< 1 Samuelova 27 >

1 Řekl pak David v srdci svém: Když tedyž sejdu od ruky Saulovy, nic mi lepšího není, než abych naprosto utekl do země Filistinské. I pustí o mně Saul, a nebude mne více hledati v žádných končinách Izraelských, a tak ujdu ruky jeho.
Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
2 Tedy vstav David, odebral se sám i těch šest set mužů, kteříž byli s ním, k Achisovi synu Maoch, králi Gát.
Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
3 I bydlil David s Achisem v Gát, on i muži jeho, jeden každý s čeledí svou, David i dvě ženy jeho, Achinoam Jezreelská, a Abigail Karmelská někdy žena Nábalova.
Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
4 A když bylo oznámeno Saulovi, že utekl David do Gát, přestal ho hledati více.
Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
5 Řekl pak David Achisovi: Prosím, jestliže jsem nalezl milost před očima tvýma, ať mi dají místo v některém městě krajiny této, abych tam bydlil; nebo proč má bydliti služebník tvůj s tebou v městě královském?
Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
6 I dal mu Achis v ten den Sicelech, odkudž Sicelech bylo králů Judských až do dne tohoto.
Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
7 Byl pak počet dnů, v nichž bydlil David v krajině Filistinské, den a čtyři měsíce.
Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
8 I vycházel David s muži svými, vpády činíce na Gessurské a Gerzitské a Amalechitské, (nebo ti bydlili v zemi té od starodávna), kudy se chodí přes Sur až do země Egyptské.
Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
9 A hubil David krajinu tu, nenechávaje živého muže ani ženy; bral také ovce i voly, i osly i velbloudy, i šaty, a navracoval se a přicházel k Achisovi.
Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
10 A když se ptal Achis: Kam jste dnes vpadli? odpověděl David: K straně polední Judově, a k straně polední Jerachmeelově, a k straně polední Cinejského.
Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
11 Neživil pak David ani muže ani ženy, aby koho přivoditi měl do Gát; nebo myslil: Aby na nás nežalovali, řkouce: Tak učinil David. A ten obyčej jeho byl po všecky dny, dokudž zůstával v krajině Filistinské.
Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
12 I věřil Achis Davidovi, řka: Jižtě se velice zošklivil lidu svému Izraelskému, protož budeť mi za služebníka na věky.
Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”

< 1 Samuelova 27 >