< Ester 1 >

1 Stalo se pak za času krále Asvera, (to jest ten Asverus, jenž kraloval od Indie až k Mouřenínské zemi nad sto dvadcíti a sedmi krajinami),
Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
2 Že toho času, když seděl král Asverus na stolici království svého, jenž byla v Susan, městě královském,
Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
3 Léta třetího kralování svého, učinil u sebe hody všechněm knížatům svým a služebníkům svým, nejznamenitějším Perským a Médským, hejtmanům a vládařům nad krajinami,
ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
4 Ukazuje bohatství, slávu království svého a čest, i ozdobu důstojnosti své za mnoho dnů, totiž za sto a osmdesáte dnů.
Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
5 (A když se vyplnili dnové ti, učinil král všemu lidu, což ho koli bylo v Susan městě královském, od největšího až do nejmenšího, hody za sedm dní na paláci v zahradě při domě královském.)
Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
6 Též čalouny bílé, zelené a z postavce modrého, zavěšené na provázcích kmentových a šarlatových u kroužků stříbrných, na sloupích mramorových, lůžka zlatá a stříbrná na podlaze porfyretové a mramorové, pariové a socharetové.
Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
7 Nápoj pak dávali v nádobách zlatých, a to v nádobách jiných a jiných, i vína královského v hojnosti, jakž slušelo na krále.
Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
8 Ale ku pití, podlé nařízení, žádný nenutil. Nebo tak poručil král všechněm správcům domu svého, aby činili podlé vůle jednoho každého.
Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
9 Také i královna Vasti učinila hody ženám v domě královském krále Asvera.
Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
10 Dne pak sedmého, když se podveselil král vínem, rozkázal Mehumanovi, Biztovi, Charbonovi, Bigtovi a Abagtovi, Zetarovi a Karkasovi, sedmi komorníkům, kteříž sloužili před oblíčejem krále Asvera,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
11 Aby přivedli Vasti královnu před oblíčej krále v koruně královské, aby okázal národům i knížatům krásu její; nebo velmi krásná byla.
kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
12 Ale odepřela královna Vasti přijíti k rozkazu královskému, skrze ty komorníky vzkázanému. Pročež král rozhněval se velmi a rozpálil se hněvem sám v sobě.
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
13 I řekl král mudrcům znajícím časy, (nebo tak každé věci podával král na všecky zběhlé v právích a soudech),
Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
14 A nejbližšímu sebe Charsenovi, Setarovi, Admatovi, Tarsisovi, Meresovi, Marsenovi, Memuchanovi, sedmi vývodám Perským a Médským, jenž vídali tvář královskou, a sedali první po králi:
Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
15 Co se má podlé práva státi s královnou Vasti, proto že nevyplnila rozkazu krále Asvera, stalého skrze komorníky?
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
16 Tedy řekl Memuchan před králem i knížaty: Ne proti samému králi zavinila královna Vasti, ale proti všechněm knížatům, a proti všechněm národům všech krajin Asvera krále.
Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
17 Nebo když se donese to, co učinila královna, všech žen, zlehčí sobě muže své a řeknou: An král Asverus rozkázal přivésti královnu Vasti před oblíčej svůj, a však nepřišla.
Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
18 Nýbrž ještě tohoto dne budou to mluviti kněžny Perské a Médské, (kteréž slyšely, co učinila královna), všechněm knížatům královským, i naplodí se hojně pýchy a zpoury.
Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
19 Jestliže se tedy králi za dobré vidí, nechť se stane výpověď královská od oblíčeje jeho, a nechť jest vepsána mezi práva Perská a Médská, kteráž by nemohla změněna býti, že nechtěla přijíti Vasti před oblíčej krále Asvera, pročež království její dá král jiné, lepší nežli ona.
“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
20 Tak když uslyší výpověd královskou, kterouž vyhlásiti dá po všem království svém, jakkoli veliké jest, všecky ženy v poctivosti míti budou manžely své, od největšího až do nejmenšího.
Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
21 I líbila se ta rada králi i knížatům, a učinil král podlé rady Memuchanovy.
Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
22 A rozeslal listy do všech krajin královských, do jedné každé krajiny písmem jejím, a do každého národu jazykem jeho, aby každý muž byl pánem domu svého. Což oznámil každý hejtman lidu jazykem jeho.
Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

< Ester 1 >