< Ezechiel 39 >

1 Ty synu člověčí, prorokuj ještě proti Gogovi a rci: Takto praví Panovník Hospodin: Aj, já povstanu proti tobě, ó Gogu, kníže a hlavo v Mešech a Tubal.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 A odvedu tě zpět, navštívě tě šesti ranami, když tě vzbudím, abys přitáhl od stran půlnočních, a přivedu tě na hory Izraelské.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 Nebo vyrazím lučiště tvé z ruky tvé levé, a střely z ruky tvé pravé vyvrhu.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Na horách Izraelských padneš ty i všickni houfové tvoji i národové, kteříž budou s tebou; ptákům a všemu ptactvu křídla majícímu i zvěři polní dám tě k sežrání.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Na svrchku pole padneš; neboť jsem já mluvil, praví Panovník Hospodin.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 Vypustím také oheň na Magoga i na ty, kteříž přebývají na ostrovích bezpečně, i zvědíť, že já jsem Hospodin.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 A jméno svatosti své uvedu v známost u prostřed lidu svého Izraelského. Nedopustím, pravím, více poškvrňovati jména svatosti své, i zvědíť národové, že já jsem Hospodin Svatý v Izraeli.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Aj, přijdeť a stane se to, praví Panovník Hospodin, téhož dne, o kterémž jsem mluvil.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Tehdy vyjdou obyvatelé měst Izraelských, a zapálíce, popálí zbroj a štíty i pavézy, lučiště i střely, dřevce i kopí, a budou je páliti ohněm sedm let.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Aniž nositi budou dříví s pole, ani sekati v lesích, proto že zbrojí zaněcovati budou oheň, když zloupí ty, kteříž je loupívali, a mocí poberou těm, kteříž jim mocí brávali, praví Panovník Hospodin.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 I stane se v ten den, že dám Gogovi místo ku pohřbu tam v Izraeli, údolí, kudyž se jde k východní straně k moři, kteréžto zacpá ústa tudy jdoucích. I pohřbí tam Goga i všecko množství jeho, a nazovou je údolí množství Gogova.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 Nebo pochovávati je budou dům Izraelský za sem měsíců proto, aby vyčistili zemi.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 A tak pohřbí je všecken lid té země, a bude jim to ku poctivosti v den, v kterýž oslaven budu, praví Panovník Hospodin.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 Oddělíť pak muže statečné, kteříž by procházeli tu zemi, proto aby pochovávali ty, kteříž by pozůstali na svrchku země, aby ji vyčistili. Po vyjití sedmi měsíců přehledávati začnou.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 A ti procházejíce, choditi budou po zemi, a když uzří kosti člověčí, vzdělají při nich znamení pamětné, aby je pohřbili hrobaři v údolí množství Gogova.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 Nýbrž to množství jeho bude k slávě i městu, když vyčistí tu zemi.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Ty pak synu člověčí, takto praví Panovník Hospodin: Rci ke všelijakým ptákům křídla majícím i ke všelijaké zvěři polní: Shromažďte se a přiďte, zbeřte se odevšad k obětem mým, kterýchž já nabiji vám, obětí velikých na horách Izraelských, a budete jísti maso a píti krev.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 Maso silných reků jísti budete, a krev knížat zemských píti, skopců, beranů a kozlů, volků, všecko tučných Bázanských.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 A budete jísti tuk do sytosti, a píti krev do opití z obětí mých, kterýchž vám nabiji.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 A nasytíte se z stolu mého koňmi i jezdci, silnými reky i všemi muži válečnými, dí Panovník Hospodin.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 A tak zjevím slávu svou mezi národy, aby viděli všickni národové soud můj, kterýž jsem vykonal, i ruku mou, kterouž jsem doložil na ně.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 I zvíť dům Izraelský, že já jsem Hospodin Bůh jejich, od tohoto dne i potom.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 Zvědí také i národové, že pro svou nepravost zajat jest dům Izraelský, proto že se dopouštěli přestoupení proti mně; pročež jsem skryl tvář svou před nimi, a vydal jsem je v ruku protivníků jejich, aby padli mečem všickni napořád.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 Podlé nečistoty jejich a podlé zpronevěření se jejich učinil jsem jim, a skryl jsem tvář svou před nimi.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Z té příčiny takto praví Panovník Hospodin: Jižť zase přivedu zajaté Jákobovy, a smiluji se nade vším domem Izraelským a horliti budu příčinou jména svatosti své,
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 Ač ponesou potupu svou a všecko přestoupení své, kteréhož se dopustili proti mně, když bydlili v zemi své bezpečně, aniž byl, kdo by je přestrašil.
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 A však je zase přivedu z národů, a shromáždím je z zemí nepřátel jejich, a posvěcen budu v nich před očima národů mnohých.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 A tak poznají, že já jsem Hospodin Bůh jejich, když zaveda je do národů, shromáždím je do země jejich, a nepozůstavím tam žádného z nich.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 Aniž skryji více tváři své před nimi, když vyleji Ducha svého na dům Izraelský, praví Panovník Hospodin.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezechiel 39 >