< Ezechiel 24 >

1 Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně léta devátého, měsíce desátého, desátého dne téhož měsíce, řkoucí:
Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Synu člověčí, napiš sobě jméno tohoto dne, vlastně dnešního dne tohoto: nebo oblehl král Babylonský Jeruzalém právě tohoto dnešního dne.
“Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino.
3 A předlož tomu domu zpurnému podobenství, řka k nim: Takto praví Panovník Hospodin: Přistav tento hrnec, přistav a nalej také do něho vody.
Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti, “‘Ikani mʼphika pa moto, ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.
4 A sebera kusy náležité do něho, každý kus dobrý, stehno i plece, a nejlepšími kostmi napln jej.
Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama, nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba. Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.
5 Přivezmi i nejlepších bravů, a udělej oheň z kostí pod ním, způsob, ať to vře, ažby kypělo, ať se i kosti jeho rozvaří v něm.
Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri. Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo. Madzi awire. Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’
6 Protož takto praví Panovník Hospodin: Běda městu tomu vražedlnému, hrnci, v němž zůstává připálenina jeho, z něhož, pravím, připálenina jeho nevychází. Po kusích, po kusích vytahuj z něho, nepadneť na něj los.
“‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti, “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi, tsoka kwa mʼphika wadzimbiri; dzimbiri lake losachoka! Mutulutsemo nthuli imodzimodzi osasankhulapo.
7 Nebo krev jest u prostřed něho. Na vysedlou skálu vystavilo ji; nevylilo jí na zemi, aby ji prach přikryl.
“‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo. Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala. Sanawakhutulire pa dothi kuopa kuti fumbi lingawafotsere.
8 I já zanítě prchlivost k vykonání pomsty, vystavím krev na vysedlou skálu, aby nebyla přikryta.
Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala kuti asafotseredwe ndi fumbi chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.
9 Protož takto praví Panovník Hospodin: Běda městu vražedlnému, i já udělám veliký oheň,
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi! Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.
10 Přikládaje dříví, rozněcuje oheň, v nic obraceje maso, a kořeně kořením, tak že i kosti spáleny budou.
Choncho wonjeza nkhuni ndipo muyatse moto. Phikani nyamayo bwinobwino, muthiremo zokometsera, mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.
11 A postavím ten hrnec na uhlí jeho prázdný, aby se zhřela i rozpálila měď jeho, ažby se vyvařila u prostřed něho nečistota jeho, a vyprázdnila připálenina jeho.
Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo mpaka utenthe kuchita kuti psuu kuti zonyansa zake zisungunuke ndi kuti dzimbiri lake lichoke.
12 Klamy svými bylo mi těžké, protož nevyjde z něho množství šumu jeho; do ohně musí šum jeho.
Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa. Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka ngakhale ndi moto womwe.
13 V tvé nečistotě jest nešlechetnost, proto že jsem tě očišťoval, však nejsi očištěno. Nebudeš více očišťováno od nečistoty své, až i doložím prchlivost svou na tebe.
“‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.
14 Já Hospodin mluvil jsem, dojdeť, a učiním to; neustoupímť, aniž se slituji, ani želeti budu. Podlé cest tvých a činů tvých budou tě souditi, praví Panovník Hospodin.
“‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’”
15 Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Yehova anandiyankhula kuti:
16 Synu člověčí, aj, já odejmu od tebe žádost očí tvých v náhle, však nekvěl ani plač, a nechť nevycházejí slzy tvé.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi.
17 Stonati přestaň, smutku, jakž bývá nad mrtvým, nenes, klobouk svůj vstav na sebe, a střevíce své obuj na nohy své, a nezastírej brady své, aniž pokrmu čího jez.
Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”
18 Což když jsem pověděl lidu ráno, tedy umřela žena má u večer. I učinil jsem na ráno, jakž mi rozkázáno bylo.
Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.
19 I řekl ke mně lid: Což nám neoznámíš, co tyto věci nám znamenají, kteréž činíš?
Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”
20 Tedy řekl jsem jim: Slovo Hospodinovo stalo se ke mně, řkoucí:
Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti,
21 Rci domu Izraelskému: Takto praví Panovník Hospodin: Aj, já poškvrním svatyně své, vyvýšenosti síly vaší, žádosti očí vašich a toho, čehož šanuje duše vaše. Též synové vaši i dcery vaše, kterýchž jste zanechali, mečem padnou.
‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga.
22 I budete tak činiti, jakž já činím. Brady nezastřete, aniž čího pokrmu jísti budete.
Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa.
23 A majíce klobouky své na hlavách svých a střevíce na nohách svých, nebudete kvíliti ani plakati, ale svadnouce pro nepravosti své, úpěti budete jeden s druhým.
Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu.
24 Nebo jest vám Ezechiel zázrakem. Všecko, což on činí, budete činiti, a když to přijde, tedy zvíte, že já jsem Panovník Hospodin.
Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’
25 Ty pak synu člověčí, zdali v ten den, když já odejmu od nich sílu jejich, veselé okrasy jejich, žádost očí jejich, a to, po čemž touží duše jejich, syny jejich i dcery jejich,
“Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi.
26 Zdali v ten den přijde k tobě ten, kdož uteče, vypravuje tu novinu?
Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo.
27 V ten den otevrou se ústa tvá při přítomnosti toho, kterýž ušel, i budeš mluviti, a nebudeš více němým. Takž jim budeš zázrakem, i zvědí, že já jsem Hospodin.
Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezechiel 24 >