< Kazatel 9 >

1 Všecko to zajisté rozvažoval jsem v srdci svém, abych vysvětlil všecko to, že spravedliví a moudří, i skutkové jejich jsou v rukou Božích. Jakož milosti, tak ani nenávisti nezná člověk ze všech věcí, kteréž jsou před oblíčejem jeho.
Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
2 Všecko se děje jednostejně při všech; jedna a táž případnost jest spravedlivého jako bezbožného, dobrého a čistého jako nečistého, obětujícího jako toho, kterýž neobětuje, tak dobrého jako hříšníka, přisahajícího jako toho, kterýž se přísahy bojí.
Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
3 A toť jest přebídná věc mezi vším tím, což se děje pod sluncem, že případnost jednostejná jest všechněch, ovšem pak že srdce synů lidských plné jest zlého, a že bláznovství přídrží se srdce jejich, pokudž živi jsou, potom pak umírají,
Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
4 Ačkoli ten, kterýž tovaryší se všechněmi živými, má naději, an psu živému lépe jest nežli lvu mrtvému.
Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
5 Nebo živí vědí, že umříti mají, mrtví pak nevědí nic, aniž více mají odplaty, proto že v zapomenutí přišla památka jejich.
Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
6 Anobrž i milování jejich, i nenávist jejich, i závist jejich zahynula, a již více nemají dílu na věky v žádné věci, kteráž se děje pod sluncem.
Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
7 Nuže tedy jez s radostí chléb svůj, a pí s veselou myslí víno své, nebo již oblibuje Bůh skutky tvé.
Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
8 Každého času ať jest roucho tvé bílé, a oleje na hlavě tvé nechť není nedostatku.
Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
9 Živ buď s manželkou, kterouž jsi zamiloval, po všecky dny života marnosti své, kterýžť dán pod sluncem po všecky dny marnosti tvé; nebo to jest podíl tvůj v životě tomto a při práci tvé, kterouž vedeš pod sluncem.
Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
10 Všecko, což by před se vzala ruka tvá k činění, podlé možnosti své konej; nebo není práce ani důmyslu ani umění ani moudrosti v hrobě, do něhož se béřeš. (Sheol h7585)
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
11 A obrátiv se, spatřil jsem pod sluncem, že nezáleží běh na rychlých, ani boj na udatných, nýbrž ani živnost na moudrých, ani bohatství na opatrných, ani přízeň na umělých, ale podlé času a příhody přihází se všechněm.
Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
12 Nebo tak nezná člověk času svého jako ryby, kteréž loveny bývají sítí škodlivou, a jako ptáci polapeni bývají osídlem; tak zlapáni bývají synové lidští v čas zlý, když na ně připadá v náhle.
Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
13 Také i tuto moudrost viděl jsem pod sluncem, kteráž za velikou byla u mne:
Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
14 Bylo město malé, a v něm lidí málo, k němuž přitáhl král mocný, a obehnav je, zdělal proti němu náspy veliké.
Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
15 I nalezen jest v něm muž chudý moudrý, kterýž vysvobodil to město moudrostí svou, ačkoli žádný nevzpomenul na muže toho chudého.
Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
16 Protož řekl jsem já: Lepší jest moudrost než síla, ačkoli moudrost chudého toho byla v pohrdání, a slov jeho neposlouchali.
Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
17 Slov moudrých pokojně poslouchati sluší, raději než křiku panujícího mezi blázny.
Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
18 Lepší jest moudrost než nástrojové váleční, ale nemoudrý jeden kazí mnoho dobrého.
Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

< Kazatel 9 >