< 2 Samuelova 14 >

1 Srozuměv pak Joáb syn Sarvie, že by naklonilo se srdce královo k Absolonovi,
Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
2 Poslav do Tekoa, a povolav odtud ženy moudré, řekl jí: Medle, udělej se, jako bys zámutek měla, a oblec se, prosím, v roucho smutku, a nepomazuj se olejem, ale buď jako žena již za mnoho dní zámutek mající nad mrtvým.
Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
3 I půjdeš k králi a mluviti mu budeš vedlé řeči této. A naučil ji Joáb, co by měla mluviti.
Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
4 Protož mluvila žena ta Tekoitská králi, padši na tvář svou k zemi, a poklonu učinivši, řekla: Spomoz, ó králi.
Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
5 I řekl jí král: Což jest tobě? Odpověděla ona: Zajisté žena vdova jsem, a umřel mi muž můj.
Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
6 Měla pak služebnice tvá dva syny, kteříž svadili se spolu na poli, a když nebyl, kdo by je rozvadil, udeřil jeden druhého a zabil ho.
Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
7 Aj, teď povstala všecka rodina proti služebnici tvé, a řekli: Vydej toho, jenž zabil bratra svého, ať ho zabijeme za život bratra jeho, kteréhož zamordoval, nýbrž zahubíme i dědice. A tak uhasí jiskru mou, kteráž pozůstala, aby nezanechali muži mému jména a ostatku na zemi.
Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
8 Tedy řekl král ženě: Navrať se do domu svého, a jáť poručím o tobě.
Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
9 I odpověděla žena Tekoitská králi: Nechť jest, pane můj králi, na mne ta nepravost, a na dům otce mého, král pak a stolice jeho ať jest bez viny.
Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
10 Řekl také král: Bude-li kdo mluviti co proti tobě, přiveď ho ke mně, a nedotkneť se tebe více.
Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
11 Tedy ona řekla: Rozpoměň se, prosím, králi, na Hospodina Boha svého, aby se nerozmnožili mstitelé krve k zhoubě a nezahladili syna mého. I odpověděl: Živť jest Hospodin, žeť nespadne vlas syna tvého na zemi.
Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
12 K tomu řekla žena: Nechť promluví, prosím, služebnice tvá pánu svému králi slovo. Kterýžto odpověděl: Mluv.
Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
13 I řekla žena: Proč jsi tedy myslil podobnou věc proti lidu Božímu? Nebo mluví král řeč tuto jako ten, kterýž sebe vinného činí, poněvadž nechce zase povolati vyhnaného svého.
Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
14 Všickniť jsme zajisté nepochybně smrtelní a jako vody, kteréž rozlity jsouce po zemi, zase sebrány býti nemohou, aniž se Bůh na něčí osobu ohlédá; ovšemť i myšlení svá vynesl, aby vyhnaného nevyháněl od sebe.
Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
15 Nyní pak, že jsem přišla ku pánu svému králi mluviti řeči tyto, příčina jest, že mne strašil lid. Protož řekla služebnice tvá: Budu nyní mluviti králi, snad naplní král žádost služebnice své.
“Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
16 Neboť vyslyší král a vysvobodí služebnici svou z ruky muže, chtějícího vyhladiti mne i syna mého spolu z dědictví Božího.
Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
17 Řekla také služebnice tvá: Vždyť mi bude slovo pána mého krále k odtušení; (nebo jako anděl Boží, tak jest pán můj král, když slyší dobré aneb zlé), a Hospodin Bůh tvůj bude s tebou.
“Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
18 A odpovídaje král, řekl ženě: Medle, netaj přede mnou toho, nač se já tebe vzeptám. I řekla žena: Mluv, prosím, pane můj králi.
Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
19 Tedy řekl král: Není-liž Joáb jednatel všeho tohoto? I odpověděla žena a řekla: Jako jest živa duše tvá, pane můj králi, žeť se nelze uchýliti na pravo aneb na levo ode všeho toho, což mluvil pán můj král; nebo služebník tvůj Joáb, onť jest mi rozkázal, a on naučil služebnici tvou všechněm slovům těmto,
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
20 A abych tak příkladně vedla řeč tuto, způsobil to služebník tvůj Joáb. Ale pán můj moudrý jest jako anděl Boží, věda, což se koli děje na zemi.
Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
21 A protož řekl král Joábovi: Aj, již jsem to učinil. Jdiž tedy, přiveď mládence Absolona.
Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
22 I padl Joáb na tvář svou k zemi, a pokloniv se, poděkoval králi, a řekl Joáb: Dnes jest poznal služebník tvůj, že jsem nalezl milost před očima tvýma, pane můj králi, poněvadž jest král naplnil žádost služebníka svého.
Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
23 Tedy vstav Joáb, odšel do Gessur, a přivedl Absolona do Jeruzaléma.
Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
24 I řekl král: Nechť se navrátí do domu svého, ale tváři mé ať nevidí. A tak navrátil se Absolon do domu svého, ale tváři královské neviděl.
Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
25 Nebylo pak žádného muže tak krásného jako Absolon ve všem Izraeli, aby takovou chválu měl. Od paty nohy jeho až do vrchu hlavy jeho nebylo na něm poškvrny.
Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
26 A když střihával vlasy hlavy své, (měl pak obyčej každého roku je střihati, protože jej obtěžovaly, i střihával je), tedy vážíval vlasy hlavy své, a bývalo jich dvě stě lotů váhy obecné.
Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
27 Zrodili se pak Absolonovi tři synové a jedna dcera, jejíž jméno bylo Támar, kteráž byla žena vzezření krásného.
Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
28 I byl Absolon v Jeruzalémě dvě létě, a tváři královské neviděl.
Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
29 A protož poslal Absolon k Joábovi, chtěje ho poslati k králi. Kterýžto nechtěl přijíti k němu. I poslal ještě podruhé, a nechtěl přijíti.
Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
30 Tedy řekl služebníkům svým: Shlédněte dědinu Joábovu vedlé pole mého, kdežto má ječmen; jděte a spalte jej. I zapálili služebníci Absolonovi dědinu tu.
Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
31 A vstav Joáb, přišel k Absolonovi do domu jeho, a řekl jemu: Proč jsou služebníci tvoji zapálili dědinu mou?
Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
32 Odpověděl Absolon Joábovi: Aj, poslal jsem k tobě, řka: Přiď sem, a pošli tě k králi, abys řekl jemu: I proč jsem přišel z Gessur? Lépe mi bylo ještě tam zůstati. Protož nyní nechať uzřím tvář královu. Pakliť jest na mně nepravost, nechť mne rozkáže zabiti.
Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
33 Tedy přišel Joáb k králi a oznámil to jemu. I povolal Absolona. Kterýž přišed k králi, poklonil se na tvář svou až k zemi před ním. I políbil král Absolona.
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.

< 2 Samuelova 14 >