< 1 Kronická 28 >

1 Shromáždil pak David všecka knížata Izraelská, knížata jednoho každého pokolení, a knížata houfů sloužících králi, i hejtmany a setníky, i úředníky nade vším statkem a jměním královým i synů jeho s komorníky, i se všemi vzácnými a udatnými lidmi, do Jeruzaléma.
Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
2 A povstav David král na nohy své, řekl: Slyšte mne, bratří moji a lide můj. Já jsem uložil v srdci svém vystavěti dům k odpočinutí truhle úmluvy Hospodinovy, a ku podnoži noh Boha našeho, a připravil jsem byl potřeby k stavení.
Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
3 Ale Bůh mi řekl: Nebudeš stavěti domu jménu mému, proto že jsi muž válkami zaměstknaný a krev jsi vyléval.
Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
4 Vyvolil pak Hospodin Bůh Izraelský mne ze vší čeledi otce mého, abych byl králem nad Izraelem na věky; nebo z Judy vybral vývodu a z domu Judova čeled otce mého, a z synů otce mého mne ráčil za krále ustanoviti nade vším Izraelem.
“Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
5 Tolikéž ze všech synů mých, (nebo mnoho synů dal mi Hospodin), vybral Šalomouna syna mého, aby seděl na stolici království Hospodinova nad Izraelem,
Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
6 A řekl mi: Šalomoun syn tvůj, ten mi vzdělá dům můj a síně mé; nebo jsem jej sobě zvolil za syna, a já budu jemu za otce.
Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
7 I utvrdím království jeho až na věky, bude-li stálý v ostříhání přikázaní mých a soudů mých, jako i nynějšího času.
Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
8 Nyní tedy při přítomnosti všeho Izraele, shromáždění Hospodinova, an slyší Bůh náš, napomínám vás: Zachovávejte a dotazujte se na všecka přikázaní Hospodina Boha svého, abyste vládli zemí dobrou, a v dědictví její uvedli i syny své po sobě až na věky.
“Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
9 Ty také, Šalomoune, synu můj, znej Boha otce svého, a služ jemu celým srdcem a myslí ochotnou. Nebo všecka srdce zpytuje Hospodin a všeliká mysli tanutí zná. Budeš-li ho hledati, nalezneš jej; pakli ho opustíš, zavrže tě na věky.
“Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
10 A tak viziž, že tě Hospodin zvolil, abys vystavěl dům svatyně; posilniž se a dělej.
Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
11 Dal pak David Šalomounovi synu svému formu síňce i pokojů jejích, a sklepů i paláců a komor jejích vnitřních, i domu pro slitovnici,
Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
12 A formu všeho toho, což byl složil v mysli své o síních domu Hospodinova, i o všech komorách vůkol chrámu pro poklady domu Božího, i pro poklady věcí posvátných,
Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
13 I pro houfy kněží a Levítů, a pro všecko dílo služby domu Hospodinova, a pro všecko nádobí k přisluhování v domě Hospodinově.
Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
14 Dal též zlata v jisté váze na nádobí zlaté, na všelijaké nádobí k jedné každé službě, též stříbra na všecky nádoby stříbrné v jisté váze na všelijaké nádobí k jedné každé službě,
Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
15 Totiž váhu na svícny zlaté, a lampy jejich zlaté podlé váhy jednoho každého svícnu i lamp jeho, na svícny pak stříbrné podlé váhy svícnu každého a lamp jeho, jakž potřebí bylo každému svícnu.
kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
16 Zlata též váhu na stoly předložení na jeden každý stůl, i stříbra na stoly stříbrné,
kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
17 I na vidličky a na kotlíky, i na přikryvadla zlata ryzího, a na medenice zlaté váhu na jednu každou medenici, tolikéž na medenice stříbrné jistou váhu na jednu každou medenici.
muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
18 Také na oltář k kadění zlata ryzího váhu, zlata i k udělání vozů cherubínů, kteříž by roztaženými křídly zastírali truhlu úmluvy Hospodinovy.
ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
19 Všecko to skrze vypsání z ruky Hospodinovy mne došlo, kterýž mi to dal, abych vyrozuměl všemu dílu formy té.
Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
20 A tak řekl David Šalomounovi synu svému: Posilniž se a zmocni a dělej; neboj se, ani lekej. Nebo Hospodin Bůh, Bůh můj s tebou bude, nenecháť tebe samého, aniž tě opustí, až i dokonáno bude všecko dílo služby domu Hospodinova.
Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
21 Hle, i houfové kněží a Levítů ke všeliké službě domu Božího s tebou také budou při všelikém díle, jsouce všickni ochotní a prozřetelní v moudrosti při všeliké práci, knížata také i všecken lid ke všechněm slovům tvým.
Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”

< 1 Kronická 28 >