< 2 Královská 17 >

1 Léta dvanáctého Achasa krále Judského kraloval Ozee syn Ela v Samaří nad Izraelem devět let.
Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
2 A činil to, což jest zlého před očima Hospodinovýma, ač ne tak jako jiní králové Izraelští, kteříž byli před ním.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
3 Proti němuž přitáhl Salmanazar král Assyrský. I učiněn jest Ozee služebníkem jeho, a dával mu plat.
Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
4 Shledal pak král Assyrský při Ozee puntování; nebo poslal posly k Sua králi Egyptskému, a neposílal králi Assyrskému ročního platu. Protož oblehl ho král Assyrský, a svázaného dal do žaláře.
Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
5 I táhl král Assyrský po vší zemi; přitáhl také do Samaří, a ležel u ní tři léta.
Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
6 Léta pak devátého Ozee vzal král Assyrský Samaří, a přenesl Izraele do Assyrie, a osadil je v Chelach a v Chabor při řece Gozan, a v městech Médských.
Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
7 To se stalo, proto že hřešili synové Izraelští proti Hospodinu Bohu svému, kterýž je vyvedl z země Egyptské, aby nebyli pod mocí Faraona krále Egyptského, a ctili bohy cizí,
Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
8 Chodíce v ustanoveních pohanů, (kteréž byl vyvrhl Hospodin od tváři synů Izraelských), a králů Izraelských, kteráž nařídili.
ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
9 Přesto pokrytě se měli synové Izraelští, činíce to, což není dobrého před Hospodinem Bohem svým, a vzdělali sobě výsosti ve všech městech svých, od věže strážných až do města hrazeného.
Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
10 A nastavěli sobě obrazů i hájů na všelikém pahrbku vysokém, a pod každým stromem zeleným,
Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
11 Zapalujíce tam vonné věci na všech výsostech, rovně jako pohané, kteréž vyhnal Hospodin od tváři jejich. A činili věci nejhorší, popouzejíce Hospodina.
Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
12 A sloužili bohům nečistým, o nichž byl Hospodin řekl jim, aby nečinili toho.
Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
13 I osvědčoval Hospodin proti Izraelovi a proti Judovi skrze všecky proroky i všecky vidoucí, řka: Odvraťte se od cest svých zlých, a ostříhejte přikázaní mých a ustanovení mých vedlé všeho zákona, kterýž jsem vydal otcům vašim, a kterýž jsem poslal k vám skrze služebníky své proroky.
Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
14 Však neposlechli, ale zatvrdili šíji svou, jako i otcové jejich šíje své, kteříž nevěřili v Hospodina Boha svého.
Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
15 A opovrhli ustanovení jeho i smlouvu jeho, kterouž učinil s otci jejich, i osvědčování jeho, kterýmiž se jim osvědčoval, a odešli po marnosti, a marní učiněni jsou, následujíce pohanů, kteříž byli vůkol nich, o nichž jim byl přikázal Hospodin, aby nečinili jako oni.
Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
16 A opustivše všecka přikázaní Hospodina Boha svého, udělali sobě slitinu, dvé telat a háj, a klaněli se všemu vojsku nebeskému; sloužili také Bálovi.
Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
17 A vodili syny své a dcery své skrze oheň, a obírali se s hádáním a kouzly, a tak vydali se v činění toho, což jest zlé před očima Hospodinovýma, popouzejíce ho.
Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
18 Protož rozhněval se Hospodin náramně na Izraele, a zahnal je od tváři své, nezanechav z nich nic, kromě samého pokolení Judova.
Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
19 Ano i Juda neostříhal přikázaní Hospodina Boha svého, ale chodili v ustanoveních Izraelských, kteráž byli nařídili.
Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
20 A protož opovrhl Hospodin všecko símě Izraelské a ssužoval je, a vydal je v ruku loupežníků, až je i zavrhl od tváři své.
Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
21 Nebo odtrhl Izraele od domu Davidova, a krále ustanovili Jeroboáma syna Nebatova, Jeroboám pak odvrátil Izraele od následování Hospodina, a přivedl je k hřešení hříchem velikým.
Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
22 A chodili synové Izraelští ve všech hříších Jeroboámových, kteréž on činil, a neodstoupili od nich,
Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
23 Až zavrhl Hospodin Izraele od tváři své, jakož byl mluvil skrze všecky služebníky své proroky. I vyhnán jest Izrael z země své do Assyrie až do tohoto dne.
mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
24 Potom král Assyrský přivedl lidi z Babylona, a z Kut a z Ava, a z Emat a z Sefarvaim, a osadil je v městech Samařských místo synů Izraelských, kteříž opanovavše Samaří, bydlili v městech jejich.
Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
25 I stalo se, když tam bydliti počali, a nesloužili Hospodinu, že poslal na ně Hospodin lvy, kteříž je dávili.
Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
26 Protož mluvili králi Assyrskému, řkouce: Národové ti, kteréž jsi přenesl a osadil v městech Samařských, neznají obyčeje Boha země té; protož poslal na ně lvy, kteříž je hubí, proto že neznají obyčeje Boha země té.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
27 I přikázal král Assyrský, řka: Doveďte tam jednoho z těch kněží, kteréž jste odtud přivedli, a odejdouce, nechť tam bydlí, a učí je obyčeji Boha země té.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
28 Přišel tedy jeden z kněží, kteréž byli přivedli z Samaří, a bydlil v Bethel, a učil je, jak by měli sloužiti Hospodinu.
Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
29 A však nadělali sobě jeden každý národ bohů svých, kteréž stavěli v domě výsostí, jichž byli nadělali Samařští, jeden každý národ v městech svých, v nichž bydlili.
Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
30 Muži zajisté Babylonští udělali Sukkot Benot, muži pak Kutští udělali Nergale, a muži Ematští udělali Asima.
Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
31 Hevejští tolikéž udělali Nibchaz a Tartak, a Sefarvaimští pálili syny své ohněm Adramelechovi a Anamelechovi, bohům Sefarvaimským.
Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
32 A tak sloužili Hospodinu, nadělavše sobě z počtu svého kněží výsostí, kteříž přisluhovali jim v domích výsostí.
Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
33 Hospodina ctili, však předce bohům svým sloužili vedlé obyčeje těch národů, odkudž převedeni byli.
Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
34 A do dnes činí vedlé obyčejů starých; nebojí se Hospodina, a nečiní vedlé ustanovení a úsudků jeho, ani vedlé zákona a přikázaní, kteráž vydal Hospodin synům Jákobovým, jehož nazval Izraelem.
Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
35 Učinil také byl Hospodin s nimi smlouvu, a přikázal jim, řka: Nebudete ctíti bohů cizích, ani se jim klaněti, ani jim sloužiti, ani jim obětovati.
Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
36 Ale Hospodina, kterýž vás vyvedl z země Egyptské v síle veliké a v rameni vztaženém, toho ctíti budete, a jemu se klaněti, a jemu obětovati.
Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
37 Také ustanovení a úsudků, i zákona a přikázaní, kteráž napsal vám, ostříhati budete, plníce je po všecky dny, a nebudete ctíti bohů cizích.
Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
38 Nadto na smlouvu, kterouž jsem učinil s vámi, nezapomínejte, aniž ctěte bohů cizích.
Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
39 Ale Hospodina Boha vašeho se bojte; onť vás vysvobodí z ruky všech nepřátel vašich.
Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
40 A však neposlechli, ale vedlé obyčeje svého starého činili.
Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
41 A tak ti národové ctili Hospodina, a však proto rytinám svým sloužili. Takž i synové jejich a synové synů jejich vedlé toho, což činili otcové jejich, také činí až do dnešního dne.
Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.

< 2 Královská 17 >