< Daniel 4 >

1 Nabuchodonozor král všechněm lidem, národům i jazykům, kteříž bydlí na vší zemi: Pokoj váš rozmnožen buď.
Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
2 Znamení a divy, kteréž učinil při mně Bůh nejvyšší, vidělo mi se za slušné, abych vypravoval.
Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
3 Znamení jeho jak veliká jsou, a divové jeho jak mocní jsou, království jeho království věčné, a panování jeho od národu do pronárodu.
Zizindikiro zake ndi zazikulu,
4 Já Nabuchodonozor, užívaje pokoje v domě svém, a kveta na palácu svém,
Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
5 Měl jsem sen, kterýž mne zhrozil, a myšlení na ložci svém, a to, což jsem viděl, znepokojilo mne.
Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
6 A protož vyšla ode mne ta výpověd, aby uvedeni byli přede mne mudrci Babylonští, kteříž by mi výklad toho snu oznámili.
Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
7 Tedy předstoupili mudrci, hvězdáři, Kaldejští a hadači. I pověděl jsem jim sen, a však výkladu jeho nemohli mi oznámiti.
Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
8 Až naposledy předstoupil přede mne Daniel, jehož jméno Baltazar, podlé jména boha mého, a v němž jest duch bohů svatých. Jemuž jsem oznámil sen:
Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
9 Baltazaře, kníže mudrců, já vím, že duch bohů svatých jest v tobě, a nic tajného není tobě nesnadného. Vidění snu mého, kterýž jsem měl, i výklad jeho oznam.
Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
10 U vidění pak, kteréž jsem viděl na ložci svém, viděl jsem, a aj, strom u prostřed země, jehož vysokost byla veliká.
Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
11 Veliký byl strom ten a mocný, a výsost jeho dosahovala až k nebi, a patrný byl až do končin vší země.
Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
12 Lístí jeho bylo pěkné, a ovoce jeho hojné, všechněm za pokrm, pod stínem pak jeho byla zvěř polní, a na ratolestech jeho bydlili ptáci nebeští, a z něho potravu měl všeliký živočich.
Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
13 Viděl jsem také u viděních svých na ložci svém, a aj, hlásný a svatý s nebe sstoupiv,
“Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
14 Volal ze vší síly, a tak pravil: Podetněte strom ten, a osekejte ratolesti jeho, a otlucte lístí jeho, a rozmecte ovoce jeho; nechať se vzdálí zvěř od něho, a ptáci z ratolestí jeho.
Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
15 A však kmene kořenů jeho v zemi zanechejte, a v poutech železných a ocelivých na trávě polní, aby rosou nebeskou smáčín byl, a díl jeho s zvěří v bylině zemské.
Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
16 Srdce jeho od lidského ať jest rozdílné, a srdce zvířecí nechť jest dáno jemu, ažby sedm let vyplnilo se při něm.
Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
17 Usouzení hlásných a řeč žádosti svatých stane se, ažby k tomu přišlo, aby poznali lidé, že Nejvyšší panuje nad královstvím lidským, a že komuž chce, dává je, a toho, kterýž jest ponížený mezi lidmi, ustanovuje nad ním.
“‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
18 Tento sen viděl jsem já Nabuchodonozor král, ty pak, Baltazaře, oznam výklad jeho. Nebo všickni mudrci v království mém nemohli mi výkladu oznámiti, ale ty můžeš, proto že duch bohů svatých jest v tobě.
“Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
19 Tedy Daniel, jemuž jméno Baltazar, předěšený stál za jednu hodinu, a myšlení jeho strašila ho. A odpověděv král, řekl: Baltazaře, sen ani výklad jeho nechť nestraší tebe. Odpověděl Baltazar a řekl: Pane můj, sen tento přiď na ty, kteříž tě v nenávisti mají, a výklad jeho na tvé nepřátely.
Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
20 Strom ten, kterýž jsi viděl, veliký a mocný, jehož výsost dosahovala až k nebi, a kterýž patrný byl po vší zemi.
Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
21 A lístí jeho pěkné, a ovoce jeho hojné, a z něhož všickni pokrm měli, pod nímž byla zvěř polní, a na ratolestech jeho bydlili ptáci nebeští,
mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
22 Ty jsi ten, ó králi, kterýž jsi rozšířil se a zmocnil, a velikost tvá vzrostla a vznesla se až k nebi, a panování tvé až do konce země.
Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
23 Že pak viděl král hlásného a svatého sstupujícího s nebe, kterýž řekl: Podetněte strom ten a zkazte jej, a však kmene kořenů jeho v zemi zanechejte, a v okovách železných a ocelivých ať jest na trávě polní, aby rosou nebeskou smáčín byl, a s zvěří polní díl jeho, ažby sedm let vyplnilo se při něm:
“Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
24 Tenť jest výklad, ó králi, a ortel Nejvyššího, kterýž vyšel na pána mého krále.
“Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
25 Nebo zaženou tě lidé od sebe, a s zvěří polní bude bydlení tvé, a bylinu jako volům tobě jísti dávati budou, a rosou nebeskou smáčín budeš, až se vyplní sedm let při tobě, dokudž bys nepoznal, že panuje Nejvyšší nad královstvím lidským, a že komuž chce, dává je.
Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
26 Že pak řekli, aby zanechán byl kmen kořenů toho stromu, království tvé tobě zůstane, jakž jen poznáš, že nebesa panují.
Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
27 Protož ó králi, přijmi radu mou, a hříchy své spravedlností přetrhuj, a nepravosti své milostivostí k ssouženým, zdaby prodloužen byl pokoj tvůj.
Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
28 Všecko to přišlo na krále Nabuchodonozora.
Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
29 Nebo po dokonání dvanácti měsíců, procházeje se po palácu královském v Babyloně,
Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
30 Mluvil král a řekl: Zdaliž toto není ten Babylon veliký, kterýž jsem já vystavěl mocí síly své, aby byl stolicí království k ozdobě slávy mé?
iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
31 Ještě ta řeč byla v ústech krále, a aj, hlas s nebe přišel: Toběť se praví, Nabuchodonozoře králi, že království odešlo od tebe,
Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
32 Nýbrž tě lidé i z sebe vyvrhou, a s zvěří polní bydliti budeš. Bylinu jako volům tobě jísti dávati budou, ažby sedm let vyplnilo se při tobě, dokudž bys nepoznal, že panuje Nejvyšší nad královstvím lidským, a že komuž chce, dává je.
Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
33 V touž hodinu řeč ta naplnila se při Nabuchodonozorovi. Nebo z spolku lidí vyvržen byl, a bylinu jako vůl jedl, a rosou nebeskou tělo jeho smáčíno bylo, až na něm vlasy zrostly jako peří orličí, a nehty jeho jako pazoury ptačí.
Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
34 Při skonání pak těch dnů já Nabuchodonozor pozdvihl jsem očí svých k nebi, a rozum můj ke mně se zase navrátil. I dobrořečil jsem Nejvyššímu, a živého na věky chválil jsem a oslavoval; nebo panování jeho jest panování věčné, a království jeho od národu do pronárodu.
Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
35 A všickni obyvatelé země jako za nic počteni jsou, a podlé vůle své činí mezi vojskem nebeským i obyvateli země, aniž jest kdo, ješto by mu přes ruku dáti mohl, a říci jemu: Co to děláš?
Anthu onse a dziko lapansi
36 Téhož času rozum můj navrátil se ke mně, a k slávě království mého ozdoba má, i důstojnost má navrátila se ke mně; nadto i hejtmané moji a knížata má hledali mne, a zmocněn jsem v království svém, a velebnost větší jest mi přidána.
Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
37 Nyní tedy já Nabuchodonozor chválím, vyvyšuji a oslavuji krále nebeského, jehož všickni skutkové jsou pravda, a stezky jeho soud, a kterýž chodící v pýše může snižovati.
Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.

< Daniel 4 >