< 2 Petrův 3 >
1 Nejmilejší, již toto druhý list vám píši, v kterýchžto listech vzbuzuji skrze napomínání vaši upřímnou mysl,
Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera.
2 Abyste pamatovali na slova předpověděná od svatých proroků, a na přikázání vydané vám od nás apoštolů Pána a Spasitele,
Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.
3 Toto nejprve vědouce, žeť přijdou v posledních dnech posměvači, podle svých vlastních žádostí chodící,
Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa.
4 A říkající: Kdež jest to zaslibování příchodu jeho? Nebo jakž otcové naši zesnuli, všecko tak trvá od počátku stvoření.
Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.”
5 Tohoť zajisté z úmysla věděti nechtí, že nebesa již dávno slovem Božím byla učiněna, i země z vody a na vodě upevněna.
Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi.
6 Pročež onen první svět vodou jsa zatopen, zahynul.
Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa.
7 Ta pak nebesa, kteráž nyní jsou, i země, týmž slovem odložena jsou a zachována k ohni, ke dni soudu a zatracení bezbožných lidí.
Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.
8 Ale tato jedna věc nebudiž před vámi skryta, nejmilejší, že jeden den u Pána jest jako tisíc let, a tisíc let jako jeden den.
Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi!
9 Nemeškáť Pán s naplněním slibů, (jakož někteří za to mají, že obmeškává, ) ale shovívá nám, nechtě, aby kteří zahynuli, ale všickni ku pokání se obrátili.
Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.
10 Přijdeť zajisté den Páně, jako zloděj v noci, v kterémžto nebesa jako v prudkosti vichru pominou, a živlové pálivostí ohně rozplynou se, země pak i ty věci, kteréž jsou na ní, vypáleny budou.
Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.
11 Poněvadž tedy to všecko má se rozplynouti, jací pak vy býti máte v svatých obcováních a v zbožnosti,
Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu
12 Očekávajíce a chvátajíce ku příští dne Božího, v němžto nebesa, hoříce, rozpustí se, a živlové pálivostí ohně rozplynou se?
pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha.
13 Nového pak nebe a nové země podle zaslíbení jeho čekáme, v kterýchžto spravedlnost přebývá.
Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.
14 Protož, nejmilejší, takových věcí čekajíce, snažtež se, abyste bez poskvrny a bez úhony před ním nalezeni byli v pokoji;
Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye.
15 A Pána našeho dlouhočekání za spasení mějte, jakož i milý bratr náš Pavel, podle sobě dané moudrosti, psal vám,
Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa.
16 Jako i ve všech epištolách svých, mluvě v nich o těch věcech. Mezi nimiž některé jsou nesnadné k vyrozumění, kterýchžto neučení a neutvrzení natahují, jako i jiných Písem, k svému vlastnímu zatracení.
Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.
17 Vy tedy, nejmilejší, to prve vědouce, střeztež se, abyste bludem těch nešlechetných lidí nebyli pojati a nevypadli od své pevnosti.
Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa.
18 Ale rozmáhejtež se v milosti a v známosti Pána našeho a Spasitele Jezukrista, jemuž sláva i nyní i na časy věčné. Amen. (aiōn )
Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )