< 2 Královská 16 >

1 Sedmnáctého léta Pekacha syna Romeliova kraloval Achas syn Jotama, krále Judského.
Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Ve dvadcíti letech byl Achas, když kralovati počal, a šestnácte let kraloval v Jeruzalémě, ale nečinil toho, což pravého jest, před Hospodinem Bohem svým, jako David otec jeho.
Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
3 Nýbrž chodil po cestě králů Izraelských; nadto i syna svého dal provésti skrze oheň vedlé ohavností pohanských, kteréž byl Hospodin vyplénil před oblíčejem synů Izraelských.
Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
4 Obětoval také a kadil na výsostech a na pahrbcích, i pod každým stromem zeleným.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
5 Tedy vytáhl Rezin král Syrský a Pekach syn Romeliášův, král Izraelský, proti Jeruzalému k boji, a oblehli Achasa. Ale nemohli ho dobyti.
Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
6 (Toho času Rezin král Syrský odtrhl zase město Elat k Syrii, a vyplénil Židy z Elot; Syrští pak přišedše do Elat, bydlili tam až do dnešního dne.)
Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
7 I poslal Achas posly k Tiglatfalazarovi králi Assyrskému, řka: Služebník tvůj a syn tvůj jsem, přitáhni a vysvoboď mne z ruky krále Syrského, a z ruky krále Izraelského, kteříž povstali proti mně.
Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
8 A pobrav Achas stříbro a zlato, kteréž se nalézti mohlo v domě Hospodinově a v pokladích domu královského, poslal králi Assyrskému dar.
Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
9 Tedy povolil jemu král Assyrský, a přitáhl k Damašku a dobyl ho, a přenesl obyvatele jeho do Kir, Rezina pak zabil.
Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
10 I vypravil se král Achas vstříc Tiglatfalazarovi králi Assyrskému do Damašku. A uzřev král Achas oltář v Damašku, poslal k Uriášovi knězi podobenství toho oltáře, a formu jeho vedlé všelikého díla jeho.
Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
11 I vzdělal Uriáš kněz oltář vedlé všeho toho, což byl poslal král Achas z Damašku. Tak učinil kněz Uriáš, prvé než se vrátil král Achas z Damašku.
Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
12 Když se pak navrátil král z Damašku, uzřev ten oltář přistoupil k němu a obětoval na něm.
Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
13 A tak zapálil zápal svůj i suchou obět svou, a obětoval obět mokrou svou, a pokropil krví oltáře z pokojných obětí svých.
Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
14 Oltář pak měděný, kterýž byl před Hospodinem, přenesl z přední strany domu, aby nestál mezi oltářem jeho a mezi domem Hospodinovým, a postavil jej po boku oltáře svého k půlnoci.
Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
15 I přikázal král Achas knězi Uriášovi, řka: Na větším oltáři obětuj zápaly jitřní, a obět suchou večerní, a obět zápalnou královskou s obětí suchou její, i obět zápalnou všeho lidu země, a oběti suché jejich, i oběti mokré jejich, a všelikou krví zápalu a všelikou krví oběti kropiti budeš na něj, oltář pak měděný bude mi k doptávání se Boha.
Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
16 Tedy učinil Uriáš kněz všecko, jakž mu přikázal Achas.
Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
17 Osekal také král Achas přepásaní podstavků, a odjal od nich pánve, a moře složil s volů měděných, kteříž byli pod ním, a položil je na dlážení kamenné.
Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
18 Zastření také sobotní, kteréž byli udělali v domě, a vcházení královské z zevnitř odjal od domu Hospodinova, boje se krále Assyrského.
Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
19 Jiní pak skutkové krále Achasa, kteréž činil, zapsáni jsou v knize o králích Judských.
Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 I usnul Achas s otci svými, a pochován jest s nimi v městě Davidově, a kraloval Ezechiáš syn jeho místo něho.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Královská 16 >