< 2 Mojžišova 38 >

1 Udělal také oltář k zápalu z dříví setim, pěti loket zdélí a pěti loket zšíří, čtverhraný, a tří loket zvýší.
Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
2 A zdělal mu rohy na čtyřech úhlech jeho; z něho byli rohové jeho, a obložil jej mědí.
Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
3 Nadělal také všelijakých nádob k oltáři, hrnců a lopat, a kotlíků a vidliček, a nádob jeho k uhlí; všecka nádobí jeho udělal měděná.
Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 Udělal k oltáři i rošt mřežovaný, měděný, pod okolkem oltáře dole, až do prostřed něho.
Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
5 A slil čtyři kruhy na čtyřech krajích k roštu měděnému, v nichž by sochorové bývali.
Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
6 Sochory pak udělal z dříví setim a obložil je mědí.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
7 A uvlékl ty sochory do těch kruhů po obou stranách oltáře k nošení jeho na nich; prázdný z prken udělal jej.
Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
8 Udělal též umyvadlo měděné, a podstavek jeho měděný z zrcadel houfně přicházejících žen, kteréž přicházely ke dveřím stánku úmluvy.
Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
9 Udělal také síň k straně polední; koltry očkovaté síně té z bílého hedbáví přesukovaného na sto loket,
Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 Sloupů jejich dvadceti, a k nim podstavků dvadceti z mědi, háky na sloupích, a přepásaní jejich z stříbra.
Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 Tolikéž k straně půlnoční koltry na sto loket, sloupů k nim dvadceti a podstavků jejich dvadceti z mědi, háky na sloupích a přepásaní jejich z stříbra.
Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 K straně pak západní koltry očkovaté na padesáte loket, sloupů k nim deset a podstavků jejich deset, háky na sloupích a přepásaní jejich z stříbra.
Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
13 A v straně přední na východ padesáti loktů,
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
14 Koltry očkovaté patnácti loktů byly při straně jedné, sloupové k nim tři, a podstavkové jejich tři.
Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
15 A k straně druhé, u brány síně té, jakž tam, tak tuto, koltry očkovaté patnácti loktů, sloupové k nim tři a podstavkové jejich tři.
polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Všecky koltry síně vůkol očkovaté z bílého hedbáví přesukovaného.
Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
17 Podstavkové pak sloupů z mědi, hákové na sloupích a přepásaní jich z stříbra, a obložení makovic jejich z stříbra; všickni také sloupové síně přepásáni byli stříbrem.
Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
18 Zastření pak brány síňce dílem krumpéřským z postavce modrého a šarlatu, a červce dvakrát barveného a hedbáví bílého přesukovaného; dlouhost jeho dvadceti loktů, výsost pak šířky pěti loktů, jako i jiných koltr síně očkovatých.
Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
19 A sloupové k ní čtyři a podstavkové jejich čtyři z mědi, hákové jejich stříbrní, a obložení makovic jejich a přepásaní jejich z stříbra.
pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
20 Všickni pak kolíkové příbytku a síně vůkol byli z mědi.
Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
21 Tyto jsou věci vyčtené k příbytku, příbytku svědectví, kteréž jsou vyčteny podlé rozkázaní Mojžíšova, skrze Itamara, syna Arona kněze, k službě Levítů.
Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
22 A Bezeleel, syn Uri, syna Hur, z pokolení Juda, udělal všecky tyto věci, kteréž přikázal Hospodin Mojžíšovi;
Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
23 A s ním Aholiab, syn Achisamechův z pokolení Dan, tesař a vtipný řemeslník, a krumpéř na modrém postavci a šarlatu, a červci dvakrát barveném a kmentu.
pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
24 Všeho zlata vynaloženého na samo dílo, na všecko dílo svatyně, (bylo pak zlato obětované), devět a dvadceti centnéřů, a sedm set třidceti lotů podlé váhy svatyně.
Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
25 Stříbra pak od těch, jenž náležejí ku počtu shromáždění, sto centnéřů, a tisíc sedm set sedmdesáte pět lotů podlé váhy svatyně.
Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
26 Půl lotu z každé hlavy podlé váhy svatyně, ode všech jdoucích v počet od dvadcíti let a výše, jichž bylo šestkrát sto tisíc, tři tisíce pět set a padesáte.
Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
27 A bylo sto centnéřů stříbra k slévání podstavků svatyně a podstavků opony; sto podstavků ze sta centnéřů, centnéř do podstavku.
Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
28 A z tisíce sedmi set sedmdesáti pěti lotů udělal háky na sloupy, a obložil makovice jejich a přepásal je.
Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
29 Mědi pak obětované bylo sedmdesáte centnéřů a dva tisíce a čtyři sta lotů.
Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
30 A udělal z ní podstavky ke dveřům stánku svědectví a oltář měděný, a rošt měděný k němu, a všecky nádoby oltáře,
Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
31 A podstavky síně vůkol a podstavky brány síně, všecky také kolíky příbytku a všecky kolíky síňce vůkol.
matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

< 2 Mojžišova 38 >