< 1 Kronická 29 >

1 Potom řekl David král všemu shromáždění: Šalomouna syna mého jediného vyvolil Bůh ještě maličkého a mladého, dílo pak toto veliké jest; nebo ne člověku palác ten, ale Hospodinu Bohu býti má.
Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu.
2 Já zajisté podlé své nejvyšší možnosti nachystal jsem potřeb k domu Boha svého, zlata k nádobám zlatým, a stříbra k stříbrným, mědi k měděným, železa k železným a dříví k dřevěným, kamení onychinového i kamení k vsazování, i karbunkulového, a rozličných barev, a všelijakého kamení drahého, i kamení mramorového hojně.
Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka.
3 Nadto z veliké lásky k domu Boha svého, maje zvláštní poklad zlata a stříbra, i ten dávám k domu Boha svého mimo všecko to, což jsem připravil k domu svatyně,
Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu:
4 Totiž tři tisíce centnéřů zlata, zlata z Ofir, a sedm tisíc centnéřů stříbra přečištěného k potažení stěn domů svatých,
Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba,
5 Zlata k nádobám zlatým a stříbra k stříbrným i ke všelikému dílu řemeslnému. A jestliže jest kdo více, ješto by co chtěl dobrovolně obětovati dnes Hospodinu?
zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”
6 Tedy knížata čeledí otcovských a knížata pokolení Izraelských, i hejtmané a setníci i úředníci nad dílem královským dobrovolně obětovali.
Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu.
7 A dali k službě domu Božího zlata pět tisíc centnéřů, a deset tisíc zlatých, stříbra pak deset tisíc centnéřů, a mědi osmnácte tisíc centnéřů, a železa sto tisíc centnéřů.
Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo.
8 Kdožkoli měli kamení drahé, dávali do pokladu domu Hospodinova do rukou Jechiele Gersunského.
Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni.
9 I veselil se lid, že tak ochotně obětovali; nebo celým srdcem dobrovolně obětovali Hospodinu. Nýbrž i král David radoval se radostí velikou.
Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.
10 A protož dobrořečil David Hospodinu před oblíčejem všeho shromáždění, a řekl David: Požehnaný jsi ty Hospodine, Bože Izraele otce našeho, od věků až na věky.
Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti, “Mutamandidwe Inu Yehova Mulungu wa kholo lathu Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya.
11 Tváť jest, ó Hospodine, velebnost i moc i sláva, i vítězství i čest, ano i všecko, což jest v nebi i v zemi. Tvé jest, ó Hospodine, království, a ty jsi vyšší nad všelikou vrchnost.
Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu, ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola. Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu. Wanu, Inu Yehova ndi ufumu; Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.
12 I bohatství i sláva od tebe jest, a ty panuješ nade vším, a v ruce tvé jest moc a síla, a v ruce tvé také jest i to, kohož chceš zvelebiti a upevniti.
Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu; Inu ndinu wolamulira zinthu zonse. Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu, kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.
13 Nyní tedy, Bože náš, děkujeme tobě, a chválíme jméno slávy tvé.
Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.
14 Nebo kdo jsem já, a co jest lid můj, abychom mohli míti moc k tak dobrovolnému obětování tobě? Od tebeť jest zajisté všecko, a i to z ruky tvé dali jsme tobě.
“Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu.
15 Nebo my příchozí jsme před tebou a hosté, jako i všickni otcové naši; dnové naši jsou jako stín běžící po zemi beze vší zástavy.
Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo.
16 Hospodine, Bože náš, všecka ta hojnost, kterouž jsme připravili k stavení domu tvého, jménu svatému tvému, z ruky tvé jest, a tvé jsou všecky věci.
Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu.
17 Známť pak, Bože můj, že ty zpytuješ srdce, a upřímnost oblibuješ; protož já z upřímnosti srdce svého ochotně obětoval jsem toto všecko. Ano i lid tvůj, kterýž se teď shledal, viděl jsem, jak s radostí chtivě obětuje tobě.
Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu.
18 Hospodine, Bože Abrahama, Izáka a Izraele, otců našich, zachovejž to na věky, totiž snažnost takovou srdce lidu svého, a nastrojuj srdce jejich sobě.
Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu.
19 Šalomounovi také synu mému dej srdce upřímé, aby ostříhal přikázaní tvých, svědectví tvých a ustanovení tvých, a aby činil všecko, a vystavěl dům ten, k němuž jsem potřeby připravil.
Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”
20 Potom řekl David všemu shromáždění: Dobrořečte nyní Hospodinu Bohu svému. I dobrořečilo všecko shromáždění Hospodinu Bohu otců svých, a přisehnuvše hlavy, poklonili se Hospodinu i králi.
Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.
21 Zatím obětovali Hospodinu oběti, obětovali také zápaly Hospodinu nazejtří, volů tisíc, skopců tisíc, beranů tisíc, s mokrými obětmi jejich, a jiných obětí množství za všecken lid Izraelský.
Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse.
22 I jedli a pili před Hospodinem v ten den s radostí velikou. Potom za krále ustanovili po druhé Šalomouna syna Davidova, a pomazali jej Hospodinu za vývodu, a Sádocha za kněze.
Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri. Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe.
23 A tak dosedl Šalomoun na stolici Hospodinovu, aby byl králem místo Davida otce svého. I vedlo se mu šťastně, a poslouchal ho všecken Izrael.
Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera.
24 Tolikéž i všecka knížata a znamenití, i všickni synové krále Davida poddali se Šalomounovi králi.
Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.
25 I zvelebil Hospodin Šalomouna náramně před očima všeho Izraele, a dal mu slávu královskou, jakéž neměl před ním žádný král v Izraeli.
Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.
26 Kraloval pak byl David syn Izai nade vším Izraelem.
Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse.
27 A dnů, v nichž kraloval David nad Izraelem, bylo čtyřidceti let. V Hebronu kraloval sedm let, a v Jeruzalémě kraloval třidceti a tři léta.
Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu.
28 I umřel v starosti dobré, pln jsa dnů, bohatství a slávy, a kraloval Šalomoun syn jeho místo něho.
Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Èinové pak Davida krále první i poslední popsáni jsou v knize Samuele proroka, a v knize Nátana proroka, též v knize Gáda proroka,
Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi,
30 Se vším kralováním i silou jeho, i se všemi příběhy časů při něm i při lidu Izraelském, i při všech královstvích zemských.
pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.

< 1 Kronická 29 >