem postavil u prostřed pohanů, a vůkol otočil krajinami,
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
6 Změnil soudy mé v bezbožnost více než pohané, a ustanovení má více než jiné země, kteréž jsou vůkol něho; nebo soudy mými pohrdli, a v ustanoveních mých nechodili.
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
7 Protož takto praví Panovník Hospodin: Proto že mnohem více než pohané, kteříž jsou vůkol vás, v ustanoveních mých nechodili jste, a soudů mých nečinili jste, nýbrž ani tak jako pohané, kteříž jsou vůkol vás, soudů nekonali jste:
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
8 Protož takto praví Panovník Hospodin: Aj, já na tebe, aj já, a vykonám u prostřed tebe soudy před očima pohanů.
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
9 Nebo učiním při tobě to, čehož jsem prv neučinil, a čehož podobně neučiním více pro všecky ohavnosti tvé,
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
10 Tak že otcové jísti budou syny u prostřed tebe, a synové jísti budou otce své, a vykonám proti tobě soudy, a rozptýlím všecky ostatky tvé na všecky strany.
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
11 Protož živť jsem já, praví Panovník Hospodin, že poněvadž jsi ty svatyně mé poškvrnil všelikými mrzkostmi svými, a všelikými ohavnostmi svými, i já také zlehčím tebe, a neodpustíť oko mé, a nikoli se neslituji.
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
12 Třetina tebe morem zemře a hladem zhyne u prostřed tebe, a třetina druhá mečem padne vůkol tebe, ostatní pak třetinu na všecky stany rozptýlím, a mečem dobytým stihati je budu.
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
13 A tak do konce vylit bude hněv můj, a dotru prchlivostí svou na ně, i potěším se. I zvědíť, že já Hospodin mluvil jsem v horlivosti své, když vykonám prchlivost svou na nich,
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
14 A obrátím tě v poušť, a dám tě v útržku mezi národy, kteříž jsou vůkol tebe, před očima každého tudy jdoucího.
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
15 A tak budeš k útržce, posměchu, k hroznému příkladu a k užasnutí národům, kteříž jsou vůkol tebe, tehdáž když vykonám proti tobě soudy v hněvě a v prchlivosti a v žehrání zůřivém. Já Hospodin mluvil jsem.
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
16 Tehdáš když vystřelím jízlivé střely hladu k záhubě vaší, kteréž vystřelím, abych vás vyhubil, a hlad shromáždě proti vám, zlámi vám hůl chleba.
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
17 Pošli zajisté na vás hlad a zvěř lítou, kteráž tě na sirobu přivede; i mor a krev přijde na tebe, když uvedu na tě meč. Já Hospodin mluvil jsem.
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

< Ezechiel 5 >