< 2 Kronická 20 >

1 I stalo se potom, že přitáhli synové Moáb a synové Ammon, a s nimi někteří od Ammonitských, proti Jozafatovi na vojnu.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 A přišedše, oznámili Jozafatovi, řkouce: Přitáhlo proti tobě množství veliké z zámoří, z země Syrské, a aj, jsou v Hasesontamar, jenž jest Engadi.
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 I ulekl se, a obrátil Jozafat tvář svou k hledání Hospodina, a vyhlásil půst všemu lidu Judskému.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 A tak shromáždil se lid Judský, aby hledali Hospodina. Také i ze všech měst Judských sešli se hledati Hospodina.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Tedy stál Jozafat v shromáždění Judském a Jeruzalémském, v domě Hospodinově před síní novou,
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 A řekl: Hospodine, Bože otců našich, zdaliž ty sám nejsi Bohem na nebi? Zdaliž ty nepanuješ nade všemi královstvími národů? Zdaliž v ruce tvé není síly a moci, tak že není, kdo by se mohl postaviti proti tobě?
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 Zdaliž jsi ty, Bože náš, nevyhnal obyvatelů země této před tváří lidu svého Izraelského, a dal jsi ji semeni Abrahama, milovníka svého na věky?
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Kteřížto bydlili v ní, a vzdělali tobě v ní svatyni, jménu tvému, řkouce:
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 Jestliže by na nás přišly zlé věci, meč pomsty, buď morová rána, buď hlad, postavíme se před tímto domem a před tebou, (poněvadž jméno tvé jest v domě tomto), a budeme volati k tobě v úzkostech svých, i vyslyšíš a vysvobodíš.
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 A nyní, aj, synové Ammon a Moáb, a hora Seir, skrze něž jsi nedopustil jíti Izraelovi, když se brali z země Egyptské, ale uhnuli se od nich, a nepohubili jich,
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 Aj hle, oni odplacejí se nám, přitáhše, aby nás vyhnali z dědictví tvého, kteréž jsi právem dědičným dal nám.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Bože náš, zdali jich souditi nebudeš? V násť zajisté není žádné síly proti množství tomuto velikému, kteréž táhne proti nám, aniž my víme, co bychom činiti měli, toliko na tě patří oči naše.
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Všecken také lid Judský stáli před Hospodinem, též i dítky jich, ženy i synové jejich.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 Jachaziel pak syn Zachariáše syna Benaiášova, syna Jehielova, syna Mataniášova, Levíta z synů Azafových, nadšen jsa duchem Hospodinovým, u prostřed toho shromáždění,
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Řekl: Pozorujte všecken Judo a obyvatelé Jeruzalémští, i ty králi Jozafate. Takto vám praví Hospodin: Nebojte se vy, ani se lekejte množství tohoto velikého; nebo ne váš bude boj, ale Boží.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Zítra vytáhněte proti nim, aj, oni potáhnou po stráni Ziz, a naleznete je při konci údolí naproti poušti Jeruel.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Nebudete vy bojovati tuto. Postavte se, stůjte a vizte vysvobození Hospodinovo při sobě, ó Judo a Jeruzaléme. Nebojte se, aniž se strachujte; zítra vyjděte proti nim, a Hospodin bude s vámi.
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 I sklonil se Jozafat tváří k zemi, a všecken lid Judský i obyvatelé Jeruzalémští padli před Hospodinem, klanějíce se Hospodinu.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 Vstali pak Levítové z synů Kahat a z synů Chóre, aby chválili Hospodina Boha Izraelského hlasem velikým a vysokým.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Potom vstavše ráno, vytáhli na poušť Tekoe. A když vycházeli, stál Jozafat a řekl: Slyšte mne, Judo a obyvatelé Jeruzalémští. Věřte v Hospodina Boha svého, a stane se vám věrně; věřte prorokům jeho, a šťastně se vám povede.
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 A tak poradiv se s lidem, postavil zpěváky Hospodinu, aby chválili okrasu svatosti, a když by vycházeli sšikovaní k boji, aby oni napřed šli a říkali: Oslavujte Hospodina, nebo na věky milosrdenství jeho.
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Tu chvíli pak, když oni začali zpěv a chválení, obrátil Hospodin ty, kteříž byli v zálohách, na syny Ammon, Moáb a obyvatele hory Seir, ješto však byli přitáhli proti Judovi, a tak sami se bili.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Nebo povstali synové Ammon a Moábští proti obyvatelům hory Seir, aby zmordovali a shladili je. A když dokonali boj proti obyvatelům hory Seir, pomáhali sobě a hubili jedni druhé.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Mezi tím lid Judský přitáhl k stráži, kteráž jest na poušti, a uzřeli to množství, a aj, mrtví leží na zemi, aniž kdo ušel.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Pročež přistoupil Jozafat s lidem svým, aby rozebrali loupeže jejich, a nalezli u nich hojnost zboží i klénotů na tělích zbitých. I rozbitovali toho mezi sebou, tak že unesti nemohli; za tři dni dělili ty loupeže, proto že jich mnoho bylo.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 V den pak čtvrtý shromáždili se do údolí Beracha, a že tu dobrořečili Hospodinu, protož nazvali jméno místa toho údolí Beracha až do dnešního dne.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Zatím obrátili se všickni muži Judští a Jeruzalémští, a Jozafat před nimi, aby se navrátili do Jeruzaléma s veselím; nebo byl obveselil je Hospodin nad nepřátely jejich.
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 I vešli do Jeruzaléma s loutnami a harfami a s trubami do domu Hospodinova.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Tedy připadl strach Boží na všecka království zemská, když uslyšeli, že Hospodin bojoval proti nepřátelům lidu Izraelského.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 A tak v pokoji bylo království Jozafatovo; nebo odpočinutí dal jemu Bůh jeho odevšad.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Kraloval pak Jozafat nad Judou. Ve třidcíti pěti letech byl, když kralovati začal, a pětmecítma let kraloval v Jeruzalémě. Jméno matky jeho Azuba, dcera Silchi.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 A chodil po cestě Azy otce svého, aniž se uchýlil od ní, čině to, což pravého jest před očima Hospodinovýma.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 A však výsosti nebyly zkaženy, nebo ještě lid byl nenastrojil srdce svého k Bohu otců svých.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 O jiných pak věcech Jozafatových, prvních i posledních, sepsáno jest v knihách Jéhu syna Chanani, kterémuž bylo poručeno, aby to vložil do knihy o králích Izraelských.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Potom stovaryšil se Jozafat král Judský s Ochoziášem králem Izraelským, kterýž sobě bezbožně počínal.
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 Stovaryšil se pak s ním proto, aby nadělal lodí, kteréž by přecházely přes moře. I nadělali lodí v Aziongaber.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 Protož prorokoval Eliezer syn Dodavahův z Maresa proti Jozafatovi, řka: Jakž jsi se stovaryšil s Ochoziášem, roztrhl Hospodin skutky tvé. I stroskotány jsou lodí, a tak nemohly se doplaviti přes moře.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.

< 2 Kronická 20 >