< 1 Královská 3 >

1 Spříznil se pak Šalomoun s Faraonem králem Egyptským, nebo pojal dceru Faraonovu a uvedl ji do města Davidova, dokudž nedostavěl domu svého, a domu Hospodinova i zdi Jeruzalémské vůkol.
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 Toliko lid obětoval na výsostech, proto že nebyl vystaven dům jménu Hospodinovu až do těch dnů.
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 Nebo miloval Šalomoun Hospodina, chodě v přikázaních Davida otce svého, a toliko na těch výsostech obětoval a kadil.
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 Protož šel král do Gabaon, aby tam obětoval; ta výsost zajisté byla největší. Tisíc obětí zápalných obětoval Šalomoun na tom oltáři.
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 Ukázal se pak Hospodin v Gabaon Šalomounovi ve snách noci té, a řekl Bůh: Žádej začkoli, a dám tobě.
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 I řekl Šalomoun: Ty jsi učinil s služebníkem svým Davidem, otcem mým, milosrdenství veliké, když chodil před tebou v pravdě a v spravedlnosti, a v upřímnosti srdce stál při tobě. Ovšem zachoval jsi jemu zvláštní toto milosrdenství, že jsi dal jemu syna, kterýž by seděl na stolici jeho, jakž se to dnes vidí.
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 Ačkoli pak nyní, ó Hospodine Bože můj, ty jsi ustanovil služebníka svého králem místo Davida otce mého, já však jsa velmi mladý, neumím vycházeti ani vcházeti.
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 Služebník, pravím, tvůj jest u prostřed lidu tvého, kterýž jsi vyvolil, lidu velikého, kterýž nemůže ani sečten ani sepsán býti pro množství.
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 Dejž tedy služebníku svému srdce rozumné, aby soudil lid tvůj, a aby rozeznal mezi dobrým a zlým; nebo kdo bude moci souditi tento lid tvůj tak mnohý?
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 I líbilo se to Hospodinu, že žádal Šalomoun za tu věc.
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 A řekl jemu Bůh: Proto že jsi žádal věci takové, a neprosils sobě za dlouhý věk, aniž jsi žádal sobě bohatství, aniž jsi žádal bezživotí nepřátel svých, ale žádal jsi sobě rozumnosti, abys slýchati uměl rozepře,
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 Aj, učinil jsem vedlé řeči tvé, aj, dalť jsem srdce moudré a rozumné, tak že rovného tobě nebylo před tebou, ani po tobě aby nepovstal rovný tobě.
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 K tomu i to, začež jsi nežádal, dal jsem tobě, totiž bohatství a slávu, tak aby nebylo rovného tobě žádného mezi králi po všecky dny tvé.
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 Přes to jestliže choditi budeš po cestách mých, ostříhaje ustanovení mých a přikázaní mých, jako chodil David otec tvůj, prodlím i dnů tvých.
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 A když procítil Šalomoun, a aj, byl sen. I přišel do Jeruzaléma a stál před truhlou smlouvy Hospodinovy, a obětoval oběti zápalné a oběti pokojné; udělal také hody všechněm služebníkům svým.
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 Tedy přišly dvě ženy hokyně k králi, a stály před ním.
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 I řekla jedna z těch žen: Prosím, pane můj, já a žena tato bydlíme v jednom domě. I porodila jsem u ní v témž domě.
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 Potom stalo se dne třetího po porodu mém, že porodila také žena tato, a byly jsme spolu. Nebylo žádného cizího s námi v domě, kromě nás dvou v témž domě.
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 Umřel pak syn ženy této v noci, nebo spěci, udávila ho.
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 A vstavši o půl noci, vzala syna mého ode mne, když spala služebnice tvá, a položila jej v lůnu svém, a syna svého mrtvého položila do lůna mého.
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 Ale když jsem vstala ráno, abych přikojila syna svého, a aj, mrtvý. Na kteréhož když jsem ráno pilněji pohleděla, a aj, nebyl syn můj, kteréhož jsem porodila.
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 I řekla žena druhá: Není tak, ale syn můj jest ten živý, a ten mrtvý jest syn tvůj. Ona pak řekla: Nikoli, ale syn tvůj jest ten mrtvý, a syn můj jest ten živý. A tak se hádaly před králem.
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 I řekl král: Tato praví: Ten živý jest syn můj, a syn tvůj jest ten mrtvý. Tato zase praví: Neníť tak, ale syn tvůj jest ten mrtvý, a syn můj jest ten živý.
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 Protož řekl král: Přineste mi meč. I přinesli meč před krále.
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 Tedy řekl král: Rozetněte to dítě živé na dvé, a dejte jednu polovici jedné, a polovici druhou druhé.
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 Ale žena, jejíž syn byl ten, kterýž živ zůstal, mluvila králi, (nebo pohnula se střeva její nad synem jejím), a řekla: Prosím, pane můj, dejte jí nemluvňátko to živé, a nikoli nezabijejte ho. Druhá pak řekla: Nechť není ani mně ani tobě, rozetněte.
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 K čemuž odpovídaje král, řekl: Dejtež této dítě to živé, a nikoli nezabijejte ho, onať jest matka jeho.
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 Tedy uslyšavše všickni Izraelští soud tento, kterýž vynesl král, báli se krále; nebo viděli, že moudrost Boží jest v srdci jeho k vykonávání soudu.
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.

< 1 Královská 3 >