< 2 Samuelova 1 >

1 Stalo se pak po smrti Saulově, když se navrátil David od porážky Amalechitských, že pobyl v Sicelechu za dva dni.
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 A aj, dne třetího přišel jeden z vojska Saulova, maje roucho roztržené a prach na hlavě své. Kterýž když přišel k Davidovi, padl na zemi a poklonil se.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 I řekl jemu David: Odkud jdeš? Jemuž odpověděl: Z vojska Izraelského utekl jsem.
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 Opět řekl jemu David: Cože se stalo? Medle, pověz mi. Kterýž odpověděl: To, že utekl lid z boje, a množství lidu padlo a zbito jest; též i Saul i Jonata syn jeho zbiti jsou.
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 Řekl ještě David mládenci, kterýž mu to oznámil: Kterak ty víš, že umřel Saul i Jonata syn jeho?
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 Odpověděl mládenec, kterýž to oznamoval jemu: Náhodou přišel jsem na horu Gelboe, a aj, Saul nalehl byl na kopí své, a vozové i jezdci postihali ho.
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 Kterýžto ohlédna se zpátkem, uzřel mne a zavolal na mne. I řekl jsem: Aj, teď jsem.
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 Tedy řekl mi: Kdo jsi ty? Odpověděl jsem jemu: Amalechitský jsem.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 I řekl mi: Přistup medle sem a zabí mne, nebo mne obklíčila úzkost, a ještě všecka duše má jest ve mně.
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 Protož stoje nad ním, zabil jsem ho, nebo jsem věděl, že nebude živ po svém pádu. A vzal jsem korunu, kteráž byla na hlavě jeho, i záponu, kteráž byla na rameni jeho, a teď jsem to přinesl ku pánu svému.
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 Tedy David uchytiv roucho své, roztrhl je; tolikéž i všickni muži, kteříž s ním byli.
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 A nesouce smutek, plakali a postili se až do večera pro Saule a pro Jonatu syna jeho, i pro lid Hospodinův a pro dům Izraelský, že padli od meče.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 Řekl pak David mládenci, kterýž mu to oznámil: Odkud jsi ty? Odpověděl: Syn muže příchozího Amalechitského jsem.
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 Opět mu řekl David: Kterak jsi směl vztáhnouti ruku svou, abys zahubil pomazaného Hospodinova?
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 A zavolav David jednoho z mládenců, řekl jemu: Přistoupě, oboř se na něj. Kterýžto udeřil ho, tak že umřel.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 I řekl jemu David: Krev tvá budiž na hlavu tvou, neboť jsou ústa tvá svědčila na tebe, řkouce: Já jsem zabil pomazaného Hospodinova.
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 Tedy naříkal David naříkáním tímto nad Saulem a nad Jonatou synem jeho,
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 (Přikázav však, aby synové Judovi učeni byli stříleti z luku, jakož psáno v knize Upřímého.):
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 Ó kráso Izraelská, na výsostech tvých zraněni, jakť jsou padli udatní!
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Neoznamujtež v Gát, ani toho ohlašujte na ulicích Aškalon, aby se neveselily dcery Filistinských, a neplésaly dcery neobřezaných.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 Ó hory Gelboe, ani rosa, ani déšť nespadej na vás, ani tu buď pole úrodné; nebo tam jest povržen štít udatných, štít Saulův, jako by nebyl pomazán olejem.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 Od krve raněných a od tuku udatných lučiště Jonatovo nikdy zpět neodskočilo, a meč Saulův nenavracoval se prázdný.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Saul a Jonata milí a utěšení v životě svém, také při smrti své nejsou rozloučeni. Nad orlice bystřejší, nad lvy silnější byli.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 Dcery Izraelské, plačte Saule, kterýž vás odíval červcem dvakrát barveným rozkošně, kterýž dával ozdoby zlaté na roucha vaše.
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 Ach, jakť jsou padli udatní u prostřed boje? Jonata na výsostech tvých zabit jest.
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Velice jsem po tobě teskliv, bratře můj Jonato. Byl jsi mi příjemný náramně; vzácnější u mne byla milost tvá nežli milost žen.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 Ach, jakť jsou padli udatní, a zahynula odění válečná.
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< 2 Samuelova 1 >