< 2 Kronická 14 >

1 Když pak usnul Abiáš s otci svými, a pochovali jej v městě Davidově, kraloval Aza syn jeho místo něho. Za jeho dnů v pokoji byla země deset let.
Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.
2 I činil Aza to, což se dobře líbilo Hospodinu Bohu jeho.
Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
3 Nebo zbořil oltáře cizí i výsosti, a stroskotal obrazy jejich, a posekal háje jejich.
Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera.
4 A přikázal Judovi, aby hledali Hospodina Boha otců svých, a ostříhali zákona a přikázaní jeho.
Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake.
5 Zkazil, pravím, po všech městech Judských výsosti a slunečné obrazy, a bylo v pokoji království za času jeho.
Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake.
6 Zatím vzdělal města hrazená v Judstvu, proto že v pokoji byla země, aniž jaká proti němu válka povstala těch let; nebo Hospodin dal jemu odpočinutí.
Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.
7 I řekl lidu Judskému: Vzdělejme ta města, a ohraďme je zdmi a věžemi, branami i závorami, dokudž země jest v moci naší. Aj, že jsme hledali Hospodina Boha svého, hledali jsme ho, a dal nám odpočinutí odevšad. A tak stavěli a šťastně se jim zvedlo.
Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.
8 Měl pak Aza vojsko těch, kteříž nosili štíty a kopí, z pokolení Judova třikrát sto tisíců, a z Beniaminova pavézníků a střelců dvě stě a osmdesáte tisíců. Všickni ti byli muži udatní.
Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.
9 I vytáhl proti nim Zerach Mouřenín, maje v vojště desetkrát sto tisíců, a vozů tři sta, a přitáhl až k Maresa.
Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa.
10 Vytáhl též i Aza proti němu. I sšikovali vojska v údolí Sefata u Maresa.
Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.
11 Tedy volal Aza k Hospodinu Bohu svému, a řekl: Hospodine, neníť potřebí tobě velikého množství, když ty chceš pomoci mdlejším. Pomoziž nám, Hospodine Bože náš, neboť v tebe doufáme, a ve jménu tvém jdeme proti množství tomuto. Hospodine, ty jsi Bůh náš; nechť nemá moci proti tobě bídný člověk.
Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”
12 I ranil Hospodin Mouřeníny před Azou a před lidem Judským, tak že utíkali Mouřenínové.
Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa,
13 A honil je Aza i lid, kterýž byl s ním, až do Gerar. I padli Mouřenínové, že se nijakž otaviti nemohli; nebo potříni jsou před Hospodinem a před vojskem jeho. I odnesli onino kořistí velmi mnoho.
ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo.
14 Pohubili také všecka města vůkol Gerar; strach zajisté Hospodinův připadl na ně. I vzebrali všecka města; nebo mnoho kořistí v nich bylo.
Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko.
15 Též i obyvatele v staních při dobytcích zbili, a zajavše ovec velmi mnoho a velbloudů, navrátili se do Jeruzaléma.
Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Kronická 14 >