< 5 Mojžišova 25 >
1 Vznikla-li by jaká nesnáz mezi některými, a přistoupili by k soudu, aby je rozsoudili, tedy spravedlivého ospravedlní, a nepravého odsoudí.
Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
2 Bude-li pak hoden mrskání nepravý, tedy káže ho položiti soudce a mrskati před sebou, vedlé nepravosti jeho v jistý počet ran.
Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
3 Ètyřidcetikrát káže ho mrštiti, aniž přidá více, aby, jestliže by jej nadto mrskal ranami mnohými, nebyl příliš zlehčen bratr tvůj před očima tvýma.
koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
4 Nezavížeš úst vola mlátícího.
Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
5 Když by bratří spolu bydlili, a umřel by jeden z nich, nemaje syna, nevdá se ven žena toho mrtvého za jiného muže; bratr jeho vejde k ní, a vezme ji sobě za manželku, a právem švagrovství přižení se k ní.
Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
6 Prvorozený pak, kteréhož by porodila, nazván bude jménem bratra jeho mrtvého, aby nebylo vyhlazeno jméno jeho z Izraele.
Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
7 Nechtěl-li by pak muž ten pojíti příbuzné své, tedy přijde příbuzná jeho k bráně před starší a řekne: Nechce příbuzný můj vzbuditi bratru svému jména v Izraeli, a nechce podlé práva švagrovství pojíti mne.
Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
8 Tedy povolají ho starší města toho, a mluviti budou s ním; a stoje, řekl-li by: Nechci jí pojíti,
Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
9 Přistoupí příbuzná jeho k němu před staršími, a szuje střevíc jeho s nohy jeho, a pline mu na tvář a odpoví, řkuci: Tak se má státi muži tomu, kterýž by nechtěl vzdělati domu bratra svého.
mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
10 I bude nazváno jméno jeho v Izraeli: Dům bosého.
Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
11 Když by se svadili někteří spolu jeden s druhým, a přistoupila by žena jednoho, aby vysvobodila muže svého z ruky bijícího jej, i vztáhla by ruku svou a uchopila by ho za lůno:
Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
12 Tedy utneš ruku její, neslituje se nad ní oko tvé.
muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
13 Nebudeš míti v pytlíku svém nejednostejného kamene, většího a menšího.
Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
14 Aniž budeš míti v domě svém nejednostejného korce, většího a menšího.
Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
15 Váhu celou a spravedlivou míti budeš, též míru celou a spravedlivou budeš míti, aby se prodlili dnové tvoji v zemi, kterouž Hospodin Bůh tvůj dává tobě.
Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
16 Nebo v ohavnosti jest Hospodinu Bohu tvému, kdožkoli činí ty věci, všeliký činící nepravost.
Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
17 Pamatuj na to, coť učinil Amalech na cestě, když jste šli z Egypta:
Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
18 Kterak vyšed tobě v cestu, zadní houf tvůj všech mdlých, kteříž šli za tebou, pobil, když jsi ty byl zemdlený a ustalý, a nebál se Boha.
Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
19 Protož když byl Hospodin Bůh tvůj dal tobě odpočinutí ode všech nepřátel tvých vůkol v zemi, kterouž Hospodin Bůh tvůj dává tobě v dědictví, abys dědičně obdržel ji, vyhladíš památku Amalecha pod nebem; nezapomínejž na to.
Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!