< 1 Kronická 9 >

1 A tak všickni Izraelští sečteni byli, a aj, zapsáni jsou v knize králů Izraelských a Judských, a přeneseni jsou do Babylona pro přestoupení své.
Aisraeli onse analembedwa potsata mibado yawo mʼbuku la mafumu a Aisraeli. Anthu a ku Yuda anatengedwa kunka ku ukapolo ku Babuloni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.
2 Ti pak, kteříž bydlili prvé v vládařství svém v městech svých, totiž Izraelští, kněží, Levítové a Netinejští,
Tsono anthu oyamba kukhala mʼmadera awo anali Aisraeli wamba, ansembe, Alevi ndi otumikira ku Nyumba ya Yehova.
3 Bydlili v Jeruzalémě, z synů Judových, z synů Beniaminových, ano i z synů Efraimových a Manassesových:
Anthu a ku Yuda, Benjamini ndi Efereimu ndiponso Manase amene anakhala mu Yerusalemu anali awa:
4 Uttai syn Amiuda, syna Amri, syna Imri, syna Bani, z synů Fáresových, syna Judova.
Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, chidzukulu cha Perezi mwana wa Yuda.
5 A z čeledi Silonovy: Azaiáš prvorozený a synové jeho.
A banja la Siloni: Asaya mwana wake woyamba pamodzi ndi ana ake.
6 A z synů Zerachových: Jehuel, a příbuzných jejich šest set a devadesát.
A banja la Zera: Yeueli. Anthu ochokera ku Yuda analipo 690.
7 Z synů pak Beniaminových: Sallu syn Mesullama, syna Hodavia, syna Hasenuova,
A fuko la Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuya;
8 A Ibneiáš syn Jerochamův, Ela syn Uzi, syna Michri, a Mesullam syn Sefatiáše, syna Rehuelova, syna Ibniášova.
Ibineya mwana wa Yerohamu; Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri; ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli mwana wa Ibiniya.
9 Bratří také jejich po pokoleních jejich, devět set padesáte a šest; všickni ti muži knížata čeledí po domích otců svých.
Anthu ochokera ku Benjamini monga analembedwera mwa mibado yawo, analipo 956. Anthu onsewa anali atsogoleri a mabanja awo.
10 Z kněží také Jedaiáš, Jehoiarib a Jachin,
Ansembe: Yedaya, Yehoyaribu; Yakini;
11 Azariáš syn Helkiáše, syna Mesullamova, syna Sádochova, syna Meraiotova, syna Achitobova, kníže v domě Božím.
Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi, wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu;
12 A Adaiáš syn Jerochama, syna Paschurova, syna Malchiášova, a Masai syn Adiele, syna Jachzery, syna Mesullamova, syna Mesillemitova, syna Immerova.
Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya; ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yahizera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri.
13 A bratří jejich knížata po domích otců svých, tisíc sedm set a šedesát mužů udatných v práci přisluhování domu Božího.
Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu.
14 A z Levítů: Semaiáš syn Chasuba, syna Azrikamova, syna Chasabiášova, z synů Merari.
Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, wa mʼbanja la Merari;
15 A Bakbakar Cheres, a Galal, a Mataniáš syn Míchy, syna Zichri, syna Azafova.
Bakibakara, Heresi, Galali ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;
16 A Abdiáš syn Semaiáše, syna Galalova, syna Jedutunova, a Berechiáš syn Asy, syna Elkánova, kterýž přebýval ve vsech Netofatských.
Obadiya mwana wa Semaya mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, amene ankakhala ku midzi ya Anetofati.
17 Též vrátní: Sallum a Akkub, a Talmon, Achiman, i bratří jejich, z nichž byl Sallum kníže.
Alonda a pa makomo: Salumu, Akubu, Talimoni, Ahimani ndi abale awo. Mtsogoleri wawo anali Salumu.
18 Kterýž až po dnes v bráně královské stával k východu, onino pak vrátnými byli po houfích synů Léví.
Amenewa amakhala pa chipata cha mfumu kummawa mpaka lero lino. Alonda a gulu la Alevi anali awa:
19 Ale Sallum syn Chóre, syna Abiazafova, syna Chóre, a bratří jeho z domu otce jeho, Chorejští, nad pracemi přisluhování, ostříhali prahů při stánku, tak jako otcové jejich nad vojskem Hospodinovým, kteříž ostříhali vcházení.
Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, pamodzi ndi abale ake a ku banja la makolo ake, Akora aja ankanyangʼanira khomo la Tenti monga ankachitira abambo awo polondera khomo la malo okhalapo Yehova.
20 Nad kterýmiž Fínes syn Eleazarův byl někdy knížetem, a Hospodin byl s ním.
Masiku oyamba Finehasi mwana wa Eliezara anali woyangʼanira alonda apakhomo ndipo Yehova anali naye.
21 Zachariáš pak syn Meselemiášův vrátným byl u dveří stánku úmluvy.
Zekariya mwana wa Meselemiya anali mlonda woyangʼanira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
22 Všickni ti voleni za vrátné k veřejím, osob dvě stě a dvanáct. Ti ve vsech svých vyčteni jsou, kteréž nařídil David a Samuel vidoucí, pro jejich věrnost,
Onse amene anasankhidwa kukhala alonda pa khonde analipo 212. Iwo analembedwa mwa mibado yawo ku midzi yawo. Davide ndi mneneri Samueli ndiwo anawayika mʼmalo awo antchito chifukwa cha kukhulupirika kwawo.
