< Ezechiel 1 >

1 Stalo se pak třidcátého léta, čtvrtého měsíce, dne pátého, když jsem byl mezi zajatými u řeky Chebar, že otevřína byla nebesa, a viděl jsem vidění Boží.
Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.
2 Pátého dne téhož měsíce, pátého léta zajetí krále Joachina,
Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende,
3 V pravdě stalo se slovo Hospodinovo k Ezechielovi knězi, synu Buzi, v zemi Kaldejské u řeky Chebar, a byla nad ním ruka Hospodinova.
Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.
4 I viděl jsem, a aj, vítr tuhý přicházel od půlnoci, a oblak veliký, a oheň plápolající, a okolo něho byl blesk, a z prostředku jeho jako nějaká velmi prudká světlost, z prostředku toho ohně.
Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira.
5 Z prostředku jeho také ukázalo se podobenství čtyř zvířat, jejichž takový byl způsob: Podobenství člověka měli.
Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu
6 A po čtyřech tvářích jedno každé, a po čtyřech křídlích jedno každé mělo.
koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi.
7 Jejichž nohy nohy přímé, ale zpodek noh jejich jako zpodek nohy telecí, a blyštěly se podobně jako ocel pulerovaná.
Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira.
8 Ruce pak lidské pod křídly jejich, po čtyřech stranách jejich, a tváři jejich i křídla jejich na čtyřech těch stranách.
Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko,
9 Spojena byla křídla jejich jednoho s druhým. Neobracela se, když šla; jedno každé přímo na svou stranu šlo.
ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.
10 Podobenství pak tváří jejich s předu tvář lidská, a tvář lvová po pravé straně každého z nich; tvář pak volovou po levé straně všech čtvero, též tvář orličí s zadu mělo všech čtvero z nich.
Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga.
11 A tváři jejich i křídla jejich pozdvižena byla zhůru. Každé zvíře dvě křídla pojilo s křídly dvěma druhého, dvěma pak přikrývala těla svá.
Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake.
12 A každé přímo na svou stranu šlo. Kamkoli ukazoval duch, aby šla, tam šla, neuchylovala se, když chodila.
Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita.
13 Podobnost také těch zvířat na pohledění byla jako uhlí řeřavého, na pohledění jako pochodně. Kterýžto oheň ustavičně chodil mezi zvířaty, a ten oheň měl blesk, a z téhož ohně vycházelo blýskání.
Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo.
14 Také ta zvířata běhala, a navracovala se jako prudké blýskání.
Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.
15 A když jsem hleděl na ta zvířata, a aj, kolo jedno bylo na zemi při zvířatech u čtyř tváří jednoho každého z nich.
Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi.
16 Na pohledění byla kola, a udělání jich jako barva tarsis, a podobnost jednostejnou měla všecka ta kola, a byla na pohledění i udělání jejich, jako by bylo kolo u prostřed kola.
Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana.
17 Na čtyři strany své jíti majíce, chodila, a neuchylovala se, když šla.
Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka.
18 A loukoti své, i vysokost měla, že hrůza z nich šla, a šínové jejich vůkol všech čtyř kol plní byli očí.
Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.
19 Když pak chodila zvířata, chodila kola podlé nich, a když se vznášela zvířata vzhůru od země, vznášela se i kola.
Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso.
20 Kdekoli chtěl Duch, aby šla, tam šla; kde Duch chtěl jíti, i kola vznášela se naproti nim, nebo duch zvířat byl v kolách.
Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija.
21 Když ona šla, šla, a když ona stála, stála, a když se vznášela od země, vznášela se také kola s nimi, nebo duch zvířat byl v kolách.
Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.
22 Podobenství pak oblohy bylo nad hlavami zvířat jako podobenství křištálu roztaženého nad hlavami jejich svrchu.
Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake.
23 A pod oblohou křídla jejich pozdvižená byla, jedno připojené k druhému. Každé mělo dvě, jimiž se přikrývalo, každé, pravím, mělo dvě, jimiž přikrývalo tělo své.
Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake.
24 I slyšel jsem zvuk křídel jejich jako zvuk vod mnohých, jako zvuk Všemohoucího, když chodila, zvuk hluku jako zvuk vojska. Když pak stála, spustila křídla svá.
Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.
25 Byl také zvuk svrchu nad oblohou, kteráž byla nad hlavou jejich, když stála a spustila křídla svá.
Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake.
26 Svrchu pak na obloze, kteráž byla nad hlavou jejich, bylo podobenství trůnu, na pohledění jako kámen zafirový, a nad podobenstvím trůnu na něm svrchu, na pohledění jako tvárnost člověka.
Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu.
27 I viděl jsem na pohledění jako velmi prudkou světlost, a u vnitřku jejím vůkol na pohledění jako oheň, od bedr jeho vzhůru; od bedr pak jeho dolů viděl jsem na pohledění jako oheň, a blesk vůkol něho.
Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo.
28 Na pohledění jako duha, kteráž bývá na oblace v čas deště, takový na pohledění byl blesk vůkol. To bylo vidění podobenství slávy Hospodinovy. Kteréžto viděv, padl jsem na tvář svou, a slyšel jsem hlas mluvícího.
Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula. Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.

< Ezechiel 1 >