< 1 Kronická 16 >

1 A když přinesli truhlu Boží a postavili ji u prostřed stánku, kterýž jí byl rozbil David, tedy obětovali oběti zápalné a oběti pokojné před Bohem.
Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
2 Zatím dokonav David obětování obětí zápalných a pokojných, dal požehnání lidu ve jménu Hospodinovu.
Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
3 Rozdělil také všechněm mužům Izraelským, od muže až do ženy, jednomu každému po pecnu chleba a kusu masa, a í láhvici.
Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
4 Potom postavil před truhlou Hospodinovou služebníky z Levítů k připomínání, k vyznávání a k chválení Hospodina Boha Izraelského.
Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
5 Azaf byl přední, a druhý po něm Zachariáš, Jehiel, Semiramot, Jechiel, Mattitiáš, Eliab, Benaiáš, Obededom a Jehiel. Ti na nástrojích, na loutnách a harfách, ale Azaf na cymbálích hral.
Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
6 Benaiáš pak a Jachaziel kněží s trubami byli ustavičně před truhlou smlouvy Boží.
ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
7 Teprv toho dne ponejprvé nařídil David, aby slaven byl Hospodin zpěvem tímto od Azafa a bratří jeho:
Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
8 Slavte Hospodina, zvěstujte jméno jeho, a oznamujte mezi národy skutky jeho.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
9 Zpívejte a žalmy prozpěvujte jemu, rozmlouvejte o všech divných skutcích jeho.
Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
10 Chlubte se v svatém jménu jeho, vesel se srdce těch, jenž hledají Hospodina.
Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
11 Hledejte Hospodina i síly jeho, hledejte tváři jeho ustavičně.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
12 Rozpomínejte se na divné skutky jeho, kteréž činil, na zázraky jeho, i na soudy úst jeho.
Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
13 Ó símě Izraele, služebníka jeho, ó synové Jákobovi, vyvolení jeho,
inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
14 Onť jest Hospodin Bůh náš, na vší zemi soudové jeho.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
15 Rozpomínejte se ustavičně na smlouvu jeho, na slovo, kteréž přikázal až do tisíce pokolení,
Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
16 Kterouž učinil s Abrahamem, a na přísahu jeho Izákovi.
pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
17 A vystavil ji Jákobovi za ustanovení, Izraelovi za smlouvu věčnou,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
18 Pravě: Tobě dám zemi Kananejskou za provazec vládařství vašeho,
“Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
19 Ačkoli vás byl malý počet, a maličko byli jste v ní pohostinu.
Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
20 A přecházeli od národu do národu, a z království k jinému lidu.
iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
21 Nedopustil žádnému ublížiti jim, ano i krále pro ně trestal, řka:
Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
22 Nedotýkejte se pomazaných mých, a prorokům mým nečiňte nic zlého.
“Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
23 Zpívejte Hospodinu všecka země, zvěstujte den po dni spasení jeho.
Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
24 Vypravujte mezi pohany slávu jeho, a mezi všemi národy divy jeho.
Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
25 Nebo veliký jest Hospodin, a chvalitebný náramně, hroznější nade všecky bohy.
Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
26 Všickni zajisté bohové národů jsou modly, Hospodin pak nebesa učinil.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
27 Sláva a jasnost před ním, síla a veselé na místě jeho.
Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
28 Vzdejte Hospodinu čeledi národů, vzdejte Hospodinu slávu i moc.
Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
29 Vzdejte Hospodinu čest jména jeho, přineste dary a přiďte před oblíčej jeho, a sklánějte se před Hospodinem v okrase svatosti.
perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
30 Bojte se oblíčeje jeho všickni obyvatelé země, a budeť upevněn okršlek země, aby se nepohnul.
Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
31 Veseliti se budou nebesa, a plésati bude země, a řeknou mezi pohany: Hospodin kraluje.
Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
32 Zvuk vydá moře, i což v něm jest, veseliti se bude pole i vše, což jest na něm.
Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
33 Tedy prozpěvovati bude dříví lesní před Hospodinem, neboť se béře, aby soudil zemi.
Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
34 Oslavujte Hospodina, neb dobrý jest, nebo na věky milosrdenství jeho.
Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 A rcete: Zachovej nás, Bože spasení našeho, a shromažď nás, a vytrhni nás z pohanů, abychom slavili svaté jméno tvé, a chlubili se v chvále tvé.
Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
36 Požehnaný Hospodin Bůh Izraelský od věků a až na věky. I řekl všecken lid: Amen, i Halelujah.
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
37 I nechal tu David před truhlou smlouvy Hospodinovy Azafa a bratří jeho, aby přisluhovali před truhlou ustavičně podlé povinnosti dne každého.
Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
38 Též i Obededoma s bratřími jejich, osob šedesáte osm, Obededoma, pravím, syna Jedutunova, a Chosi, aby vrátní byli.
Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
39 Sádocha také kněze a bratří jeho za kněží nechal před příbytkem Hospodinovým na výsosti, kteráž byla v Gabaon,
Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
40 Aby obětovali zápaly Hospodinu na oltáři zápalu ustavičně, ráno i večer, podlé všeho, což psáno jest v zákoně Hospodinově, jejž vydal Izraelovi.
kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
41 A s nimi nechal Hémana a Jedutuna a jiných vybraných, kteříž vyčteni byli zejména, aby vzdávali chválu Hospodinu, proto že na věky trvá milosrdenství jeho.
Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
42 Těm také, totiž Hémanovi a Jedutunovi, nechal trub a cymbálů, aby zvučeli, i jiných nástrojů muziky Boží, syny pak Jedutunovy postavil u vrat.
Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
43 A tak rozešel se všecken lid, jeden každý do domu svého; David též navrátil se, aby požehnání dal domu svému.
Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

< 1 Kronická 16 >