< 2 Kronická 1 >

1 Když se pak zmocnil Šalomoun syn Davidův v království svém, a Hospodin Bůh jeho byl s ním, a zvelebil ho náramně:
Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.
2 Tedy rozkázal Šalomoun všemu Izraelovi i hejtmanům, setníkům i soudcům, i všechněm knížatům nade vším Izraelem, i přednějším v čeledech otcovských.
Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja.
3 I bral se Šalomoun a všecko to shromáždění s ním na výsost, kteráž byla v Gabaon; nebo tam byl stánek shromáždění Božího, kterýž byl udělal Mojžíš služebník Hospodinův na poušti.
Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja.
4 (Truhlu pak Boží přivezl byl David z Kariatjeharim, připraviv jí místo; nebo byl rozbil jí stan v Jeruzalémě.)
Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu.
5 A oltář měděný, kterýž byl udělal Bezeleel syn Uri, syna Hur, byl tam před stánkem Hospodinovým, kdež hledal ho Šalomoun i všecko to shromáždění.
Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko.
6 I obětoval tam Šalomoun před Hospodinem na oltáři měděném, kterýž byl před stánkem úmluvy, a obětoval na něm tisíc zápalů.
Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.
7 Té noci ukázal se Bůh Šalomounovi, a řekl jemu: Žádej, zač chceš, a dám tobě.
Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
8 I řekl Šalomoun Bohu: Ty jsi učinil otci mému Davidovi milosrdenství veliké, mne jsi též ustanovil králem místo něho.
Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake.
9 Již tedy, Hospodine Bože, budiž stálé slovo tvé mluvené s Davidem otcem mým; nebo ty jsi mne ustanovil za krále nad lidem tak mnohým, jako jest prachu zemského.
Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi.
10 Protož dej mi moudrost a umění, aťbych vycházeti mohl před lidem tímto i vcházeti. Nebo kdož by mohl souditi tento lid tvůj tak mnohý?
Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
11 Tedy odpověděl Bůh Šalomounovi: Proto že bylo to v srdci tvém, a nežádal jsi bohatství, ani zboží, ani slávy, ani bezživotí těch, jenž tebe nenávidí, aniž jsi také za dlouhý věk žádal, ale žádal jsi sobě moudrosti a umění, abys soudil lid můj, nad nímž jsem tě ustanovil za krále:
Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo,
12 Moudrost a umění dáno jest tobě, k čemužť přidám i bohatství a zboží, i slávy, tak že žádný z králů, kteříž byli před tebou, nebyl tobě rovný, aniž bude po tobě takového.
Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”
13 I navrátil se Šalomoun s výsosti, kteráž byla v Gabaon, do Jeruzaléma, od stánku úmluvy, a tak kraloval nad Izraelem.
Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.
14 Nashromáždil pak Šalomoun vozů a jezdců, a měl tisíc a čtyři sta vozů, a dvanácte tisíc jezdců, kteréž rozsadil do měst vozů, a při králi v Jeruzalémě.
Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu.
15 I složil král stříbra a zlata v Jeruzalémě jako kamení, a dříví cedrového jako planého fíkoví, kteréž roste v údolí u velikém množství.
Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
16 Přivodili také Šalomounovi koně z Egypta a koupě rozličné; nebo kupci královští brávali koupě rozličné za slušnou mzdu.
Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe.
17 A vycházejíce, vodívali spřež vozníků z Egypta za šest set lotů stříbra, koně pak za půl druhého sta. A tak všechněm králům Hetejským i králům Syrským oni dodávali.
Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.

< 2 Kronická 1 >