< 1 Samuelova 18 >

1 I stalo se, že když přestal mluviti k Saulovi, duše Jonatova spojila se s duší Davidovou, tak že ho zamiloval Jonata jako sebe samého.
Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha.
2 A tak Saul vzal jej k sobě toho dne, a nedopustil mu navrátiti se do domu otce jeho.
Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake.
3 I učinil Jonata s Davidem smlouvu, proto že ho miloval jako duši svou.
Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera.
4 A složiv Jonata s sebe plášť, kterýmž byl odín, dal jej Davidovi, i roucho své, až do meče svého, a až do lučiště svého, i do pasu svého.
Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.
5 Vycházel pak David, k čemuž ho koli posílal Saul, opatrně sobě počínaje. I ustanovil ho Saul nad vojáky, a líbil se všemu lidu, též i služebníkům Saulovým.
Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.
6 Stalo se pak, když se oni domů brali, a David též se navracoval od zabití Filistinského, že vyšly ženy z každého města Izraelského, zpívajíce a plésajíce, vstříc Saulovi králi s bubny, s veselím a s husličkami.
Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira.
7 A prozpěvovaly jedny po druhých ženy ty, hrajíce, a řekly: Porazilť jest Saul svůj tisíc, ale David svých deset tisíců.
Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati: “Sauli wapha 1,000, Koma Davide wapha miyandamiyanda.”
8 I rozhněval se Saul náramně, nebo nelíbila se mu ta řeč. Pročež řekl: Dali Davidovi deset tisíc, a mně dali toliko tisíc. Co mu ještě přes to přivlastní, leč království?
Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?”
9 Protož Saul zlobivě hleděl na Davida od toho dne i vždycky.
Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.
10 Stalo se pak druhého dne, že duch Boží zlý napadl Saule, a prorokoval u prostřed domu svého, a David hral rukou svou jako i jindy vždycky. Saul pak měl kopí v ruce své.
Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake.
11 I vyhodil Saul kopí, řka: Prohodím Davida až do stěny. Ale David uhnul se jemu po dvakrát.
Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.
12 A bál se Saul Davida, proto že Hospodin byl s ním, a od Saule odstoupil.
Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli.
13 Protož vybyl ho Saul od sebe, a učinil jej sobě hejtmanem nad tisíci; kterýžto vycházel i vcházel před lidem.
Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa.
14 David pak ve všech cestách svých opatrně sobě počínal, nebo Hospodin byl s ním.
Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.
15 A když to viděl Saul, že sobě velmi opatrně počíná, bál se ho.
Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri.
16 Ale všecken Izrael i Juda miloval Davida, nebo vycházel i vcházel před nimi.
Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.
17 Tedy řekl Saul Davidovi: Aj, dceru svou starší Merob dámť za manželku, toliko mi buď muž silný, a veď boje Hospodinovy. (Saul pak myslil: Nechť neschází od mé ruky, ale od ruky Filistinských.)
Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”
18 I řekl David Saulovi: Kdo jsem já, a jakýž jest rod můj a čeled otce mého v Izraeli, abych byl zetěm královým?
Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?”
19 I stalo se, že když již Merob dcera Saulova měla dána býti Davidovi, dána jest Adrielovi Molatitskému za manželku.
Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.
20 Milovala pak Míkol dcera Saulova Davida; což když oznámili Saulovi, líbilo se to jemu.
Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera.
21 (Nebo řekl Saul: Dámť mu ji, aby mu byla osídlem, a aby proti němu byla ruka Filistinských.) A tak řekl Saul Davidovi: Po této druhé budeš mi již zetěm.
Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
22 I rozkázal Saul služebníkům svým: Mluvte k Davidovi tajně, řkouce: Aj, libuje tě sobě král, a všickni služebníci jeho laskavi jsou na tebe; nyní tedy budiž zetěm královým.
Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’”
23 A když mluvili služebníci Saulovi v uši Davidovy slova ta, odpověděl David: Zdaliž se vám malá věc zdá, býti zetěm královým? A já jsem člověk chudý a opovržený.
Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”
24 Tedy služebníci Saulovi oznámili jemu, řkouce: Taková slova mluvil David.
Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide.
25 I řekl Saul: Takto rcete Davidovi: Není žádostiv král věna, toliko sto obřízek Filistinských, aby byla pomsta nad nepřátely královskými. (Saul pak to obmýšlel, aby David upadl v ruku Filistinských.)
Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.
26 Protož oznámili služebníci jeho Davidovi slova ta, a líbilo se to Davidovi, aby byl zetěm královým. Ještě se pak nebyli vyplnili dnové ti,
Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe,
27 Když vstav David, odšel, on i muži jeho, a zbil z Filistinských dvě stě mužů, jejichž obřízky přinesl David, a z úplna je dali králi, aby byl zetěm královým. I dal jemu Saul Míkol dceru svou za manželku.
Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.
28 A vida Saul, nýbrž zkušené maje, že jest Hospodin s Davidem, a že Míkol dcera jeho miluje ho,
Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide,
29 Ještě tím více Saul obával se Davida. I byl Saul nepřítelem Davidovým po všecky dny.
iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.
30 Vtrhovali pak do země knížata Filistinská; i bývalo, že kdyžkoli vycházeli, opatrněji sobě počínal David proti nim nade všecky služebníky Saulovy, pročež i jméno jeho bylo velmi slavné.
Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.

< 1 Samuelova 18 >