< 2 Samuelova 9 >

1 Tedy řekl David: Jest-li ještě kdo pozůstalý z domu Saulova, abych jemu učinil milosrdenství pro Jonatu?
Davide anafunsa kuti, “Kodi alipo amene watsala mʼbanja la Sauli kuti ndimuchitire chifundo chifukwa cha Yonatani?”
2 Byl pak služebník domu Saulova, jehož jméno bylo Síba. I zavolali ho k Davidovi. I řekl král jemu: Ty-li jsi Síba? Odpověděl: Jsem služebník tvůj.
Tsono panali mtumiki wina wa banja la Sauli wotchedwa Ziba. Iwo anamuyitana kuti aonekere pamaso pa Davide, ndipo mfumu inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe Ziba?” Iyeyo anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
3 Řekl jemu král: Jest-liž ještě kdo z domu Saulova, abych jemu učinil milosrdenství Boží? Odpověděl Síba králi: Ještě jest syn Jonatův chromý na nohy.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi palibe amene watsala wa banja la Sauli amene ndingamuchitire chifundo cha Mulungu?” Ziba anayankha mfumu kuti, “Alipo mwana wa Yonatani, koma ndi wolumala mapazi ake onse.”
4 I řekl jemu král: Kdež jest? Odpověděl Síba králi: Tam jest v domě Machiry, syna Amielova v Lodebar.
Mfumu inafunsa kuti, “Ali kuti?” Ziba anayankha kuti, “Iye ali ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli ku Lodebara.”
5 Protož poslav král David, vzal ho z domu Machiry, syna Amielova z Lodebar.
Kotero mfumu inamubweretsa kuchokera ku Lodebara, ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli.
6 A když přišel Mifibozet syn Jonaty, syna Saulova, k Davidovi, padl na tvář svou a poklonil se. I řekl David: Mifibozete. Kterýž odpověděl: Aj, služebník tvůj.
Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli atafika kwa Davide, anawerama pansi kupereka ulemu kwa iye. Davide anati, “Mefiboseti!” Iye anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”
7 Řekl jemu David: Neboj se, nebo jistě učiním s tebou milosrdenství pro Jonatu otce tvého, a navrátím tobě všecka pole Saule otce tvého, a ty jídati budeš za stolem mým vždycky.
Davide anati kwa iye, “Usachite mantha, pakuti ndidzakuchitira ndithu chifundo chifukwa cha abambo ako Yonatani. Ine ndidzakubwezera iwe dziko lonse limene linali la agogo ako Sauli, ndipo iweyo udzadya ndi ine nthawi zonse.”
8 Kterýž pokloniv se, řekl: Co jest služebník tvůj, že jsi se ohlédl na psa mrtvého, jakýž jsem já?
Mefiboseti anawerama pansi ndipo anati, “Mtumiki wanu ndine yani kuti musamale galu wakufa ngati ine?”
9 Zatím povolal král Síby, služebníka Saulova a řekl jemu: Cožkoli měl Saul i všecka čeled jeho, to jsem dal synu pána tvého.
Kenaka Davide anayitanitsa Ziba, mtumiki wa Sauli, ndipo anati, “Ine ndapereka kwa chidzukulu cha mbuye wako chilichonse chimene chinali cha Sauli ndi banja lake.
10 Budeš tedy jemu spravovati rolí, ty i synové tvoji i služebníci tvoji, a snášeti budeš, aby měl syn pána tvého pokrm, kterýž by jedl, ale Mifibozet syn pána tvého jídati bude vždycky za stolem mým. (Měl pak Síba patnácte synů a dvadceti služebníků.)
Iwe ndi ana ndi antchito anu muzimulimira mʼdziko lake ndipo muzibweretsa zokololazo kuti chidzukulu cha mbuye wako chikhale ndi chakudya. Ndipo Mefiboseti, chidzukulu cha mbuye wako adzadya ndi ine nthawi zonse.” (Tsono Ziba anali ndi ana aamuna khumi ndi asanu ndi antchito makumi awiri).
11 Odpověděl Síba králi: Vedlé všeho, jakž přikázal pán můj král služebníku svému, tak učiní služebník tvůj, ačkoli i Mifibozet mohl by jídati za stolem mým jako jeden z synů královských.
Ndipo Ziba anati kwa mfumu, “Mtumiki wanu adzachita chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mudzalamulire wantchito wanu kuti achite.” Kotero Mefiboseti ankadya ndi Davide monga mmodzi wa ana a mfumu.
12 Měl také Mifibozet syna malého, jemuž jméno bylo Mícha; a všickni, kteříž bydlili v domě Síbově, byli za služebníky Mifibozetovi.
Mefiboseti anali ndi mwana wamngʼono wamwamuna wotchedwa Mika, ndipo onse a banja la Ziba anali antchito a Mefiboseti.
13 A tak Mifibozet zůstával v Jeruzalémě, proto že vždycky za stolem královským jídal; a byl kulhavý na obě noze.
Ndipo Mefiboseti anakhala mu Yerusalemu chifukwa nthawi zonse amadya ndi mfumu. Iye anali wolumala mapazi ake onse.

< 2 Samuelova 9 >