< 1 Kronická 17 >

1 I stalo se, když bydlil David v domě svém, že řekl Nátanovi proroku: Aj, já přebývám v domě cedrovém, truhla pak smlouvy Hospodinovy jest pod kortýnami.
Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
2 I řekl Nátan Davidovi: Cožkoli jest v srdci tvém, učiň; nebo Bůh s tebou jest.
Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
3 Potom té noci stalo se slovo Boží k Nátanovi, řkoucí:
Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
4 Jdi a rci Davidovi služebníku mému: Toto dí Hospodin: Ne ty stavěti mi budeš dům k bydlení,
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
5 Poněvadž jsem nebydlil v žádném domě od toho dne, jakž jsem vyvedl syny Izraelské, až do dne tohoto, ale procházel jsem se z stánku do stánku, také i vně kromě příbytku.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
6 Nadto kudyž jsem koli chodil se vším Izraelem, zdali jsem slovo řekl kterému z soudců Izraelských, (jimž jsem přikázal, aby pásli lid můj), řka: Proč jste mi neustavěli domu cedrového?
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
7 Protož nyní toto díš služebníku mému Davidovi: Takto praví Hospodin zástupů: Já jsem tě vzal z ovčince, když jsi chodil za stádem, abys byl vývodou lidu mého Izraelského.
Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
8 A býval jsem s tebou všudy, kamž jsi koli se obrátil, všecky také nepřátely tvé vyhladil jsem před tváří tvou, a učinilť jsem jméno veliké, jako jméno vznešených na zemi.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
9 Ano i lidu svému Izraelskému způsobil jsem místo, a vštípil jej tu. I bude bydliti na místě svém, a nepohne se více, aniž na něj dotírati budou lidé nešlechetní, jako prvé,
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
10 Hned od toho času, jakž jsem ustanovil soudce nad lidem svým Izraelským, až jsem ponížil všech nepřátel tvých; nýbrž oznamujiť, že Hospodin sám vystaví tobě dům.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
11 Nebo když se vyplní dnové tvoji, abys šel za otci svými, vzbudím símě tvé po tobě, kteréž bude z synů tvých, a utvrdím království jeho.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
12 Onť mi ustaví dům, a já utvrdím trůn jeho až na věky.
Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
13 Já budu jemu otcem, a on mi bude synem, a milosrdenství svého neodejmu od něho, jako jsem je odjal od toho, kterýž byl před tebou.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
14 Ale postavím jej v domě svém a v království svém až na věky, a trůn jeho bude nepohnutelný až na věky.
Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
15 Podlé všech slov těchto, a podlé všeho vidění tohoto, tak mluvil Nátan Davidovi.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
16 Tedy všed král David, posadil se před Hospodinem, a řekl: Kdož jsem já, ó Hospodine Bože, a jaký jest dům můj, že jsi mne tak zvýšil?
Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
17 Anobrž i to jsi za málo u sebe položil, ó Bože, pročež jsi zamluvil se o domu služebníka svého i na dlouhé časy, a popatřil jsi na mne, jako na osobu člověka vzácného, Hospodine Bože.
Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
18 Což ještě více mluviti má David před tebou o zvelebení služebníka tvého? Ty zajisté znáš služebníka svého.
“Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
19 Hospodine, pro služebníka svého a podlé srdce svého činíš velikou věc tuto, abys v známost uvedl všecky převeliké věci.
Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
20 Hospodine, neníť tobě rovného, anobrž není žádného Boha kromě tebe, podlé toho všeho, jakž jsme slýchali ušima svýma.
“Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
21 Nebo kde jest který národ na zemi, jako lid tvůj Izraelský, jehož by Bůh šel, aby vykoupil sobě lid a dobyl sobě jména, čině veliké a hrozné věci, vyháněje před tváří lidu svého, kterýž jsi vykoupil z Egypta, pohany?
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
22 Zvolil jsi zajisté lid svůj Izraelský sobě za lid až na věky, a ty, Hospodine, sám jsi jejich Bohem.
Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
23 Nyní tedy, Hospodine, slovo to, jímž jsi zamluvil se služebníku svému a domu jeho, budiž jisté až na věky, a učiň tak, jakž jsi mluvil.
“Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
24 Budiž, pravím, jisté, tak aby velebeno bylo jméno tvé až na věky, a říkáno: Hospodin zástupů, Bůh Izraelský, jest Bůh nad Izraelem, a dům Davida služebníka tvého ať jest nepohnutelný před oblíčejem tvým.
kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
25 Nebo ty, Bože můj, zjevil jsi služebníku svému, že mu ustavíš dům, a protož směl služebník tvůj modliti se před tebou.
“Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
26 A tak, ó Hospodine, ty jsi sám Bůh, a mluvil jsi o služebníku svém dobré věci tyto.
Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
27 Nyní tedy ráčil jsi požehnati domu služebníka svého, aby trval na věky před oblíčejem tvým; nebo jsi ty, Hospodine, požehnal, i budeť požehnaný na věky.
Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< 1 Kronická 17 >