< Efezským 5 >

1 Buďtež tedy následovníci Boží, jakožto synové milí.
Choncho, monga ana okondedwa, tsatirani chitsanzo cha Mulungu.
2 A choďtež v lásce, jakož i Kristus miloval nás, a vydal sebe samého za nás, dar a obět Bohu u vůni rozkošnou.
Muzikondana monga Khristu anakonda ife nadzipereka yekha chifukwa cha ife monga chopereka cha fungo lokoma ndi nsembe kwa Mulungu.
3 Smilstvo pak a všeliká nečistota, neb lakomství, aniž jmenováno buď mezi vámi, jakož sluší na svaté,
Koma pakati panu pasamveke nʼpangʼono pomwe zadama, kapena za mtundu wina uliwonse wa chodetsa, kapena za umbombo, chifukwa izi ndi zosayenera kwa anthu oyera a Mulungu.
4 A tolikéž mrzkost, ani bláznové mluvení, ani šprýmování, kteréžto věci jsou nenáležité, ale raději ať jest díků činění.
Musamatukwane, kuyankhula zopusa kapena kunena nthabwala zopanda pake, zomwe ndi zosayenera, koma mʼmalo mwake muziyamika.
5 Víte zajisté o tom, že žádný smilník aneb nečistý, ani lakomec, (jenž jest modloslužebník, ) nemá dědictví v království Kristově a Božím.
Dziwani ichi, palibe wadama, wochita zonyansa kapena waumbombo, munthu wotero ali ngati wopembedza mafano, amenewa alibe malo mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu.
6 Žádný vás nesvoď marnými řečmi; nebo pro takové věci přichází hněv Boží na syny nepoddané.
Musalole wina akunamizeni ndi mawu opanda pake, pakuti chifukwa cha zinthu ngati izi mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa amene samvera.
7 Nebývejtež tedy účastníci jejich.
Nʼchifukwa chake musamayanjane nawo anthu otere.
8 Byli jste zajisté někdy temnosti, ale již nyní jste světlo v Pánu. Jakožto synové světla choďte,
Pajatu inu nthawi ina munali mdima, koma tsopano ndinu kuwunika mwa Ambuye. Mukhale ngati ana akuwunika
9 (Nebo ovoce Ducha záleží ve vší dobrotě, a spravedlnosti, a v pravdě, )
(pakuti pamene pali kuwunika pamapezekaponso zabwino zonse, chilungamo ndi choonadi).
10 O to stojíce, což by se dobře líbilo Pánu.
Inu mufufuze chimene chimakondweretsa Ambuye.
11 A neobcujte s skutky neužitečnými tmy, ale raději je trescete.
Musayanjane nazo ntchito zosapindulitsa za mdima, koma mʼmalo mwake muzitsutse.
12 Nebo což se tajně děje od nich, mrzko jest o tom i mluviti.
Pakuti ndi zochititsa manyazi ngakhale kutchula zomwe zimachitika mseri.
13 Všecko pak, což bývá trestáno, od světla bývá zjeveno; nebo to, což všecko zjevuje, světlo jest.
Koma kuwala kumawunikira zinthu, ndipo chilichonse chimaonekera poyera. Choncho chilichonse choonekera poyera chimasandukanso kuwala.
14 Protož praví: Probuď se ty, jenž spíš, a vstaň z mrtvých, a zasvítíť se tobě Kristus.
Nʼchifukwa chake Malemba akuti, “Dzuka, wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.”
15 Viztež tedy, kterak byste opatrně chodili, ne jako nemoudří, ale jako moudří,
Samalani makhalidwe anu, musakhale ngati opanda nzeru koma ngati anzeru.
16 Vykupujíce čas; nebo dnové zlí jsou.
Gwiritsani ntchito mpata uliwonse, chifukwa masiku ano ndi oyipa.
17 Protož nebývejte neopatrní, ale rozumějící, která by byla vůle Páně.
Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite.
18 A neopíjejte se vínem, v němžto jest prostopášnost, ale naplněni buďte Duchem svatým,
Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera.
19 Mluvíce sobě vespolek v žalmích, a v chvalách, a v písničkách duchovních, zpívajíce a plésajíce v srdcích vašich Pánu,
Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu.
20 Díky činíce vždycky ze všeho ve jménu Pána našeho Jezukrista Bohu a Otci,
Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
21 Poddáni jsouce jedni druhým v bázni Boží.
Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu.
22 Ženy mužům svým poddány buďte jako Pánu.
Inu akazi, muzigonjera amuna anu, monga mumagonjera kwa Ambuye.
23 Nebo muž jest hlava ženy, jako i Kristus jest hlava církve, a onť jest Spasitel těla.
Pakuti mwamuna ndi mutu wa mkazi monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, thupi lake, limene Iyeyo ndi Mpulumutsi wake.
24 A tak jakož církev poddána jest Kristu, tak i ženy mužům svým ať jsou poddány ve všem.
Tsono monga mpingo umagonjera Khristu, momwemonso akazi akuyenera kugonjera amuna awo mu zonse.
25 Muži milujte ženy své, jako i Kristus miloval církev, a vydal sebe samého za ni,
Inu amuna, kondani akazi anu monga momwe Khristu anakondera mpingo nadzipereka yekha mʼmalo mwa mpingowo
26 Aby ji posvětil, očistiv ji obmytím vody v slovu,
kuti awupatule ukhale oyera, atawuyeretsa powusambitsa ndi madzi omwe ndi mawu ake.
27 Aby ji sobě postavil slavnou církev, nemající poskvrny, ani vrásky, neb cokoli takového, ale aby byla svatá a bez úhony.
Anachita zimenezi kuti awupereke mpingowo kwa Iye mwini, mpingo wowala ndi waulemerero, wopanda banga kapena makwinya kapena chilema chilichonse, koma oyera ndi wangwiro.
28 Takť jsou povinni muži milovati ženy své jako svá vlastní těla. Kdo miluje ženu svou, sebeť samého miluje.
Momwemonso, amuna akuyenera kukonda akazi awo monga matupi awo. Iye amene akonda mkazi wake adzikondanso yekha.
29 Žádný zajisté nikdy těla svého neměl v nenávisti, ale krmí a chová je, jakožto i Pán církev.
Pakuti palibe amene amadana nalo thupi lake, koma amalidyetsa ndi kulisamalira bwino, monga momwe Khristu amachitira ndi mpingo wake
30 Neboť jsme údové těla jeho, z masa jeho a z kostí jeho.
pakuti ndife ziwalo za thupi lake.
31 A protoť opustí člověk otce i matku, a připojí se k manželce své, i budouť dva jedno tělo.
“Pa chifukwa ichi, mwamuna adzasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
32 Tajemství toto veliké jest, ale já pravím o Kristu a o církvi.
Ichi ndi chinsinsi chozama, koma ine ndikunena za Khristu ndi mpingo.
33 Avšak i vy, jeden každý z vás, manželku svou tak jako sám sebe miluj. Žena pak ať se bojí muže svého.
Chomwecho, aliyense mwa inu akuyenera kukonda mkazi wake monga adzikondera iye mwini, ndipo mkazi akuyenera kulemekeza mwamuna wake.

< Efezským 5 >