23 Aby oni i synové jejich byli při branách domu Hospodinova, v domě stánku po strážích.
Iwo ndi zidzukulu zawo anali oyangʼanira zipata za nyumba ya Yehova imene imatchedwa Tenti.
24 Po čtyřech stranách byli vrátní, k východu, k západu, k půlnoci a ku poledni.
Alonda apakhomowa anali mbali zonse zinayi: kummawa, kumadzulo, kumpoto ndi kummwera.
25 A bratří jejich, po vsech svých bydlící, aby každého sedmého dne časy svými přicházeli s nimi.
Abale awo a ku midzi yawo amabwera nthawi ndi nthawi kudzagwira ntchito yawo kwa masiku asanu ndi awiri.
26 Nebo Levítové byli pod spravou těch čtyř předních vrátných, a byli nad komorami a nad poklady domu Božího,
Koma atsogoleri akuluakulu anayi a alonda, amene anali Alevi, anapatsidwa udindo woyangʼanira zipinda ndi chuma cha nyumba ya Mulungu.
27 A aby vůkol domu Božího ponocovali; nebo jim poručena stráž, a otvírati každý den ráno.
Iwo amakhala usiku wonse atayima mozungulira Nyumba ya Mulungu, chifukwa anayenera kuyilondera. Ndipo anali ndi kiyi wotsekulira mmawa uliwonse.
28 Z těch také ustaveni nad nádobami přisluhování; nebo v počtu vnášeli je, a v jistém počtu též vynášeli.
Ena amayangʼanira zipangizo zimene amagwiritsa ntchito pa ntchito mʼNyumba ya Mulungu. Iwo amaziwerenga zikamalowetsedwa ndi potulutsidwa.
29 Z nichž opět někteří postaveni byli nad nádobami jinými a nade všemi nádobami posvátnými, a nad bělí, vínem, olejem, kadidlem a vonnými věcmi.
Ena anapatsidwa udindo wosamalira zipangizo ndi zinthu zina zonse za ku malo opatulika, pamodzi ndi ufa, vinyo, mafuta, lubani ndi zonunkhira.
30 Někteří také synové kněžští strojili masti z těch vonných věcí.
Koma ansembe ena amasakaniza zonunkhirazo.
31 Matatiáš pak z Levítů, prvorozený Salluma Choritského, správcí byl těch věcí, kteréž se na pánvi smažily.
Mlevi wotchedwa Matitiya mwana woyamba wa Salumu wa mʼbanja la Kora, anapatsidwa udindo woyangʼanira zophikidwa mʼziwaya.
32 A z synů Kahat, z bratří jejich, byli ustanoveni nad chlebem předložení, aby jej připravovali na každou sobotu.
Abale ake ena a mʼbanja la Akohati amaphika buledi wa pa Sabata lililonse amene amayikidwa pa tebulo.
33 Z těch také byli zpěváci, přednější z čeledí otcovských mezi Levíty bydlíce, nejsouce zaměstknaní něčím jiným; nebo ve dne i v noci k své povinnosti státi musili.
Atsogoleri a mabanja a Alevi, amene anali ndi luso loyimba, amakhala mʼzipinda za Nyumba ya Mulungu ndipo samagwira ntchito zina chifukwa ankatumikira usana ndi usiku.
34 Ti jsou přední z čeledí otcovských mezi Levíty v čeledech svých, a ti přední jsouce, bydlili v Jeruzalémě.
Onsewa anali atsogoleri a mabanja a Alevi, akuluakulu monga analembedwera pa mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.
35 V Gabaon pak bydlili, otec Gabaonitských Jehiel, a jméno manželky jeho Maacha.
Yeiyeli abambo a Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni. Dzina la akazi awo linali Maaka,
36 Syn pak jeho prvorozený Abdon, Zur, Cis, Bál, Ner a Nádab.
ndipo mwana wawo woyamba kubadwa anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu,
37 Ale Gedor, Achio, Zachariáš a Miklot,
Gedori, Ahiyo, Zekariya ndi Mikiloti.
38 (Miklot pak zplodil Simam), ti také naproti bratřím svým bydlili v Jeruzalémě s bratřími svými.
Mikiloti anabereka Simeamu. Iwonso ankakhala ndi abale awo ku Yerusalemu.
39 Ner pak zplodil Cisa, a Cis zplodil Saule, Saul pak zplodil Jonatu, Melchisua, Abinadaba a Ezbále.
Neri anabereka Kisi, Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
40 Syn pak Jonatův Meribbál, a Meribbál zplodil Mícha.
Mwana wa Yonatani anali Meri-Baala, amene anabereka Mika.
41 Synové pak Míchovi: Piton, Melech, Tarea.
Ana a Mika anali: Pitoni, Meleki, Tahireya ndi Ahazi.
42 Achaz pak zplodil Járu, Jára pak zplodil Alemeta, Azmaveta a Zimri. Zimri pak zplodil Mozu.
Ahazi anabereka Yara, Yara anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimiri anabereka Moza.
43 Moza pak zplodil Bina. Refaiáš syn jeho, Elasa syn jeho, Azel syn jeho.
Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Refaya, Eleasa ndi Azeli.
44 Azel pak měl šest synů, jichžto tato jsou jména: Azrikam, Bochru, Izmael, Seariáš, Abdiáš a Chanan. Ti jsou synové Azelovi.
Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi ndipo mayina awo anali awa: Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Awa anali ana a Azeli.

< 1 Kronická 9 >