< 5 Mojžišova 24 >
1 Pojal-li by muž ženu a byl by manželem jejím, přihodilo by se pak, že by nenašla milosti před očima jeho pro nějakou mrzkost, kterouž by nalezl na ní, i napsal by jí lístek zapuzení a dal v ruku její, a vyhnal by ji z domu svého;
Ngati mwamuna wakwatira mkazi amene sakukondwera naye chifukwa wapeza vuto pa mkaziyo, namulembera mkaziyo kalata ya chisudzulo, namupatsa ndi kumutulutsa mʼnyumba mwake,
2 A vyjduci z domu jeho, odešla by a vdala se za druhého muže;
mkaziyo ndi kukakwatiwa ndi mwamuna wina,
3 A ten také muž poslední v nenávisti maje ji, napsal by lístek zapuzení a dal v ruce její, a vyhnal by ji z domu svého; aneb umřel by muž její poslední, kterýž vzal ji sobě za manželku:
ndipo mwamuna wachiwiriyo nʼkuyipidwa nayenso ndi kumulemberanso kalata ya chisudzulo nʼkumutulutsa mʼnyumba mwake, kapena ngati mwamunayo amwalira,
4 Nebude moci manžel její první, kterýž ji vyhnal, zase ji vzíti sobě za manželku, když již příčinou jeho poškvrněna jest; nebo ohavnost jest před Hospodinem. Protož nedopouštěj hřešiti lidu země, kterouž Hospodin Bůh tvůj dává tobě v dědictví.
mwamuna wake woyamba uja, amene anamuleka saloledwanso kumukwatira kachiwiri popeza mkaziyo wadetsedwa. Chimenechi ndi chonyansa pamaso pa Yehova. Musalowetse tchimo mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu.
5 Když by někdo v nově pojal ženu, nevyjde k boji, aniž na něj vzkládána bude jaká obecní práce; svoboden bude v domě svém za jeden rok, a veseliti se bude s manželkou svou, kterouž pojal.
Mwamuna akangokwatira kumene asamatumizidwe ku nkhondo kapena kupatsidwa ntchito ina iliyonse. Kwa chaka chathunthu akhale ndi ufulu wokhala pa khomo pake kumasangalatsa mkazi wakeyo.
6 Žádný nevezme v zástavě svrchního i spodního žernovu, nebo takový bral by duši v základu.
Munthu akakhala nanu ndi ngongole musamutengere mwala wake wa mphero ngati chikole, chifukwa kutero nʼkumutengera moyo kukhala chikole cha ngongole.
7 Byl-li by postižen někdo, že ukradl člověka z bratří svých synů Izraelských, a k zisku by sobě jej přivedl aneb prodal jej: umře zloděj ten, a odejmeš zlé z prostředku svého.
Ngati munthu agwidwa akuba mʼbale wake wa Chiisraeli namamuzunza ngati kapolo kapena kumugulitsa, wogulitsa mnzakeyo ayenera kuphedwa. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
8 Šetř se při ráně malomocenství, abys ostříhal pilně a činil všecko, jakž učiti budou vás kněží Levítové; jakož přikázal jsem jim, ostříhati toho budete a tak činiti.
Pakagwa matenda a khate, samalitsani kuchita zonse zimene ansembe, amene ndi Alevi, anakulangizani. Mutsatire mosamalitsa zimene ndinawalamula.
9 Pomni na ty věci, které učinil Hospodin Bůh tvůj Marii na cestě, když jste vyšli z Egypta.
Kumbukirani zimene Yehova Mulungu wanu anachita kwa Miriamu muli paulendo mutatuluka mu Igupto.
10 Půjčil-li bys bližnímu svému něčeho, nevejdeš do domu jeho, abys vzal něco v zástavě od něho.
Ukabwereketsa mnzako kanthu kena kalikonse, usalowe mʼnyumba mwake kukatenga chimene wachipereka ngati chikole.
11 Ale vně staneš, a člověk, jemuž jsi půjčil, vynese tobě základ svůj ven.
Uziyima kunja kwa nyumba kuti munthu amene wamubwereketsa kanthuyo akubweretsere kunja komweko.
12 Jestliže by pak byl člověk chudý, nebudeš spáti s základem jeho.
Ngati munthuyo ndi wosauka, usamutengere chikolecho mpaka kukagona nacho kwanu.
13 Bez prodlévání navrátíš jemu zastavenou věc jeho při západu slunce, aby leže v šatech svých, dobrořečil tobě, a bude to za spravedlnost tobě před Hospodinem Bohem tvým.
Pomalowa dzuwa ukhale utamubwezera mkanjo wakewo kuti akafunde. Pamenepo adzakuthokoza, ndipo amenewa adzawerengedwa ngati machitidwe olungama kwa iweyo pamaso pa Yehova Mulungu wako.
14 Neutiskneš nájemníka chudého a nuzného, tak z bratří svých jako z příchozích, kteříž jsou v zemi tvé v branách tvých.
Osamapezera mwayi pa anthu aganyu osauka ndi aumphawi, kaya ndi Mwisraeli kapena mlendo wokhala mu umodzi mwa mizinda yanu.
15 Na každý den dáš jemu mzdu jeho, prvé nežli by slunce zapadlo; nebo chudý jest, a tím se živí, aby neúpěl proti tobě k Hospodinu, a byl by na tobě hřích.
Mumulipire malipiro ake a tsiku dzuwa lisanalowe chifukwa ndi wosauka ndipo akudalira malipirowo. Kupanda kutero adzakudandaulirani kwa Yehova ndipo mudzapezeka ochimwa.
16 Nebudou na hrdle trestáni otcové za syny, ani synové trestáni budou na hrdle za otce, jeden každý za svůj hřích umře.
Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.
17 Nepřevrátíš soudu příchozímu neb sirotku, ani vezmeš v základu roucha vdovy,
Musachitire mlendo kapena mwana wamasiye zoyipa, kapena kulanda mkazi wamasiye chovala ngati chikole cha ngongole.
18 Ale pamatuj, že jsi byl služebníkem v Egyptě, a že tě vykoupil Hospodin Bůh tvůj odtud; protož přikazujiť, abys činil toto.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwombolani kumeneko. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
19 Když bys žal obilí své na poli svém, a zapomenul bys tam některého snopu, nenavrátíš se, abys jej vzal; příchozímu, sirotku a vdově to bude, aby požehnal tobě Hospodin Bůh tvůj při všelikém díle rukou tvých.
Mukamakolola mʼmunda mwanu ndipo zokolola zina zikasiyidwa, musamabwerere kukazitola. Muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochita zanu zonse.
20 Když bys třásl olivy své, nebudeš shledávati po každé ratolesti za sebou; příchozímu, sirotku a vdově to zůstane.
Mukathyola zipatso mu mtengo wa olivi, musamabwererenso kachiwiri ku mtengo womwewo. Zotsalazo zilekereni alendo, ana ndi akazi amasiye.
21 Když bys sbíral víno na vinici své, nebudeš paběrovati jahodek za sebou; příchozímu, sirotku a vdově to bude.
Mukakolola mphesa mʼmunda mwanu musamabwereremonso kachiwiri. Zotsalazo muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye.
22 Pamatuj, že jsi byl služebníkem v zemi Egyptské; protož přikazujiť, abys to činil.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.