< 2 Samuelova 24 >

1 Tedy opět prchlivost Hospodinova popudila se proti Izraelovi; nebo byl ponukl satan Davida na ně, řka: Jdi, sečti lid Izraelský a Judský.
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 Protož řekl král Joábovi, hejtmanu vojska svého: Projdi i hned všecka pokolení Izraelská od Dan až k Bersabé, a sečtěte lid, abych věděl počet jeho.
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 Ale Joáb řekl králi: Přidejž Hospodin Bůh tvůj k lidu, jakž ho koli mnoho, stokrát více, a to aby oči pána mého krále viděly. Ale proč pán můj král jest toho tak žádostiv?
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 A však přemohla řeč králova Joába i knížata vojska. Protož vyšel Joáb a knížata vojska od tváři královy, aby sečtli lid Izraelský.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 A přepravivše se přes Jordán, položili se při Aroer po pravé straně města, kteréž jest u prostřed potoka Gád, a při Jazer.
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 Potom přišli do Galád a do země dolejší nové, odkudž šli do Dan Jáhan a do okolí Sidonského.
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 Přišli také ku pevnosti Týru, a ke všem městům Hevejských a Kananejských; odkudž šli na poledne země Judské do Bersabé.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 A když schodili všecku zemi, přišli po přeběhnutí devíti měsíců a dvadcíti dní do Jeruzaléma.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 I dal Joáb počet sečteného lidu králi. Bylo pak lidu Izraelského osmkrát sto tisíc mužů silných, kteříž mohli vytrhnouti meč k bitvě. Mužů také Judských pětkrát sto tisíc.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Potom padlo to těžce na srdce Davidovi, když již sečtl lid. I řekl David Hospodinu: Zhřešilť jsem těžce, že jsem to učinil, ale nyní, ó Hospodine, odejmi, prosím, nepravost služebníka svého, nebť jsem velmi bláznivě učinil.
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 Když pak vstal David ráno, stalo se slovo Hospodinovo k Gádovi proroku, vidoucímu Davidovu, řkoucí:
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 Jdi a rci Davidovi: Toto praví Hospodin: Trojíť věci podávám, vyvol sobě jednu z nich, kteroužť bych učinil.
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 Protož přišed Gád k Davidovi, oznámil mu to, a řekl jemu: Chceš-li, aby přišel na tebe hlad za sedm let v zemi tvé? čili abys za tři měsíce utíkal před nepřátely svými, a oni aby tě honili? čili aby za tři dni byl mor v zemi tvé? Pomysliž spěšně, a viz, jakou mám odpověd dáti tomu, kterýž mne poslal.
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 I řekl David k Gádovi: Úzkostmi sevřín jsem náramně; nechať, prosím, upadneme v ruku Hospodinovu, neboť jsou mnohá slitování jeho, jediné ať v ruce lidské neupadám.
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 A tak uvedl Hospodin mor na Izraele od jitra až do času uloženého, a zemřelo jich z lidu od Dan až do Bersabé sedmdesáte tisíc mužů.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 A když vztáhl anděl ruku svou na Jeruzalém, aby hubil jej, litoval Hospodin toho zlého, a řekl andělu, kterýž hubil lid: Dostiť jest, již přestaň. Anděl pak Hospodinův byl u humna Aravny Jebuzejského.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 I mluvil David Hospodinu, když uzřel anděla, an bije lid, a řekl: Aj, já jsem zhřešil, a já jsem neprávě učinil, ale tito, jsouce jako ovce, co učinili? Nechť jest, prosím, ruka tvá proti mně a proti domu otce mého.
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 Potom navrátiv se Gád k Davidovi v ten den, řekl jemu: Vstup a vzdělej Hospodinu oltář na humně Aravny Jebuzejského.
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 I šel David vedlé řeči Gádovy, jakož byl přikázal Hospodin.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 A vyhlédaje Aravna, uzřel krále s služebníky jeho, an jdou k němu; protož vyšed Aravna, poklonil se králi tváří svou až k zemi.
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 I řekl Aravna: Proč přišel pán můj král k služebníku svému? Odpověděl David: Abych koupil od tebe humno toto, na němž bych vzdělal oltář Hospodinu, aby přestala rána tato v lidu.
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 Opět řekl Aravna Davidovi: Nechť vezme a obětuje pán můj král, což se mu za dobré vidí. Aj, teď volové k oběti zápalné, a smyky vozové i přípravy volů na drva.
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Všecky ty věci dával králík Aravna králi. Řekl ještě Aravna králi: Hospodin Bůh tvůj zalibiž tě sobě.
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 Řekl pak král Aravnovi: Nikoli, ale raději koupím od tebe, a zaplatím, aniž budu obětovati Hospodinu Bohu svému oběti zápalné darem dané. A tak koupil David humno a voly za padesáte lotů stříbra.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 A vzdělav tu David oltář Hospodinu, obětoval oběti zápalné a pokojné. I byl milostiv Hospodin zemi, a přestala zhouba v Izraeli.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.

< 2 Samuelova 24 >