< 5 Mojžišova 19 >

1 Když by vyhladil Hospodin Bůh tvůj národy, jejichžto zemi Hospodin Bůh tvůj dává tobě, a opanoval bys je dědičně, a bydlil bys v městech jejich i v domích jejich:
Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
2 Oddělíš sobě tři města u prostřed země své, kterouž Hospodin Bůh tvůj dává tobě, abys ji dědičně obdržel.
mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
3 Spravíš sobě cesty, a rozdělíš na tři díly všecku krajinu země své, kterouž v dědictví dá tobě Hospodin Bůh tvůj, i bude utíkati tam každý vražedlník:
Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
4 (Totoť pak bude právo vražedlníka, kterýž by tam utekl, aby živ byl: Kdož by zabil bližního svého nechtě, aniž by ho nenáviděl prvé.
Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
5 Jako vejda někdo s bližním svým do lesa sekati dříví, rozvedl by rukou svou sekeru, aby uťal dřevo, a ona by spadla s topořiště, a trefila by bližního jeho, tak že by umřel, ten uteče do některého z měst těchto, a živ bude.)
Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
6 Aby přítel zabitého, stihaje vražedlníka toho, když by se rozpálilo srdce jeho, nedohonil ho na daleké cestě, a ranil smrtedlně, ješto by nebyl hoden smrti, poněvadž ho prvé neměl v nenávisti.
Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
7 Protož já přikazuji tobě, řka: Tři města oddělíš sobě.
Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
8 Pakli by rozšířil Hospodin Bůh tvůj končiny tvé, jakož s přísahou zaslíbil otcům tvým, a dal by tobě všecku tu zemi, kterouž řekl dáti otcům tvým:
Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
9 (Když bys ostříhal všech přikázaní těchto, čině je, kteráž já dnes přikazuji tobě, abys miloval Hospodina Boha svého, a chodil po cestách jeho po všecky dny), tedy přidáš sobě ještě tři města mimo tři onano,
chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
10 Aby nebyla vylita krev nevinná u prostřed země tvé, kterouž Hospodin Bůh tvůj dá tobě v dědictví, a aby nebyla na tobě krev.
Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
11 Ale byl-li by kdo, maje v nenávisti bližního svého, a činil by úklady jemu, a povstana proti němu, ranil by ho smrtedlně, tak že by umřel, a utekl by do některého z těch měst:
Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
12 Tedy pošlí starší města toho, a vezmou jej odtud, a dají v ruce přítele toho zabitého, aby umřel.
akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
13 Neodpustí jemu oko tvé, ale svedeš krev nevinnou z Izraele, i bude dobře tobě.
Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
14 Nepřeneseš meze bližního svého, kterouž vymezili předkové v dědictví tvém, kteréž obdržíš v zemi, jižto Hospodin Bůh tvůj dává tobě, abys ji dědičně obdržel.
Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
15 Nepovstane svědek jeden proti někomu z příčiny jakékoli nepravosti, a jakéhokoli hříchu ze všech hříchů, kterýmiž by kdo hřešil; v ústech dvou svědků aneb v ústech tří svědků stane slovo.
Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
16 Povstal-li by svědek falešný proti někomu, aby svědčil proti němu, že odstoupil od Boha,
Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
17 Tedy postaví se ti dva muži, kteříž tu rozepři mají před Hospodinem, před kněžími aneb před soudci, kteříž by za dnů těch byli.
anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
18 A když se pilně vyptají soudcové, poznají-li, že svědek ten jest svědek lživý, mluvě falešné svědectví proti bližnímu svému,
Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
19 Tak jemu učiňte, jakž on myslil učiniti bratru svému. I odejmeš zlé z prostředku svého.
ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
20 A kteříž zůstanou, slyšíce to, báti se budou, a nikoli více nedopustí se takových zlých věcí u prostřed tebe.
Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
21 A neslituje se oko tvé; život za život, oko za oko, zub za zub, ruka za ruku, noha za nohu bude.
Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.

< 5 Mojžišova 19 >