< 2 Kronická 15 >

1 Tehdy na Azariáše syna Odedova sstoupil duch Boží.
Mzimu wa Mulungu unabwera pa Azariya mwana wa Odedi.
2 Pročež vyšed vstříc Azovi, řekl jemu: Slyšte mne, Azo i všecko pokolení Judovo a Beniaminovo. Hospodin byl s vámi, dokudž jste byli s ním, a budete-li ho hledati, najdete ho; pakli ho opustíte, opustíť vás.
Iye anapita kukakumana ndi Asa ndipo anati kwa iye, “Tandimverani, inu Asa ndi Ayuda onse ndi Benjamini. Yehova ali ndi inu, inunso mukakhala naye. Ngati inu mumufunafuna Iye mudzamupeza, koma ngati mumusiya, Iye adzakusiyani.
3 Po mnohé zajisté dny Izrael jest bez pravého Boha a bez kněží, učitelů i bez zákona,
Kwa nthawi yayitali Israeli anali wopanda Mulungu weniweni, wopanda wansembe wophunzitsa ndi wopanda malamulo.
4 Ješto, kdyby se v úzkosti své k Hospodinu Bohu Izraelskému byli obrátili a hledali ho, byliť by ho nalezli.
Koma pamene anali pa mavuto anatembenukira kwa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi kufunafuna Iye, ndipo anamupeza.
5 Ale časů těchto není bezpečno vycházeti ani vcházeti; nebo nepokoj veliký jest mezi všemi obyvateli země,
Masiku amenewo sikunali kwabwino kuyenda ulendo, pakuti anthu onse okhala mʼdziko anali pa mavuto aakulu.
6 Tak že šlapá národ po národu, a město po městu, proto že Bůh kormoutí je všelijakými úzkostmi.
Mtundu umodzi umakanthidwa ndi mtundu wina ndipo mzinda wina umakanthidwa ndi mzinda wina, pakuti Mulungu amawasautsa ndi mazunzo a mtundu uliwonse.
7 Protož vy posilňte se, a neopouštějte rukou svých; nebo má mzdu práce vaše.
Koma inu, khalani amphamvu ndipo musataye mtima, pakuti mudzalandira mphotho ya ntchito yanu.”
8 A když slyšel Aza slova ta a proroctví Odeda proroka, posilil se, a vyplénil ohavnosti ze vší země Judské a Beniaminské, i z měst, kteráž byl vzal na hoře Efraim, a obnovil oltář Hospodinův, kterýž byl před síní Hospodinovou.
Asa atamva mawu awa ndiponso uneneri wa Azariya mwana wa Odedi, analimba mtima. Iye anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi mʼmizinda yonse imene analanda a ku mapiri a Efereimu. Iye anakonzetsa guwa lansembe la Yehova limene linali kutsogolo kwa khonde la Nyumba ya Mulungu.
9 Potom shromáždil všecko pokolení Judovo i Beniaminovo, a příchozí s nimi z Efraima, Manassesa a Simeona; nebo jich bylo uteklo k němu z lidu Izraelského velmi mnoho, vidouce, že Hospodin Bůh jeho jest s ním.
Kenaka anasonkhanitsa anthu onse a ku Yuda ndi Benjamini ndiponso anthu ochokera ku Efereimu, Manase ndi Simeoni amene ankakhala pakati pawo, pakuti gulu lalikulu linabwera kwa iye kuchokera ku Israeli litaona kuti anali ndi Yehova Mulungu wake.
10 I sebrali se do Jeruzaléma třetího měsíce, patnáctého léta kralování Azova,
Iwo anasonkhana mu Yerusalemu mwezi wachitatu wa chaka cha 15 cha ulamuliro wa Asa.
11 A obětovali Hospodinu v ten den z kořistí přihnaných, volů sedm set a ovcí sedm tisíc.
Pa nthawi imeneyi anapereka nsembe kwa Yehova, ngʼombe 700 ndiponso nkhosa ndi mbuzi 7,000 zochokera pa zolanda ku nkhondo zimene anabweretsa.
12 A vešli v smlouvu, aby hledali Hospodina Boha otců svých, z celého srdce svého a ze vší duše své,
Iwo anachita pangano loti azifunafuna Yehova, Mulungu wa makolo awo, ndi mtima ndi moyo wawo wonse.
13 A kdož by koli nehledal Hospodina Boha Izraelského, aby byl usmrcen, buď malý neb veliký, buď muž neb žena.
Aliyense wosafunafuna Yehova Mulungu wa Israeli aziphedwa, kaya ndi wamngʼono kapena wamkulu, mwamuna kapena mkazi.
14 I přisáhli Hospodinu hlasem velikým, s zvukem na trouby i na pozouny.
Iwo analumbira kwa Yehova, mokweza mawu, akuyimba malipenga ndi mbetete.
15 Všecken zajisté lid Judský radoval se z přísahy té; nebo celým srdcem svým přisáhli, a se vší ochotností hledali ho, a nalezli jej. I dal jim odpočinutí Hospodin se všech stran.
Anthu onse a ku Yuda anakondwera pa kulumbirako chifukwa analumbira ndi mtima wawo wonse. Iwo anafunafuna Mulungu mwachidwi, ndipo anamupeza Iye. Kotero Yehova anawapatsa mpumulo mbali zonse.
16 Nadto i Maachu matku ssadil Aza král, aby nebyla královnou, proto že byla vzdělala v háji hroznou modlu. I podťal Aza modlu tu hroznou, a zdrobil i spálil ji při potoku Cedron.
Mfumu Asa anachotsanso Maaka agogo ake pa udindo wa amayi a mfumu chifukwa anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo, naliswa ndipo kenaka anakaliwotcha ku chigwa cha Kidroni.
17 Ačkoli výsosti nebyly zkaženy v lidu Izraelském, srdce však Azovo bylo celé po všecky dny jeho.
Ngakhale kuti sanachotse malo opembedzerako mafano mu Israeli, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova, masiku onse a moyo wake.
18 Vnesl také ty věci, kteréž posvěceny byly od otce jeho, i to, čehož sám posvětil, do domu Božího, stříbro, zlato i nádoby.
Iye anabweretsanso mʼNyumba ya Mulungu zipangizo zasiliva, golide ndi ziwiya zina zimene iyeyo ndi abambo ake anazipatula.
19 A nebylo války až do léta třidcátého pátého kralování Azova.
Panalibenso nkhondo mpaka chaka cha 35 cha ufumu wa Asa.

< 2 Kronická 15 >