< Ezechiel 17 >

1 Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Synu člověčí, vydej pohádku, a předlož podobenství o domu Izraelském,
“Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
3 A rci: Takto praví Panovník Hospodin: Orlice veliká, velikých křídel a dlouhých brků, plná peří, strakatá, přiletěvši na Libán, vzala vrch cedru.
Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
4 Vrch mladistvých ratolestí jeho ulomila, a přenesla jej do země kupecké; v městě kupeckém položila jej.
Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
5 Potom vzavši z semene té země, vsadila je v poli úrodném, a vsadila je velmi opatrně při vodách mnohých.
“‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
6 Kteréžto bylo by vzešlo, a bylo by révem bujným, jakžkoli nízké postavy, a byly by patřily ratolesti jeho k ní, a kořenové jeho poddáni byli by jí, a tak bylo by kmenem vinným, kterýž by vydal byl ratolesti, a vypustil rozvody.
Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
7 Ale byla orlice jedna veliká velikých křídel a vypeřená, a aj, ten kmen vinný připjal kořeny své k ní, a ratolesti své vztáhl k ní, aby svlažovala jej z brázd štípení svého,
“‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
8 Ješto v poli dobrém, při vodách mnohých štípen byl, aby vypustil ratolesti, a nesl ovoce, a byl kmenem slavným.
Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
9 Rci: Takto praví Panovník Hospodin: Zdaliž se podaří? Zdaliž kořenů jeho nevytrhá, a ovoce jeho neotrhá a neusuší? Zdaž všech ratolestí vyrostlých z něho neusuší? Zdaliž s velikou silou a s mnohým lidem nevyhladí ho z kořenů jeho?
“Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
10 Aj, jakžkoli štípen, zdaliž se podaří? Zdaliž, jakž se ho dotkne vítr východní, do konce neuschne? Při brázdách, při nichž se ujal, zdaž neuschne?
Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
11 Za tím stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
12 Rci nyní domu zpurnému: Nevíte-liž, co je toto? Rci: Aj, přitáhl král Babylonský do Jeruzaléma, a vzal krále jeho i knížata jeho, a zavedl je s sebou do Babylona.
“Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
13 Vzal také z semene královského, a učiniv s ním smlouvu, přísahou jej zavázal, a silné země té pobral,
Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
14 Aby bylo království snížené, proto aby se nepozdvihovalo, aby ostříhaje smlouvy jeho, tak stálo.
kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
15 Ale zprotivil se jemu, poslav posly své do Egypta, aby jemu podal koní a lidu mnohého. Zdaž se mu to podaří? Zdaž pomsty ujde ten, kdož tak činí? Ten kdož ruší smlouvu, zdaliž pomsty ujde?
Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
16 Živť jsem já, praví Panovník Hospodin, že v místě krále toho, kterýž jej králem učinil, jehož přísahou pohrdl, a jehož smlouvu zrušil, u něho v Babyloně umře.
“‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
17 Aniž mu Farao s vojskem velikým a s zástupem mnohým co napomůže v boji, když vysype násyp, a vzdělá šance, aby zahubil množství lidí,
Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
18 Poněvadž pohrdl přísahou, zrušiv smlouvu. Neb aj, podal ruky své, a však všecko toto činí. Neujdeť pomsty.
Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
19 Protož takto praví Panovník Hospodin: Živť jsem já, že přísahu svou, kterouž pohrdl, a smlouvu svou, kterouž zrušil, jistotně obrátím na hlavu jeho.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
20 Nebo roztáhnu na něj sít svou, a polapen bude do vrše mé, i zavedu jej do Babylona, a souditi se s ním budu tam pro přestoupení jeho, kteréhož se dopustil proti mně.
Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
21 Všickni též, kteříž utekli od něho se všemi houfy jeho, od meče padnou, ostatní pak na všecky strany rozprostříni budou. I zvíte, že já Hospodin mluvil jsem.
Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
22 Takto praví Panovník Hospodin: A však vezmu z vrchu cedru toho vysokého a vsadím, z vrchu mladistvých ratolestí jeho mladou větvičku ulomím, a štípím na hoře vysoké a vyvýšené.
“‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
23 Na hoře vysoké Izraelské štípím ji, i vypustí ratolesti, a ponese ovoce, a tak učiněna bude cedrem slavným, a bude bydliti pod ním všeliké ptactvo; všecko, což křídla má, v stínu ratolestí jeho bydliti bude.
Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
24 A tak zvědí všecka dříví polní, že já Hospodin snížil jsem dřevo vysoké, a povýšil jsem dřeva nízkého; usušil jsem strom zelený, a způsobil to, aby zkvetl strom suchý. Já Hospodin mluvil jsem to i učiním.
Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”

< Ezechiel 17 >