< 2 Mojžišova 1 >

1 Tato jsou pak jména synů Izraelských, kteříž vešli do Egypta s Jákobem; každý s čeledí svou přišel:
Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
2 Ruben, Simeon, Léví a Juda;
Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
3 Izachar, Zabulon a Beniamin;
Isakara, Zebuloni, Benjamini;
4 Dan a Neftalím, Gád a Asser.
Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
5 A bylo všech osob pošlých z bedr Jákobových sedmdesáte duší; Jozef pak byl v Egyptě.
Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
6 I umřel Jozef a všickni bratří jeho, a všecken ten rod.
Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
7 Synové pak Izraelští rozmnožili se a rodili se v hojnosti; a rozhojňovali se, i zsilili se náramně velmi, a naplněna jest jimi země.
Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
8 V tom povstal král nový v Egyptě, kterýž neznal Jozefa.
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
9 Ten řekl lidu svému: Aj, lid synů Izraelských jest mnohý a silnější nad nás.
Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
10 Nuže, opatrně sobě počínejme před ním, aby se nerozmohl; a když by přišla válka, aby se nepřipojil i on k nepřátelům našim, a nebojoval proti nám, a nevyšel z země.
Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
11 Protož ustanovili nad ním úředníky, kteříž by plat vybírali, aby je trápili břemeny svými. I vystavěl lid Izraelský Faraonovi města skladů, Fiton a Ramesses.
Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
12 Ale čím více trápili jej, tím více rostl a tím se více rozmáhal. I vzali sobě syny Izraelské v ošklivost.
Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
13 A tak podrobovali Egyptští syny Izraelské v službu těžkou.
ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
14 A k hořkosti přivodili život jejich robotami těžkými, v hlině a cihlách a ve všelijakém díle na poli, mimo všelikou potřebu svou, k níž práce jejich užívali nenáležitě a bez lítosti.
Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
15 I poručil král Egyptský babám Hebrejským, z nichž jedna sloula Sefora a druhá Fua,
Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
16 A řekl: Když budete pomáhati ženám Hebrejským při porodu, a uzříte, že již rodí, byl-li by syn, zabíte ho, pakli dcera, tedy ať jest živa.
“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
17 Bály se pak ty baby Boha, a nečinily tak, jakž jim poručil král Egyptský, ale živých nechávaly pacholíků.
Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
18 Povolav tedy bab král Egyptský, mluvil jim: Proč jste to učinily, že jste živé zachovaly pacholíky?
Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
19 I odpověděly baby Faraonovi: Nejsou ženy Hebrejské jako ženy Egyptské; nebo ony jsou silnějšího přirození. Dříve než přijde k nim baba, ony porodí.
Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
20 I učinil dobře Bůh těm babám. A rozmnožen jest lid, a zsilili se velmi.
Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
21 Stalo se pak proto, že se bály baby ty Boha, vzdělal jim domy.
Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
22 I přikázal Farao všemu lidu svému, řka: Každého syna, kterýž se narodí, do řeky uvrzte; každé pak dcery nechte živé.
Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

< 2 Mojžišova 1 >