< Ezechiel 44 >

1 Tedy přivedl mne zase cestou k bráně svatyně zevnitřní, kteráž patří k východu, a ta byla zavřená.
Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
2 I řekl ke mně Hospodin: Brána tato zavřená bude, nebudeť otvírána, aniž kdo bude vcházeti skrze ni. Nebo Hospodin Bůh Izraelský všel skrze ni; protož budeť zavřená.
Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
3 Knížecí jest, kníže samo v ní sedati bude, aby jídalo chléb před Hospodinem. Cestou síně této brány vejde, a cestou její vyjde.
Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
4 I vedl mne cestou k bráně půlnoční, k přední straně domu, i viděl jsem, a aj, naplnila sláva Hospodinova dům Hospodinův. I padl jsem na tvář svou.
Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
5 I řekl ke mně Hospodin: Synu člověčí, přilož srdce své, a viz očima svýma, i ušima svýma slyš, cožkoli já mluvím tobě o všech ustanoveních domu Hospodinova, i o všech zákonech jeho. Přilož, pravím, srdce své k vcházení do domu, i ke všemu vycházení z svatyně,
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
6 A rci zpurnému domu Izraelskému: Takto praví Panovník Hospodin: Dosti mějte na všech ohavnostech svých, ó dome Izraelský,
Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
7 Že jste uvodili cizozemce neobřezaného srdce a neobřezaného těla, aby bývali v svatyni mé, a poškvrňovali i domu mého, když jste obětovali chléb můj, tuk i krev, ješto oni sic rušili smlouvu mou, mimo všecky ohavnosti vaše,
Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
8 A nedrželi jste stráže nad svatými věcmi mými, ale postavili jste strážné na stráži mé, v svatyni mé místo sebe.
Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
9 Takto praví Panovník Hospodin: Žádný cizozemec neobřezaného srdce a neobřezaného těla nevejde do svatyně mé, ze všech cizozemců, kteříž mezi syny Izraelskými jsou.
Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
10 Nýbrž i Levítové, kteříž se vzdalovali ode mne, když bloudil Izrael, kteříž zbloudili ode mne za ukydanými bohy svými, ponesou nepravost svou.
“Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
11 Nebo budou v svatyni mé za služebníky, v povinnostech při branách domu, a za slouhy při domu. Oni budou zabíjeti oběti zápalné i oběti lidu, a oni stávati budou před nimi k sloužení jim,
Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
12 Proto že přisluhovali jim před ukydanými bohy jejich, a byli domu Izraelskému příčinou pádu v nepravost. Pročež přisáhl jsem jim, praví Panovník Hospodin, že ponesou nepravost svou.
Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
13 Aniž přistoupí ke mně, aby mi kněžský úřad konali, ovšem aby přistupovati měli k kterým svatým věcem mým, neb k nejsvětějším, ale ponesou pohanění své i ohavnosti své, kteréž páchali.
Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
14 Protož postavím je za strážné u domu, ke vší službě jeho i ke všemu, což činěno býti má v něm.
Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
15 Kněží pak Levítští, synové Sádochovi, kteříž drželi stráž nad svatyní mou, když zbloudili synové Izraelští ode mne, ti budou přistupovati ke mně, aby mi přisluhovali, a státi před tváří mou, obětujíce mi tuk i krev, praví Panovník Hospodin.
“Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Ti přicházeti budou k svatyni mé, a ti přistupovati k stolu mému, aby mi sloužili a drželi stráž mou.
Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
17 I stane se, když budou míti vcházeti do bran síně vnitřní, že roucha lněná oblekou, aniž na se vezmou vlněného, když by služby konati měli v branách síně vnitřní i u vnitřku.
“Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
18 Klobouky lněné míti budou na hlavě své, a košilky lněné ať mají na bedrách svých, a nepřepasují se ničímž, což by pot vyvodilo.
Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
19 A majíce vyjíti do síně zevnitřní, do síně zevnitřní k lidu, svlekou roucha svá, v kterýchž služby konali, a nechají jich v komůrkách svatyně, a oblekou roucha jiná, a nebudou posvěcovati lidu rouchem svým.
Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
20 Aniž hlavy své holiti budou, ani vlasů nositi, ale slušně ostříhají vlasy své.
“‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
21 Vína též nebude píti žádný z kněží, když budou míti vcházeti do síně vnitřní.
Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
22 Vdovy také aneb zahnané nebudou sobě pojímati za manželky, ale panny z semene domu Izraelského, aneb vdovu, kteráž by ovdověla po knězi, pojíti mohou.
Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
23 A lid můj budou rozdílu učiti mezi svatým a nesvatým, též mezi nečistým a čistým ať je učí rozeznávati.
Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
24 V rozepři pak ať se postavují k souzení, a podlé soudu mého soudí ji. Zákonů mých i ustanovení mých při všech slavnostech mých ať ostříhají, a soboty mé světí.
“‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
25 K mrtvému pak člověku nepůjde, aby se poškvrniti měl, leč při otci neb při mateři, též při synu a při dceři, při bratru a sestře, kteráž nebyla za mužem, může se poškvrniti.
“‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
26 Po očištění pak jeho (sedm dní odečtou jemu),
Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
27 V ten den, v kterýž vejde do svatyně, do síně vnitřní, aby služby konal v svatyni, obětovati bude za hřích svůj, praví Panovník Hospodin.
Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
28 Dědictví pak jejich toto: Já jsem dědictví jejich, protož vládařství nedávejte jim v Izraeli; já jsem vládařství jejich.
“‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
29 Oběti suché a za hřích i vinu, to oni jísti budou, i všelijaká věc, oddána Bohu v Izraeli, jejich bude.
Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
30 I přední věci všech prvotin ze všeho, i každá obět zhůru pozdvižení všeliké věci, ze všech obětí zhůru pozdvižení vašich, kněžské bude. I prvotiny těsta vašeho dávati budete knězi, aby odpočinulo požehnání v domě tvém.
Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
31 Žádné mrchy a udáveného, ani z ptactva ani z hovad nebudou jídati kněží.
Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”

< Ezechiel 44 >