< 1 Kronická 24 >

1 Synů pak Aronových tato jsou zpořádaní: Synové Aronovi: Nádab, Abiu, Eleazar a Itamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Ale že umřel Nádab a Abiu před otcem svým, a neměli synů, protož konali úřad kněžský Eleazar a Itamar.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Kteréž zpořádal David, totiž Sádocha z synů Eleazarových, a Achimelecha z synů Itamarových, vedlé počtu a řádu jejich v přisluhováních jejich.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Nalezeno pak synů Eleazarových více předních mužů, než synů Itamarových, a rozdělili je. Z synů Eleazarových bylo předních po domích otcovských šestnáct, a z synů Itamarových po čeledech otcovských osm.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 I rozděleni jsou losem jedni od druhých, ačkoli byli knížata nad věcmi svatými, a knížata Boží z synů Eleazarových a z synů Itamarových.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 I popsal je Semaiáš syn Natanaelův, písař z pokolení Léví před králem a knížaty, a Sádochem knězem a Achimelechem synem Abiatarovým i knížaty čeledí otcovských mezi kněžími a Levíty, tak že dům otcovský jeden zaznamenán Eleazarovi, tolikéž druhý zaznamenán Itamarovi.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Padl pak los první na Jehoiariba, na Jedaiáše druhý,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 Na Charima třetí, na Seorima čtvrtý,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 Na Malkiáše pátý, na Miamin šestý,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 Na Hakkoza sedmý, na Abiáše osmý,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 Na Jesua devátý, na Sechaniáše desátý,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 Na Eliasiba jedenáctý, na Jakima dvanáctý,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 Na Chuppa třináctý, na Jesebaba čtrnáctý,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 Na Bilgu patnáctý, na Immera šestnáctý,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 Na Chezira sedmnáctý, na Happizeza osmnáctý,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 Na Petachiáše devatenáctý, na Ezechiele dvadcátý,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 Na Jachina jedenmecítmý, na Gamule dvamecítmý,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 Na Delaiáše třímecítmý, na Maaseiáše čtyřmecítmý.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Ti jsou, jenž zřízeni byli v přisluhováních svých, aby vcházeli do domu Hospodinova podlé řádu svého, pod spravou Arona otce jejich, jakož mu byl přikázal Hospodin Bůh Izraelský.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Z synů Léví ostatních, z synů Amramových Subael, z synů Subael Jechdeiáš.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 Z Rechabiáše, z synů Rechabiášových kníže Iziáš.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Z Izara Selomot, z synů Selomotových Jachat.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 Synové pak Jeriášovi: Amariáš druhý, Jachaziel třetí, Jekamam čtvrtý.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Syn Uzielův Mícha, z synů Míchy Samir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Bratr Míchův Iziáš, a syn Iziášův Zachariáš.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Synové Merari: Moholi a Musi, synové Jaaziášovi: Beno.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Synové Merari z Jaaziáše: Beno, Soham, Zakur a Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Z Moholi Eleazar, kterýž neměl synů.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Z Cisa synové Cisovi: Jerachmeel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Synové pak Musi: Moholi, Eder a Jerimot. Ti jsou synové Levítů po domích otců svých.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 I ti také metali losy naproti bratřím svým, synům Aronovým, před Davidem králem, Sádochem a Achimelechem, i knížaty otcovských čeledí z kněží a Levítů, z čeledí otcovských, každý přednější naproti bratru svému mladšímu.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Kronická 24 >